< Oweruza 1 >
1 Atamwalira Yoswa Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Ndani mwa ife ayambe nkhondo yomenyana ndi Akanaani?”
Подир смъртта на Исуса, израилтяните се допитаха до Господа, казвайки: Кой пръв ще възлезе за нас против ханаанците да воюва против тях?
2 Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe kupita. Ndawapatsa dzikolo mʼmanja mwawo.”
И Господ каза: Юда ще възлезе, ето, предадох земята в ръката му.
3 Choncho Ayuda anawuza abale awo a fuko la Simeoni kuti, “Bwerani tipitire limodzi mʼdziko limene tapatsidwa kuti tikamenyane ndi Akanaani. Ifenso tidzapita nanu mʼdziko limene anakugawirani.” Ndipo Asimeoni anapita nawo.
Тогава Юда каза на брата си Симеона: Възлез с мене в моя предел, за да воюваме против ханаанците, и аз ще отида с тебе в твоя предел. И Симеон отиде с него.
4 Choncho Ayuda ananyamuka, ndipo Yehova anapereka Akanaani ndi Aperezi mʼmanja mwawo. Ndipo anapha anthu 10,000 ku Bezeki.
Юда, прочее възлезе; и Господ предаде ханаанците и ферезейците в ръката им; и те поразиха от тях в Везек десет хиляди мъже.
5 Ku Bezekiko anakumana ndi ankhondo a mfumu Adoni-Bezeki ndipo anamenyana nawo, ndipo Ayudawo anagonjetsa Akanaani ndi Aperezi.
И намериха Адонивезека във Везек, воюваха против него и поразиха ханаанците и ферезейците.
6 Adoni-Bezekiyo anathawa, koma anamuthamangira ndi kumupeza, namugwira. Atamugwira anamudula zala zake zazikulu za ku manja ndi miyendo.
А Адонивезек побягна; но те го погнаха и хванаха го, и отсякоха палците на ръцете му и на нозете му.
7 Tsono Adoni-Bezeki anati, “Mafumu 70 omwe anadulidwa zala zazikulu za ku manja ndi miyendo yawo ankatola nyenyeswa pansi pa tebulo langa. Mulungu tsopano wandibwezera zomwe ndinawachita.” Kenaka anapita naye ku Yerusalemu ndipo anafera komweko.
И рече Адонивезек: Седемдесет царе с отсечени палци на ръцете и на нозете си са събирали трохи под трапезата ми; както съм аз правил, така ми въздаде Бог. И доведоха го в Ерусалим, гдето и умря.
8 Pambuyo pake Ayuda anakathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu ndipo anawulanda. Anapha anthu ambiri ndi kutentha mzinda wonse.
И юдейците воюваха против Ерусалим, и, като го завлякоха, поразиха го с острото на ножа и предадоха града на огън.
9 Kenaka Ayuda anapita kukamenyana ndi Akanaani omwe amakhala ku dziko la ku mapiri, dziko la Negevi kummwera ndiponso mu zigwa.
Подир това, юдейците слязоха, за да воюват против ханаанците, които живееха в хълмистата, и в южната и в полската страни.
10 Anakalimbananso ndi Akanaani amene ankakhala ku Hebroni (mzinda womwe kale unkatchedwa Kiriyati-Araba). Kumeneko anagonjetsa Sesai, Ahimani ndi Talimai.
Юда отиде и против ханаанците, които живееха в Хеврон (а по-напред името на Хеврон беше Кириат-арва), и убиха Сесая, Ахимана и Талмая;
11 Kuchokera kumeneko, iwo anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi).
и от там отиде против жителите на Девир (а по-напред името на Девир беше Кириат-сефер).
12 Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.”
И рече Халев: Който порази Кириат-сефер и го превземе, нему ще дам дъщеря си Аса за жена.
13 Otanieli mwana wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.
И превзе го Готониил, син на Кенеза, по-малкия брат на Халева; и той му даде дъщеря си Ахса за жена.
