< Maliro 2 >

1 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
Aleph. Hou hath the Lord hilid the douyter of Sion with derknesse in his strong veniaunce? he hath caste doun fro heuene in to erthe the noble citee of Israel; and bithouyte not on the stool of hise feet, in the dai of his strong veniaunce.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
Beth. The Lord castide doun, and sparide not alle the faire thingis of Jacob; he distried in his strong veniaunce the strengthis of the virgyn of Juda, and castide doun in to erthe; he defoulide the rewme, and the princes therof.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
Gymel. He brak in the ire of his strong veniaunce al the horn of Israel; he turnede a bak his riyt hond fro the face of the enemy; and he kyndlide in Jacob, as fier of flawme deuowrynge in cumpas.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
Deleth. He as an enemye bente his bouwe, he as an aduersarie made stidfast his riyt hond; and he killide al thing that was fair in siyt in the tabernacle of the douytir of Sion; he schedde out his indignacioun as fier.
5 Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
He. The Lord is maad as an enemy; he castide doun Israel, he castide doun alle the wallis therof; he destriede the strengthis therof, and fillide in the douyter of Juda a man maad low, and a womman maad low.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
Vau. And he scateride his tent as a gardyn, he distried his tabernacle; the Lord yaf to foryetyng in Sion a feeste dai, and sabat; and the kyng and prest in to schenschipe, and in to the indignacioun of his strong veniaunce.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
Zai. The Lord puttide awei his auter, he curside his halewyng; he bitook in to the hondis of enemy the wallis of the touris therof; thei yauen vois in the hous of the Lord, as in a solempne dai.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
Heth. The Lord thouyte to distrie the wal of the douyter of Sion; he stretchide forth his coorde, and turnede not awei his hond fro perdicioun; the forwal, ether the outerward, mourenyde, and the wal was distried togidere.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
Teth. The yatis therof ben piyt in the erthe, he loste and al to-brak the barris therof; the kyng therof and the princes therof among hethene men; the lawe is not, and the profetis therof founden not of the Lord a visioun.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
Joth. Thei saten in erthe, the elde men of the douytir of Sion weren stille; thei bispreynten her heedis with aische, the eldere men of Juda ben girt with hairis; the virgyns of Juda castiden doun to erthe her heedis.
11 Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
Caph. Myn iyen failiden for teeris, myn entrails weren disturblid; my mawe was sched out in erthe on the sorewe of the douyter of my puple; whanne a litil child and soukynge failide in the stretis of the citee.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
Lameth. Thei seiden to her modris, Where is wheete, and wyn? whanne thei failiden as woundid men in the stretis of the citee; whanne thei senten out her soulis in the bosum of her modris.
13 Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
Men. To whom schal Y comparisoun thee? ether to whom schal Y licne thee, thou douyter of Jerusalem? to whom schal Y make thee euene, and schal Y coumforte thee, thou virgyn, the douyter of Sion? for whi thi sorewe is greet as the see; who schal do medicyn to thee?
14 Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
Nun. Thi profetis sien to thee false thingis, and fonned; and openyden not thi wickidnesse, that thei schulden stire thee to penaunce; but thei sien to thee false takyngis, and castyngis out.
15 Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
Sameth. Alle men passynge on the weie flappiden with hondis on thee; thei hissiden, and mouyden her heed on the douyter of Jerusalem; and seiden, This is the citee of perfit fairnesse, the ioie of al erthe.
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
Ayn. Alle thin enemyes openyden her mouth on thee; thei hissiden, and gnaistiden with her teeth, and seiden, We schulen deuoure; lo! this is the dai which we abididen, we founden, we sien.
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
Phe. The Lord dide tho thingis whiche he thouyte, he fillide hise word which he hadde comaundid fro elde daies; he distriede, and sparide not; and made glad the enemy on thee, and enhaunside the horn of thin enemyes.
18 Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
Sade. The herte of hem criede to the Lord, on the wallis of the douyter of Syon; leede thou forth teeris as a stronde, bi dai and niyt; yyue thou not reste to thee, nether the appil of thin iye be stille.
19 Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
Coph. Rise thou togidere, herie thou in the nyyt, in the begynnyng of wakyngis; schede out thin herte as watir, bifore the siyt of the Lord; reise thin hondis to hym for the soulis of thi litle children, that failiden for hungur in the heed of alle meetyngis of weies.
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
Res. Se thou, Lord, and byholde, whom thou hast maad so bare; therfor whether wymmen schulen ete her fruyt, litle children at the mesure of an hond? for a prest and profete is slayn in the seyntuarie of the Lord.
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
Syn. A child and an elde man laien on the erthe withoutforth; my virgyns and my yonge men fellen doun bi swerd; thou hast slayn hem in the dai of thi strong veniaunce, thou smotist `and didist no merci.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
Thau. Thou clepidist, as to a solempne dai, hem that maden me aferd of cumpas; and noon was that ascapide in the dai of the strong veniaunce of the Lord, and was left; myn enemy wastide hem, whiche Y fedde, and nurschide up.

< Maliro 2 >