< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
ALEPH. I am the man that sees poverty, through the rod of his wrath upon me.
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
He has taken me, and led me away into darkness, and not [into] light.
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
Nay, against me has he turned his hand all the day.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
He has made old my flesh and my skin; he has broken my bones.
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
BETH. He has built against me, and compassed my head, and brought travail [upon me].
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
He has set me in dark places, as them that have long been dead.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
He has builded against me, and I cannot come forth: he has made my brazen [chain] heavy.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
GIMEL. Yea, [though] I cry and shout, he shuts out my prayer.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
DALETH. He has built up my ways, he has hedged my paths;
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
he has troubled me, [as] a she-bear lying in wait: he is to me [as] a lion in secret places.
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
He pursued [me] after I departed, and brought me to a stand: he has utterly ruined me.
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
HE. He has bent his bow, and set me as a mark for the arrow.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
He has caused the arrows of his quiver to enter into my reins.
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
I became a laughing-stock to all my people; and their song all the day.
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
VAU. He has filled me with bitterness, he has drenched me with gall.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
And he has dashed out my teeth with gravel, he has fed me with ashes.
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
He has also removed my soul from peace: I forgot prosperity.
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
Therefore my success has perished, and my hope from the Lord.
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
ZAIN. I remembered by reason of my poverty, and because of persecution my bitterness and gall shall be remembered;
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
and my soul shall meditate with me.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
This will I lay up in my heart, therefore I will endure.
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
HETH. [It is] the mercies of the Lord, that he has not failed me, because his compassions are not exhausted. Pity [us], O Lord, early [every] month: for we are not brought to an end, because his compassions are not exhausted.
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
[They are] new every morning: great is thy faithfulness.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
The Lord is my portion, says my soul; therefore will I wait for him.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
TETH. The Lord is good to them that wait for him: the soul which shall seek him
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
[is] good, and shall wait for, and quietly expect salvation of the Lord.
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
TETH. [It is] good for a man when he bears a yoke in his youth.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
He will sit alone, and be silent, because he has borne [it] upon him.
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
JOD. He will give [his] cheek to him that smites him: he will be filled full with reproaches.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
For the Lord will not reject for ever.
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
CHAPH. For he that has brought down will pity, and [that] according to the abundance of his mercy.
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
He has not answered [in anger] from his heart, though he has brought low the children of a man.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
LAMED. To bring down under his feet all the prisoners of the earth,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
to turn aside the judgment of a man before the face of the Most High,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
to condemn a man [unjustly] in his judgment, the Lord has not given commandment.
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Who has thus spoken, and it has come to pass? the Lord has not commanded it.
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Out of the mouth of the Most High there shall not come forth evil and good.
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
MEM. Why should a living man complain, a man concerning his sin?
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
NUN. Our way has been searched out and examined, and we will turn to the Lord.
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
Let us lift up our hearts with [our] hand to the lofty One in heaven.
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
We have sinned, we have transgressed; and thou hast not pardoned.
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
SAMECH. Thou has visited [us] in wrath, and driven us away: thou has slain, thou has not pitied.
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
Thou hast veiled thyself with a cloud because of prayer, that I might be blind,
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
and be cast off. AIN. Thou hast set us [alone] in the midst of the nations.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
All our enemies have opened their mouth against us.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Fear and wrath are come upon us, suspense and destruction.
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Mine eye shall pour down torrents of water, for the destruction of the daughter of my people.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
PHE. Mine eye is drowned [with tears], and I will not be silent, so that there shall be no rest,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
until the Lord look down, and behold from heaven.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Mine eye shall prey upon my soul, because of all the daughters of the city.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
TSADE. The fowlers chased me as a sparrow, all mine enemies destroyed my life in a pit without cause,
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
and laid a stone upon me.
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Water flowed over my head: I said, I am cut off.
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
KOPH. I called upon thy name, O Lord, out of the lowest dungeon.
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
Thou heardest my voice: close not thine ears to my supplication.
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Thou drewest nigh to my help: in the day wherein I called upon thee thou saidst to me, Fear not.
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
RECHS. O Lord, thou has pleaded the causes of my soul; thou has redeemed my life.
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
Thou hast seen, O Lord, my troubles: thou hast judged my cause.
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Thou hast seen all their vengeance, [thou hast looked] on all their devices against me.
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
CHSEN. Thou hast heard their reproach [and] all their devices against me;
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
the lips of them that rose up against me, and their plots against me all the day;
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
their sitting down and their rising up: look thou upon their eyes.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Thou wilt render them a recompense, O Lord, according to the works of their hands.
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
THAU. Thou wilt give them [as] a covering, the grief of my heart.
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
Thou wilt persecute them in anger, and wilt consume them from under the heaven, O Lord.

< Maliro 3 >