< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
and to be after death Joshua and to ask son: descendant/people Israel in/on/with LORD to/for to say who? to ascend: rise to/for us to(wards) [the] Canaanite in/on/with beginning to/for to fight in/on/with him
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
and to say LORD Judah to ascend: rise behold to give: give [obj] [the] land: country/planet in/on/with hand: power his
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
and to say Judah to/for Simeon brother: male-sibling his to ascend: rise with me in/on/with allotted my and to fight in/on/with Canaanite and to go: went also I with you in/on/with allotted your and to go: went with him Simeon
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
and to ascend: rise Judah and to give: give LORD [obj] [the] Canaanite and [the] Perizzite in/on/with hand: power their and to smite them in/on/with Bezek ten thousand man
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
and to find [obj] Adoni-bezek Adoni-bezek in/on/with Bezek and to fight in/on/with him and to smite [obj] [the] Canaanite and [obj] [the] Perizzite
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
and to flee Adoni-bezek Adoni-bezek and to pursue after him and to grasp [obj] him and to cut [obj] thumb/big toe hand his and foot his
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
and to say Adoni-bezek Adoni-bezek seventy king thumb/big toe hand their and foot their to cut to be to gather underneath: under table my like/as as which to make: do so to complete to/for me God and to come (in): bring him Jerusalem and to die there
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
and to fight son: descendant/people Judah in/on/with Jerusalem and to capture [obj] her and to smite her to/for lip: edge sword and [obj] [the] city to send: burn in/on/with fire
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
and after to go down son: descendant/people Judah to/for to fight in/on/with Canaanite to dwell [the] mountain: hill country and [the] Negeb and [the] Shephelah
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
and to go: went Judah to(wards) [the] Canaanite [the] to dwell in/on/with Hebron and name Hebron to/for face: before Kiriath-arba Kiriath-arba and to smite [obj] Sheshai and [obj] Ahiman and [obj] Talmai
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
and to go: went from there to(wards) to dwell Debir and name Debir to/for face: before Kiriath-sannah Kiriath-sannah
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
and to say Caleb which to smite [obj] Kiriath-sannah Kiriath-sannah and to capture her and to give: give(marriage) to/for him [obj] Achsah daughter my to/for woman: wife
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
and to capture her Othniel son: child Kenaz brother: male-sibling Caleb [the] small: young from him and to give: give(marriage) to/for him [obj] Achsah daughter his to/for woman: wife
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
and to be in/on/with to come (in): come she and to incite him to/for to ask from with father her [the] land: country and to descend from upon [the] donkey and to say to/for her Caleb what? to/for you
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
and to say to/for him to give [emph?] to/for me blessing for land: country/planet [the] Negeb to give: put me and to give: give to/for me bowl water and to give: give to/for her Caleb [obj] bowl upper and [obj] bowl lower
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
and son: descendant/people Kenite relative Moses to ascend: rise from Ir-hatmarim [the] Ir-hatmarim with son: descendant/people Judah wilderness Judah which in/on/with Negeb Arad and to go: went and to dwell with [the] people
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
and to go: went Judah with Simeon brother: male-sibling his and to smite [obj] [the] Canaanite to dwell Zephath and to devote/destroy [obj] her and to call: call by [obj] name [the] city Hormah
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
and to capture Judah [obj] Gaza and [obj] border: area her and [obj] Ashkelon and [obj] border: area her and [obj] Ekron and [obj] border: area her
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
and to be LORD (with *L(abh)*) Judah and to possess: take [obj] [the] mountain: hill country for not to/for to possess: take [obj] to dwell [the] valley for chariot iron to/for them
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
and to give: give to/for Caleb [obj] Hebron like/as as which to speak: speak Moses and to possess: take from there [obj] three son: descendant/people [the] Anak
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
and [obj] [the] Jebusite to dwell Jerusalem not to possess: take son: descendant/people Benjamin and to dwell [the] Jebusite with son: descendant/people Benjamin in/on/with Jerusalem till [the] day: today [the] this
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
and to ascend: rise house: household Joseph also they(masc.) Bethel Bethel and LORD with them
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
and to spy house: household Joseph in/on/with Bethel Bethel and name [the] city to/for face: before Luz
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
and to see: see [the] to keep: look at man to come out: come from [the] city and to say to/for him to see: see us please [obj] entrance [the] city and to make: do with you kindness
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
and to see: see them [obj] entrance [the] city and to smite [obj] [the] city to/for lip: edge sword and [obj] [the] man and [obj] all family his to send: let go
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
and to go: went [the] man land: country/planet [the] Hittite and to build city and to call: call by name her Luz he/she/it name her till [the] day: today [the] this
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
and not to possess: take Manasseh [obj] Beth-shean Beth-shean and [obj] daughter: village her and [obj] Taanach and [obj] daughter: village her and [obj] (to dwell *Q(K)*) Dor and [obj] daughter: village her and [obj] to dwell Ibleam and [obj] daughter: village her and [obj] to dwell Megiddo and [obj] daughter: village her and be willing [the] Canaanite to/for to dwell in/on/with land: country/planet [the] this
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
and to be for to strengthen: strengthen Israel and to set: put [obj] [the] Canaanite to/for taskworker and to possess: take not to possess: take him
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
and Ephraim not to possess: take [obj] [the] Canaanite [the] to dwell in/on/with Gezer and to dwell [the] Canaanite in/on/with entrails: among his in/on/with Gezer
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zebulun not to possess: take [obj] to dwell Kitron and [obj] to dwell Nahalol and to dwell [the] Canaanite in/on/with entrails: among his and to be to/for taskworker
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Asher not to possess: take [obj] to dwell Acco and [obj] to dwell Sidon and [obj] Ahlab and [obj] Achzib and [obj] Helbah and [obj] Aphek and [obj] Rehob
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
and to dwell [the] Asherite in/on/with entrails: among [the] Canaanite to dwell [the] land: country/planet for not to possess: take him
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Naphtali not to possess: take [obj] to dwell Beth-shemesh Beth-shemesh and [obj] to dwell Beth-anath Beth-anath and to dwell in/on/with entrails: among [the] Canaanite to dwell [the] land: country/planet and to dwell Beth-shemesh Beth-shemesh and Beth-anath Beth-anath to be to/for them to/for taskworker
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
and to oppress [the] Amorite [obj] son: descendant/people Dan [the] mountain: hill country [to] for not to give: allow him to/for to go down to/for valley
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
and be willing [the] Amorite to/for to dwell in/on/with mountain: mount (Mount) Heres in/on/with Aijalon and in/on/with Shaalbim and to honor: heavy hand: power house: household Joseph and to be to/for taskworker
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
and border: boundary [the] Amorite from ascent Akrabbim from [the] Sela and above [to]

< Oweruza 1 >