14 Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani?”
И като отиваше тя му внуши щото да поиска от баща й нива; и тъй, като слезе от осела, Халев й рече: Що ти е?
15 Iye anayankha kuti, “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.
А тя му рече: Дай ми благословение; понеже си ми дал южна страна, дай ми и водни извори. И Халев й даде гоните извори и долните извори.
16 Tsono zidzukulu za Hobabu, Mkeni uja, mpongozi wa Mose, zinachoka ku Yeriko mzinda wa migwalangwa pamodzi ndi anthu a fuko la Yuda mpaka ku chipululu chimene chili kummwera kwa Aradi ndi kukakhala ndi Aamaleki.
И потомците на кенееца, Моисевия тъст, отидоха от Града на палмите, заедно с юдейците, в Юдовата пустиня, която е на юг от Арад; и отидоха та се заселиха между людете.
17 Kenaka anthu a fuko la Yuda anapita pamodzi ndi abale awo a fuko la Simeoni ndi kukagonjetsa Akanaani amene amakhala ku Zefati, ndipo mzindawo anawuwononga kwambiri. Choncho mzindawo anawutcha Horima.
Тогава Юда отиде с братята си Симеона, та поразиха ханаанците, които живееха в Сефат; и обрекоха града на изтребление; и градът се нарече Орма.
18 Anthu a fuko la Yuda analandanso mzinda wa Gaza ndi dziko lonse lozungulira, mzinda wa Asikeloni pamodzi ndi dziko lake lonse lozungulira, ndi mzinda wa Ekroni pamodzi ndi dziko lonse lozungulira.
Юда завладя и Газа с околностите му, Аскалон с околностите му и Акарон с околностите му.
19 Yehova anathandiza anthu a fuko la Yuda. Iwo analanda dziko la kumapiri, koma sanathe kuwachotsa anthu ku zigwa, chifukwa anali ndi magaleta azitsulo.
Господ беше с Юда; и той изгони жителите на хълмистата страна, обаче, не изгони жителите и на долината, защото имаха железни колесници.
20 Monga analonjezera Mose, Kalebe anapatsidwa Hebroni. Kalebe anapirikitsa mafuko atatu a Anaki mu mzindamo.
И дадоха Хеврон на Халева, според както Моисей беше казал; и той изгони от там тримата Енакови синове.
21 Koma fuko la Benjamini linalephera kuwachotsa Ayebusi, amene amakhala mu Yerusalemu. Choncho Ayebusiwo akukhalabe ndi fuko la Benjamini mu Yerusalemu mpaka lero.
А вениаминците не изгониха евусейците, които населяваха Ерусалим но евусейците живееха в Ерусалим заедно с вениаминците, както живеят и до днес.
22 A banja la Yosefe nawonso anathira nkhondo mzinda wa Beteli, ndipo Yehova anali nawo.
Също и Иосифовият дом, и те отидоха против Ветил; и Господ беше с тях.
23 Anatumiza anthu kuti akazonde Beteli. Mzindawo kale unkatchedwa Luzi.
И Иосифовият дом прати да съгледат Ветил (а по-напред името на града беше Луз).
24 Anthu okazondawo anaona munthu akutuluka mu mzindamo ndipo anamuwuza kuti, “Tisonyeze njira yolowera mu mzindamu, ndipo ife tidzakuchitira chifundo.”
И съгледателите видяха един човек, който излизаше из града, и рекоха му: Покажи ни, молим, входа на града, и ще ти покажем милост.
25 Choncho iye anawaonetsa njirayo, ndipo iwo anapha anthu onse mu mzindamo ndi lupanga koma munthu uja pamodzi ndi banja lake sanawaphe.
И той им показа входа на града, и те поразиха града с острото на ножа, а човека оставиха да излезе с цялото си семейство.
26 Ndipo iye anapita ku dziko la Ahiti, kumene anamangako mzinda nawutcha dzina lake Luzi. Mpaka lero lino mzindawo dzina lake ndi lomwelo.
