< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
And it came to pass after the death of Joshua that the children of Israel asked Jehovah, saying, Which of us shall go up against the Canaanites first, to fight against them?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
And Jehovah said, Judah shall go up: behold, I have delivered the land into his hand.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
And Judah said to Simeon his brother, Come up with me into my lot, and let us fight against the Canaanites, and I likewise will go with thee into thy lot; and Simeon went with him.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
And Judah went up; and Jehovah delivered the Canaanites and the Perizzites into their hand, and they smote them in Bezek, ten thousand men.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
And they found Adoni-Bezek in Bezek, and fought against him, and they smote the Canaanites and the Perizzites.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
And Adoni-Bezek fled, and they pursued after him, and caught him, and cut off his thumbs and his great toes.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
And Adoni-Bezek said, Seventy kings, with their thumbs and their great toes cut off, gleaned under my table: as I have done, so God has requited me. And they brought him to Jerusalem, and there he died.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
And the children of Judah fought against Jerusalem, and took it, and smote it with the edge of the sword, and set the city on fire.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
And afterwards the children of Judah went down to fight against the Canaanites, that dwelt in the hill-country, and in the south, and in the lowland.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
And Judah went against the Canaanites that dwelt in Hebron — the name of Hebron before was Kirjath-Arba; and they slew Sheshai and Ahiman and Talmai.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
And from there he went against the inhabitants of Debir; now the name of Debir before was Kirjath-sepher.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
And Caleb said, He that smites Kirjath-sepher and takes it, to him will I give Achsah my daughter as wife.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
And Othniel the son of Kenaz, Caleb's younger brother, took it; and he gave him Achsah his daughter as wife.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
And it came to pass as she came, that she urged him to ask of her father the field; and she sprang down from the ass. And Caleb said to her, What wouldest thou?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
And she said to him, Give me a blessing; for thou hast given me a southern land; give me also springs of water. And Caleb gave her the upper springs and the lower springs.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
And the children of the Kenite, Moses' father-in-law, had gone up out of the city of palm-trees with the children of Judah into the wilderness of Judah, which is in the south of Arad; and they went and dwelt with the people.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
And Judah went with Simeon his brother, and they slew the Canaanites that inhabited Zephath, and utterly destroyed it; and they called the name of the city Hormah.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
And Judah took Gazah and its border, and Ashkelon and its border, and Ekron and its border.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
And Jehovah was with Judah; and he took possession of the hill-country, for he did not dispossess the inhabitants of the valley, because they had chariots of iron.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
And they gave to Caleb Hebron, as Moses had said; and he dispossessed from thence the three sons of Anak.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
And the children of Benjamin did not dispossess the Jebusites, the inhabitants of Jerusalem; but the Jebusites dwell with the children of Benjamin in Jerusalem to this day.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
And the house of Joseph, they also went up against Bethel; and Jehovah was with them.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
And the house of Joseph sent to search out Bethel; now the name of the city before was Luz.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
And the guards saw a man come forth out of the city, and said unto him, Shew us, we pray thee, how [we] may enter into the city, and we will shew thee kindness.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
And he shewed them how to enter into the city. And they smote the city with the edge of the sword; but they let go the man and all his family.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
And the man went into the land of the Hittites, and built a city, and called its name Luz, which is its name to this day.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
And Manasseh did not dispossess Beth-shean and its dependent villages, nor Taanach and its dependent villages, nor the inhabitants of Dor and its dependent villages, nor the inhabitants of Ibleam and its dependent villages, nor the inhabitants of Megiddo and its dependent villages; and the Canaanites would dwell in that land.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
And it came to pass when Israel became strong, that they made the Canaanites tributary; but they did not utterly dispossess them.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
And Ephraim did not dispossess the Canaanites that dwelt in Gezer; but the Canaanites dwelt among them in Gezer.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Zebulun did not dispossess the inhabitants of Kitron, nor the inhabitants of Nahalol; but the Canaanites dwelt among them, and became tributaries.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Asher did not dispossess the inhabitants of Accho, nor the inhabitants of Zidon, nor Ahlab, nor Achzib, nor Helbah, nor Aphik, nor Rehob;
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
and the Asherites dwelt among the Canaanites, the inhabitants of the land; for they did not dispossess them.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Naphtali did not dispossess the inhabitants of Beth-shemesh, nor the inhabitants of Beth-anath; and he dwelt among the Canaanites, the inhabitants of the land, but the inhabitants of Beth-shemesh and of Beth-anath became tributaries to them.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
And the Amorites forced the children of Dan into the hill-country, for they would not suffer them to come down to the valley.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
And the Amorites would dwell on mount Heres, in Ajalon and in Shaalbim; but the hand of the house of Joseph prevailed, and they became tributaries.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
And the border of the Amorites was from the ascent of Akrabbim, from the rock, and upwards.

< Oweruza 1 >