< Maliro 3 >

1 Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
Jeg er den, der så nød ved hans vredes ris,
2 Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
mig har han ført og ledt i det tykkeste Mulm,
3 zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
ja, Hånden vender han mod mig Dagen lang.
4 Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
Mit Bød og min Hud har han opslidt, brudt mine Ben,
5 Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
han mured mig inde, omgav mig med Galde og Møje,
6 Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
lod mig bo i Mørke som de, der for længst er døde.
7 Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
Han har spærret mig inde og lagt mig i tunge Lænker.
8 Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
Om jeg end råber og skriger, min Bøn er stængt ude.
9 Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
Han spærred mine Veje med Kvader, gjorde Stierne kroge.
10 Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
Han blev mig en lurende Bjørn, en Løve i Baghold;
11 Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
han ledte mig vild, rev mig sønder og lagde mig øde;
12 Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
han spændte sin Bue; lod mig være Skive for Pilen.
13 Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
Han sendte sit Koggers Sønner i Nyrerne på mig;
14 Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
hvert Folk lo mig ud og smæded mig Dagen lang,
15 Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
med bittert mætted han mig, gav mig Malurt at drikke.
16 Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
Mine Tænder lod han bide i Flint, han trådte mig i Støvet;
17 Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
han skilte min Sjæl fra Freden, jeg glemte Lykken
18 Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
og sagde: "Min Livskraft, mit Håb til HERREN er ude."
19 Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
At mindes min Vånde og Flakken er Malurt og Galde;
20 Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
min Sjæl, den mindes det grant den grubler betynget.
21 Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
Det lægger jeg mig på Sinde, derfor vil jeg håbe:
22 Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
HERRENs Miskundhed er ikke til Ende, ikke brugt op,
23 Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
hans Nåde er ny hver Morgen, hans Trofasthed stor.
24 Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
Min Del er HERREN, (siger min Sjæl, ) derfor håber jeg på ham.
25 Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
Dem, der bier på HERREN, er han god, den Sjæl, der ham søger;
26 nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
det er godt at håbe i Stilhed på HERRENs Frelse,
27 Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
godt for en Mand, at han bærer Åg i sin Ungdom.
28 Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
Han sidde ensom og tavs, når han lægger det på ham;
29 Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
han trykke sin Mund mod Støvet, måske er der Håb.
30 Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
Række Kind til den, der slår ham, mættes med Hån.
31 Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
Thi Herren bortstøder ikke for evigt,
32 Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
har han voldt Kvide, så ynkes han, stor er hans Nåde;
33 Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
ej af Hjertet plager og piner han Menneskens Børn.
34 Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
Når Landets Fanger til Hobe trædes under Fod,
35 kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
når Mandens Ret for den Højestes Åsyn bøjes,
36 kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
når en Mand lider Uret i sin Sag mon Herren ej ser det?
37 Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
Hvo taler vel, så det sker, om ej Herren byder?
38 Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
Kommer ikke både ondt og godt fra den Højestes Mund?
39 Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
Over hvad skal den levende sukke? Hver over sin Synd!
40 Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
Lad os ransage, granske vore Veje og vende os til HERREN,
41 Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
løfte Hænder og Hjerte til Gud i Himlen;
42 “Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
vi syndede og stod imod, du tilgav ikke,
43 “Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
men hylled dig i Vrede, forfulgte os, dræbte uden Skånsel,
44 Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
hylled dig i Skyer, så Bønnen ej nåed frem;
45 Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
til Skarn og til Udskud har du gjort os midt iblandt Folkene.
46 “Adani anthu atitsekulira pakamwa.
De opspærred Munden imod os, alle vore Fjender.
47 Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
Vor Lod blev Gru og Grav og Sammenbruds Øde;
48 Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
Vandstrømme græder mit Øje, mit Folk brød sammen.
49 Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
Hvileløst strømmer mit Øje, det kender ej Ro,
50 mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
før HERREN skuer ned fra Himlen, før han ser til.
51 Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
Synet af Byens Døtre piner min Sjæl.
52 Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
Jeg joges som en Fugl af Fjender, hvis Had var grundløst,
53 Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
de spærred mig inde i en Grube, de stenede mig;
54 madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
Vand strømmed over mit Hoved, jeg tænkte: "Fortabt!"
55 Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
Dit Navn påkaldte jeg, HERRE, fra Grubens Dyb;
56 Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
du hørte min Røst: "O, gør dig ej døv for mit Skrig!"
57 Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
Nær var du den Dag jeg kaldte, du sagde: "Frygt ikke!"
58 Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
Du førte min Sag, o Herre, genløste mit Liv;
59 Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
HERRE, du ser, jeg lider Uret. skaf mig min Ret!
60 Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
Al deres Hævnlyst ser du, alle deres Rænker,
61 Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
du hører deres Smædeord HERRE, deres Rænker imod mig,
62 manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
mine Fjenders Tale og Tanker imod mig bestandig.
63 Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
Se dem, når de sidder eller står, deres Nidvise er jeg.
64 Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
Dem vil du gengælde, HERRE, deres Hænders Gerning,
65 Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
gør deres Hjerte forhærdet din Forbandelse over dem!
66 Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.
forfølg dem i Vrede, udryd dem under din Himmel.

< Maliro 3 >