< Maliro 2 >

1 Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
How the LORD covered the daughter of Zion with a cloud in his anger. He has cast down from heaven to the earth the splendor of Israel, and hasn't remembered his footstool in the day of his anger.
2 Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
The LORD has swallowed up all the habitations of Jacob, and has not pitied. He has thrown down in his wrath the strongholds of the daughter of Judah. He has brought them down to the ground; he has humiliated the kingdom and its rulers.
3 Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
He has cut off in fierce anger all the strength of Israel. He has drawn back his right hand before the enemy. He has blazed in Jacob like a flaming fire, which devours all around.
4 Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
He has bent his bow like an enemy; his right hand he has positioned like an adversary. He killed all that were pleasant to the eye. In the tent of the daughter of Zion he has poured out his wrath like fire.
5 Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
The LORD has become as an enemy; he has swallowed up Israel; he has swallowed up all her palaces and has destroyed its strongholds. He has multiplied in the daughter of Judah mourning and lamentation.
6 Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
He has done violence to his temple, as if it were a vineyard; he has destroyed his place of assembly. The LORD has caused solemn assembly and Sabbath to be forgotten in Zion, and he has spurned in his fierce anger king and priest and prince.
7 Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
The LORD has rejected his altar, he has disowned his sanctuary, and has given up into the hand of the enemy the walls of her palaces. They have made a shout in the house of the LORD, as in the day of a solemn assembly.
8 Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
The LORD has determined to destroy the wall of the daughter of Zion. He has stretched out the line, he has not withdrawn his hand from destroying. He has made the rampart and wall to lament; they languish together.
9 Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
Her gates are sunk into the ground; he has destroyed and broken her bars. Her king and her princes are among the nations where the law is no more, and her prophets find no vision from the LORD.
10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
The elders of the daughter of Zion sit on the ground in silence. They have cast up dust on their heads; they have clothed themselves with sackcloth. The virgins of Jerusalem hang down their heads to the ground.
11 Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
My eyes are worn out from weeping, my stomach is churning. My heart is poured on the earth, because of the destruction of the daughter of my people, because the young children and the infants faint in the streets of the city.
12 Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
They tell their mothers, "Where is grain and wine?" When they faint as the wounded in the streets of the city, as their lives fade away in their mothers' bosom.
13 Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
What shall I testify of you? What shall I liken to you, daughter of Jerusalem? What shall I compare to you, that I may comfort you, virgin daughter of Zion? For your ruin is great like the sea. Who can heal you?
14 Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
Your prophets have seen for you false and deceptive visions. They have not uncovered your iniquity, to bring back your captivity, but have seen for you false and misleading oracles.
15 Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
All that pass by clap their hands at you, they hiss and wag their head at the daughter of Jerusalem, saying, "Is this the city that men called 'The perfection of beauty,' 'The joy of the whole earth'?"
16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
All your enemies have opened wide their mouth against you. They hiss and gnash the teeth; they say, "We have swallowed her up. Certainly this is the day that we looked for; we have found, we have seen it."
17 Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
The LORD has done that which he purposed, he has fulfilled his word that he commanded in the days of old. He has thrown down, and has not pitied. He has caused the enemy to gloat over you and exalted the horn of your adversaries.
18 Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
Their heart cried to the LORD. O wall of the daughter of Zion, let tears run down like a river day and night. Give yourself no respite; do not let your tears cease.
19 Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
Arise, cry out in the night, at the beginning of the watches. Pour out your heart like water before the face of the LORD. Lift up your hands toward him for the life of your young children, that faint for hunger at the head of every street.
20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
Look, LORD, and see to whom you have done like this. Shall the women eat their fruit, the children that are dandled in the hands? Shall the priest and the prophet be killed in the sanctuary of the LORD?
21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
The youth and the old man lie on the ground in the streets; my virgins and my young men have fallen by the sword. You have killed them in the day of your anger; you have slaughtered, without pity.
22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.
You have called, as in the day of a solemn assembly, my terrors on every side. There was none that escaped or remained in the day of the LORD's anger. Those that I have borne and brought up has my enemy destroyed.

< Maliro 2 >