И човекът отиде в Хетейската земя, гдето и съгради град и нарече го Луз, както е името му и до днес.
27 Koma a fuko la Manase sanachotse nzika za mzinda wa Beti-Seani pamodzi ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena nzika za mzinda wa Taanaki ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapenanso nzika za mzinda wa Dori ndi mʼmidzi yake yozungulira. Iwo sanapirikitse nzika za mzinda wa Ibuleamu ndi mʼmidzi yake yozungulira, kapena mzinda wa Megido ndi mʼmidzi yake yozungulira. Choncho Akanaani anapitirirabe kukhala mʼdzikomo.
Манасия не изгони жителите на Ветсан и селата му, нито на Таанах и селата му, нито жителите на Дор и селата му, нито жителите на Ивреам и селата му, нито жителите на Магедон и селата му; но ханаанците настояваха да живеят в оная земя.
28 Aisraeli atakhala amphamvu, anawagwiritsa Akanaaniwo ntchito yakalavulagaga, koma sanawapirikitse.
А Израил, когато стана силен наложи на ханаанците данък, без да ги изгони съвсем.
29 Nawonso Aefereimu sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Gezeri, choncho Akanaaniwo ankakhalabe pakati pawo ku Gezeriko.
Нито Ефрем изгони ханаанците, които живееха в Гезер; но ханаанците живееха в Гезер помежду им.
30 Azebuloni sanathamangitse Akanaani amene amakhala mu Kitironi kapena a ku Nahaloli. Iwo ankakhala pakati pawo ndipo ankawagwiritsa ntchito yakalavulagaga.
Завулон тоже не изгони жителите на Китрон, нито жителите на Наалол; но ханаанците живееха между тях и бяха обложени с данък.
31 A fuko la Aseri nawo sanathamangitse amene amakhala mu Ako, Sidoni, Ahilabu, Akizibu, Heliba, Afiki, ndi Rehobu.
Асир не изгони жителите на Акхо, нито жителите на Сидон, нито на Ахлав, нито на Ахзив, нито на Хелва, нито на Афек, нито на Роов;
32 Choncho anthu a fuko la Aseri anakhala pakati pa Akanaani amene ankakhala mʼdzikomo popeza sanawapirikitse.
но асирците обитаваха между ханаанците, местните жители, защото не ги изгониха.
33 Nalonso fuko la Nafutali silinathamangitse anthu amene ankakhala ku Beti Semesi kapena ku Beti Anati. Koma Anafutaliwo ankakhala pakati pa Akanaaniwo mʼdzikomo. Koma anthu amene ankakhala ku Beti Semesi ndi ku Beti Anati anawasandutsa kukhala ogwira ntchito yathangata.
Нефталим не изгони жителите на Ветсемес, нито жителите на Ветенат, но живееше между ханаанците, местните жители; обаче жителите на Ветсемес и на Ветенат му плащаха данък.
34 Aamori anapirikitsira anthu a fuko la Dani ku dziko la ku mapiri popeza sanawalole kuti atsikire ku chigwa.
И аморейците принудиха данците да се оттеглят в хълмистата страна, защото не ги оставиха да слизат в долината;
35 Aamori anatsimikiza mtima zokhalabe ku phiri la Hara-Heresi, ku Ayaloni, ndiponso ku Saalibimu. Koma a fuko la Yosefe anakula mphamvu ndipo anagwiritsa Aamoriwo ntchito yakalavulagaga.
но аморейците настояваха да живеят в гората Ерес, в Еалон, и в Саалвим. Но при все това, ръката на Иосифовия дом преодоля, така щото ония бяха обложени с данък.
36 Malire a Aamori anayambira ku chikweza cha Akirabimu nʼkulowera ku Sela napitirira kumapita chakumapiri ndithu.
А пределите на аморейците беше от нагорнището на Акравим, от скалата и нагоре.