< Maliro 2 >

1 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
How hath the Lord in his anger covered with a cloud the daughter of Zion! He hath cast down from heaven to earth the glory of Israel, And hath not remembered his footstool in the day of his anger.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
Lord hath swallowed up without pity all the habitations of Jacob; He hath thrown down in his wrath the strongholds of the daughter of Judah; He hath brought down to the ground, he hath profaned the kingdom and its princes.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
He hath cut off, in his fierce anger, every horn of Israel; He hath drawn back his right hand from the face of the enemy, And hath burned against Jacob like a flaming fire, which devoureth round about.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
He bent his bow like an enemy; He stood with his right hand as an adversary, and slew all that was pleasant to the eye; Upon the tent of the daughter of Zion he poured out his fury like fire.
5 Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
The Lord is become as an enemy; he hath swallowed up Israel; He hath swallowed up all his palaces; he hath destroyed his strongholds; And hath multiplied in the daughter of Judah mourning and lamentation.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
He hath violently torn away his hedge, like the hedge of a garden; he hath destroyed his place of congregation; Jehovah hath caused the solemn feast and the sabbath to be forgotten in Zion; He hath despised, in his fierce anger, the king and the priest.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
The Lord hath cast off his altar; he hath abhorred his holy place; He hath given up into the hands of the enemy the walls of Zion's palaces; They have lifted up the voice in the house of Jehovah, as in the day of a solemn feast.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
Jehovah hath purposed to destroy the wall of the daughter of Zion; He hath stretched out the line, he hath not withdrawn his hand from destroying; He hath made the rampart and the wall to lament; They languish together.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
Her gates are sunk into the earth; he hath destroyed and broken her bars; Her king and her princes are among the nations; The law is no more; Her prophets also find no vision from Jehovah.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
The elders of the daughter of Zion sit upon the ground in silence; They have cast dust upon their heads; they have girded themselves with sackcloth; The virgins of Jerusalem hang down their heads to the ground.
11 Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
Mine eyes do fail with tears; my bowels boil; My liver is poured out upon the ground on account of the destruction of the daughter of my people; For the children and sucklings faint in the streets of the city.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
They say to their mothers, “Where is corn and wine?” While they faint, as one wounded, in the streets of the city; While their life is poured out into their mother's bosom.
13 Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
How shall I address thee? what shall I liken to thee, O daughter of Jerusalem? With what shall I compare thee, so as to comfort thee, O virgin daughter of Zion? Surely thy breach is wide, like the sea; who can heal thee?
14 Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
Thy prophets declare to thee that which is vain and false; They lay not open to thee thine iniquity, to bring back thy captivity; They pronounce to thee prophecies of falsehood and seduction.
15 Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
All that that pass by clap their hands at thee; They hiss, and shake their heads at the daughter of Jerusalem. “Is this the city that men called the perfection of beauty, The joy of the whole earth?”
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
All thine enemies open their mouths against thee; They hiss and gnash the teeth; They say: “We have swallowed her up; Yea, this is the day that we looked for; we have found, we have seen it.”
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
Jehovah hath accomplished that which he had devised; He hath fulfilled his word, which he had commanded in the days of old; He hath thrown down and hath not pitied; He hath caused thine enemy to rejoice over thee; he hath exalted the horn of thine adversaries.
18 Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
Their heart crieth out to the Lord. O wall of the daughter of Zion, let thy tears run down like a river day and night! Give thyself no rest! let not the apple of thine eye cease!
19 Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
Arise, cry aloud in the night at the beginning of the watches! Pour out thy heart like water before the face of Jehovah! Lift up thy hands to him for the life of thy young children, That faint for hunger at the head of all the streets!
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
“Behold, O Jehovah, and consider! With whom hast thou dealt thus? Shall women eat the fruit of the womb, children borne in the arms? Shall the priest and the prophet be slain in the holy place of the Lord?
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
“The boy and the old man lie on the ground in the streets; My virgins and my young men are fallen by the sword; Thou hast slain them in the day of thine anger; Thou hast killed, and hast shown no mercy.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
“Thou hast called, as on a festal day, my terrors around me; There was not one, in the day of Jehovah's anger, that escaped or was left; Those whom I have borne in my arms and brought up hath my enemy consumed.”

< Maliro 2 >