< Maliro 3 >
1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
I am the man, that hath seene affliction in the rod of his indignation.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
He hath ledde mee, and brought me into darkenes, but not to light.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Surely he is turned against me: he turneth his hand against me all the day.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
My flesh and my skinne hath he caused to waxe olde, and he hath broken my bones.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
He hath builded against me, and compassed me with gall, and labour.
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
He hath set me in darke places, as they that be dead for euer.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
He hath hedged about mee, that I cannot get out: he hath made my chaines heauy.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Also when I cry and showte, hee shutteth out my prayer.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
He hath stopped vp my wayes with hewen stone, and turned away my paths.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
He was vnto me as a beare lying in waite, and as a Lion in secret places.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
He hath stopped my wayes, and pulled me in pieces: he hath made me desolate.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
He hath bent his bow and made me a marke for the arrow.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
Hee caused the arrowes of his quiuer to enter into my reines.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
I was a derision to all my people, and their song all the day.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
He hath filled me with bitternes, and made me drunken with wormewood.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
He hath also broken my teeth with stones, and hath couered me with ashes.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
Thus my soule was farre off from peace: I forgate prosperitie,
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
And I saide, My strength and mine hope is perished from the Lord,
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
Remembring mine affliction, and my mourning, the wormewood and the gall.
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
My soule hath them in remembrance, and is humbled in me.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
I consider this in mine heart: therefore haue I hope.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
It is the Lordes mercies that wee are not consumed, because his compassions faile not.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
They are renued euery morning: great is thy faithfulnesse.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
The Lord is my portion, sayth my soule: therefore wil I hope in him.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
The Lord is good vnto them, that trust in him, and to the soule that seeketh him.
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
It is good both to trust, and to waite for the saluation of the Lord.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
It is good for a man that he beare the yoke in his youth.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
He sitteth alone, and keepeth silence, because he hath borne it vpon him.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
He putteth his mouth in the dust, if there may be hope.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Hee giueth his cheeke to him that smiteth him: he is filled full with reproches.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
For the Lord will not forsake for euer.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
But though he sende affliction, yet will he haue compassion according to the multitude of his mercies.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
For he doeth not punish willingly, nor afflict the children of men,
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
In stamping vnder his feete all the prisoners of the earth,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
In ouerthrowing the right of a man before the face of the most high,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
In subuerting a man in his cause: the Lord seeth it not.
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Who is he then that sayth, and it commeth to passe, and the Lord commandeth it not?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Out of the mouth of the most high proceedeth not euill and good?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Wherefore then is the liuing man sorowfull? man suffreth for his sinne.
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Let vs search and try our wayes, and turne againe to the Lord.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Let vs lift vp our hearts with our handes vnto God in the heauens.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
We haue sinned, and haue rebelled, therefore thou hast not spared.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
Thou hast couered vs with wrath, and persecuted vs: thou hast slaine and not spared.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Thou hast couered thy selfe with a cloude, that our prayer should not passe through.
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
Thou hast made vs as the ofscouring and refuse in the middes of the people.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
All our enemies haue opened their mouth against vs.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Feare, and a snare is come vpon vs with desolation and destruction.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Mine eye casteth out riuers of water, for the destruction of the daughter of my people.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Mine eye droppeth without stay and ceaseth not,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
Till the Lord looke downe, and beholde from heauen.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Mine eye breaketh mine heart because of all the daughters of my citie.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Mine enemies chased me sore like a birde, without cause.
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
They haue shut vp my life in the dungeon, and cast a stone vpon me.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Waters flowed ouer mine head, then thought I, I am destroyed.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
I called vpon thy Name, O Lord, out of the lowe dungeon.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Thou hast heard my voyce: stoppe not thine eare from my sigh and from my cry.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Thou drewest neere in the day that I called vpon thee: thou saydest, Feare not.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
O Lord, thou hast maintained the cause of my soule, and hast redeemed my life.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
O Lord, thou hast seene my wrong, iudge thou my cause.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Thou hast seene all their vengeance, and all their deuises against me.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
Thou hast heard their reproch, O Lord, and all their imaginations against me:
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
The lippes also of those that rose against me, and their whispering against me continually.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Behold, their sitting downe and their rising vp, how I am their song.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Giue them a recompence, O Lord, according to the worke of their handes.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
Giue them sorow of heart, euen thy curse to them.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Persecute with wrath and destroy them from vnder the heauen, O Lord.