< Oweruza 1 >

1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
Joshua a dueknah hnukah Israel ca rhoek loh BOEIPA te a dawt uh tih, “Ulae kaimih ham Kanaan taengla aka cet vetih a moecuek kah bangla anih te a vathoh thil lah ve,” a ti uh.
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
Te dongah BOEIPA loh, “Judah te cet saeh lamtah khohmuen he a kut ah ka paek tangtae coeng ni ke,” a ti nah.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
Te vaengah a manuca Simeon te, “Kai hmulung khuila kamah taengla ha luei lamtah Kanaan ke vathoh thil sih. Kai khaw nang hmulung kah khuikah nang taengah ka pongpa van eh,” a ti nah tih Simeon khaw anih taengla cet.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Judah a luei vaengah BOEIPA loh amih kut ah Kanaan neh Perizzi te a tloeng pah tih Bezek ah hlang thawng rha a tloek uh.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
Bezek ah Adonibezek te a hmuh uh tih anih te a tloek uh phoeiah Kanaan neh Perizzi te a tloek uh.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
Adonibezek te rhaelrham van dae a hnukah a hloem uh tih a kae uh vaengah a kut a kho kah kutnu khonu te a tlueh pauh.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
Te vaengah Adonibezek loh, “Manghai sawmrhih kut kho kah kutnu khonu ka tlueh pah tih ka caboei hmuikah cakdik aka rhut la om uh. Ka saii bangla Pathen loh kai taengah han thuung coeng,” a ti. Anih te Jerusalem la a khuen uh tih te ah te duek.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
Judah ca rhoek loh Jerusalem te a vathoh thil uh tih a buem uh. cunghang ha neh a ngawn phoeiah khopuei te hmai ah a pup uh.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Te phoeiah tlang neh tuithim kolrhawk kah aka om Kanaan te tloek ham Judah ca rhoek loh suntla uh.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Te phoeiah Hebron ah aka om Kanaan te khaw Judah loh a paan bal. Hebron kah a ming rhuem tah Kiriatharba ni. Te vaengah Sheshai, Ahiman neh Talmai te khaw a tloek uh.
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
Te lamloh Debir kah khosa rhoek te a paan uh cetuh. Derbir kah a ming rhuem tah Kiriathsepher ni.
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
Te vaengah Kaleb loh, “Kiriathsepher aka tloek tih aka buem te tah ka canu Akcah te a yuu la ka paek ni,” a ti.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
Te dongah Kaleb mana Kenaz capa Othniel loh a buem tih a canu Akcah te a yuu la a paek.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
A yuu te ha pawk vaengah a napa taengkah khohmuen bih ham a va te a vueh. laak dong lamkah a bit uh vanneh anih te Kaleb loh, “Nang ham balae kan saii eh,” a ti nah.
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
Te dongah a canu loh, “Kai ham khaw yoethennah nan suem vanbangla tuithim khohmuen ke kai m'pae mai lamtah tuidueh tui khaw kai ham nam paek mai mako,” a ti nah. Te dongah anih te Kaleb loh a siip tuidueh neh a hnawt tuidueh te a paek.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
Rhophoe khopuei lamkah Moses masae Keni ca rhoek neh Arad tuithim Judah khosoek Judah ca rhoek tah luei uh tih pilnam taengah kho a sak uh.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Te phoeiah Judah te a mana Simeon neh cet rhoi tih Zephath khosa rhoek Kanaan te a tloek rhoi. Khopuei te a thup tih khopuei ming khaw Hormah la a sak pah.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Te vaengah Judah loh Gaza neh a khorhi, Ashkelon neh a khorhi, Ekron neh a khorhi te a loh.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
Te vaengah BOEIPA loh Judah a om puei tih tlang khaw a huul coeng dae kol kah khosa rhoek tah thi leng a khueh dongah haek thai pawh.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
Moses kah a thui bangla Hebron te Kaleb taengah a paek uh hatah te lamkah Anak ca rhoek pathum te vik a vai.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
Jerusalem kah khosa Jebusi te tah Benjamin ca rhoek loh ana haek pawt dongah tihnin due Jerusalem kah Benjamin ca rhoek taengah Jebusi loh kho a sak.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
Joseph imko loh Bethel a paan uh vaengah khaw amih te BOEIPA loh a om puei.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
Lamhma a ming Luz khopuei la aka om Bethel te Joseph imko loh a yaam uh.
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
Te vaengah kho khui lamkah aka lo hlang pakhat te longyam rhoek loh a hmuh uh tih, “Khopuei khuirhai te kaimih n'tueng dae, nang taengah sitlohnah ka saii uh van bitni,” a ti nah.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
Te dongah amih te khopuei vongrhai a tueng tih khopuei te cunghang ha neh a tloek uh. Tedae hlang pakhat neh a imkhui pum te tah a loeih sakuh.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
Te dongah hlang pakhat te Khitti kho la cet tih kho a thoong. Tekah kho ming te Luz la ana khue dongah tihnin due anih ming la om.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Bethshan neh a khobuel rhoek, Taanakh neh a khobuel rhoek, Dore kah aka om, aka om neh a khobuel rhoek, Ibleam kah aka om rhoek neh a khobuel rhoek, Megiddo kah aka om rhoek neh a khobuel rhoek tah Manasseh loh ana haek pawt dongah Kanaan rhoek loh khohmuen ah khosak ham khak huul uh.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
Israel a om vaengah a moem tih Kanaan te saldong la a khueh tih a haek rhoe a haek moenih.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Gezer ah aka om Kanaan te khaw Ephraim loh ana haek pawt dongah Gezer kah Kanaan tah amih lakli ah kho a sak.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Kitron kah khosa rhoek neh Nahalal kah khosa rhoek te khaw Zebulun loh ana haek pawt dongah a lakli ah Kanaan loh kho a sak tih saldong la om uh.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Akkho kah khosa rhoek, Sidon kah khosa rhoek neh Ahlab, Akhzib, Helbah, Aphek, Rehoh te khaw Asher loh ana haek pawh.
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
Amih te ana haek pawt dongah khohmuen kah aka om Kanaan lakli ah Asher long khaw kho a sak.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Bethshemesh kah khosa rhoek neh Bethanath khosa rhoek te Naphtali loh ana haek pawt dongah khohmuen kah aka om Kanaan lakli ah kho a sak. Tedae Bethshemesh neh Bethanath kah aka om rhoek te tah amih ham saldong la om uh.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
Tlang kah Dan ca rhoek te Amori loh la a nen dongah anih te tah kol la suntlak sak ham pae pawh.
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
Amori khaw Heres tlang, Aijalon neh Shaalbim ah khosak ham huul uh ngawn dae Joseph imko kah a bong a ban a puel phoeiah tah amih te saldong la om uh.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
Amori khorhi he Akrabbim kham lamloh Sela voelh a poeng duela om.

< Oweruza 1 >