< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
Après la mort de Josué, les enfants d’Israël consultèrent Yahweh, en disant: « Qui de nous montera le premier contre les Chananéens pour les combattre? »
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
Yahweh répondit: « Juda montera; voici que j’ai livré le pays entre ses mains. »
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
Et Juda dit à Siméon, son frère: « Monte avec moi dans le pays que le sort m’a assigné, et nous combattrons les Chananéens; j’irai aussi avec toi dans le pays que le sort t’a assigné. » Et Siméon alla avec lui.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Juda monta, et Yahweh livra entre leurs mains les Chananéens et les Phérézéens; ils battirent dix mille hommes à Bézec.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
Ayant trouvé à Bézec Adoni-Bésec, ils l’attaquèrent et ils battirent les Chananéens et les Phérézéens.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
Adoni-Bésec prit la fuite, mais ils le poursuivirent et, l’ayant saisi, ils lui coupèrent les pouces des mains et des pieds.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
Adoni-Bésec dit: « Soixante-dix rois, ayant les pouces des pieds et des mains coupés, ramassaient les miettes sous ma table; ce que j’ai fait, Dieu me le rend. » On l’emmena à Jérusalem, et il y mourut.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Les fils de Juda attaquèrent Jérusalem et, l’ayant prise, ils la frappèrent du tranchant de l’épée et mirent le feu à la ville.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Ensuite les fils de Juda descendirent pour combattre les Chananéens qui habitaient la montagne, le Négéb et la Séphéla.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Juda marcha contre les Chananéens qui habitaient à Hébron, appelée autrefois Cariath-Arbé, et il battit Sésaï, Ahiman et Tholmaï.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
Il marcha de là contre les habitants de Dabir, qui s’appelait autrefois Cariath-Sépher.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
Caleb dit: « A celui qui frappera Cariath-Sépher et qui la prendra, je donnerai pour femme ma fille Axa. »
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
Othoniel, fils de Cénez, frère cadet de Caleb, s’en empara, et Caleb lui donna sa fille Axa pour femme.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
Lorsqu’elle alla chez Othoniel, elle l’excita à demander à son père un champ. Elle descendit de son âne, et Caleb lui dit: « Qu’as-tu? »
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
Elle lui répondit: « Fais-moi une faveur, car tu m’as établie dans un pays desséché; donne-moi des sources d’eau. » Et Caleb lui donna les sources supérieures et les sources inférieures.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
Les fils du Cinéen, beau-frère de Moïse, montèrent de la ville des palmiers, avec les fils de Juda, dans le désert de Juda, au midi d’Arad, et ils vinrent s’établir avec le peuple.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Juda se mit en marche avec Siméon, son frère, et ils battirent les Chananéens qui habitaient Séphaath; ils dévouèrent la ville par anathème, et on l’appela Horma.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Juda s’empara aussi de Gaza et de son territoire, d’Ascalon et de son territoire, d’Accaron et de son territoire.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
Yahweh fut avec Juda; et Juda prit possession de la montagne, mais il ne put chasser les habitants de la plaine, parce qu’ils avaient des chars de fer.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
On donna Hébron à Caleb, comme l’avait dit Moïse, et il en chassa les trois fils d’Enac.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
Les fils de Benjamin ne chassèrent pas les Jébuséens qui habitaient Jérusalem, et les Jébuséens ont habité à Jérusalem avec les fils de Benjamin, jusqu’à ce jour.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
La maison de Joseph, elle aussi, monta contre Béthel, et Yahweh fut avec eux.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
La maison de Joseph fit faire une reconnaissance à Béthel, ville dont le nom était autrefois Luz.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
Les gardes, ayant aperçu un homme qui sortait de la ville, ils lui dirent: « Montre-nous par où on peut entrer dans la ville, et nous te ferons grâce. »
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
Il leur montra par où ils pourraient entrer dans la ville, et ils frappèrent la ville du tranchant de l’épée, mais ils laissèrent aller cet homme avec toute sa famille.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
Cet homme se rendit dans le pays des Hittites; il bâtit une ville et la nomma Luz, et c’est son nom jusqu’à ce jour.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Manassé ne chassa pas les habitants de Bethsan et des villes de sa dépendance, ni ceux de Thanac et des villes de sa dépendance, ni les habitants de Dor et des villes de sa dépendance, ni les habitants de Jéblaam et des villes de sa dépendance, ni les habitants de Mageddo et des villes de sa dépendance; et les Chananéens s’enhardirent à rester dans ce pays.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
Lorsqu’Israël fut devenu assez fort, il assujettit les Chananéens à un tribut, et ne les chassa point.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Ephraïm ne chassa pas les Chananéens qui habitaient à Gaser, et les Chananéens habitèrent au milieu d’Ephraïm, à Gaser.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zabulon ne chassa pas les habitants de Cétron, ni les habitants de Naalol; et les Chananéens habitèrent au milieu de Zabulon, mais ils furent soumis à un tribut.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Aser ne chassa pas les habitants d’Accho, ni les habitants de Sidon, ni ceux d’Ahalab, d’Achazib, d’Helba, d’Aphec et de Rohob;
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
et les fils d’Aser demeurèrent au milieu des Chananéens, habitants du pays, car ils ne les chassèrent point.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Nephthali ne chassa pas les habitants de Beth-Samès, ni les habitants de Beth-Anath, et il demeura au milieu des Chananéens, habitants du pays; mais les habitants de Beth-Samès et de Beth-Anath furent soumis à un tribut en sa faveur.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
Les Amorrhéens refoulèrent dans la montagne les fils de Dan, et ne les laissèrent pas descendre dans la plaine.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
Les Amorrhéens s’enhardirent à rester à Har-Harés, à Ajalon et à Salebim; mais la main de la maison de Joseph s’appesantit sur eux, et ils furent soumis à un tribut.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
Le territoire des Amorrhéens s’étendait de la montée d’Acrabbim, de Séla, et au-dessus.

< Oweruza 1 >