< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
И Авимелех син Јеровалов отиде у Сихем к браћи матере своје и рече њима и свему роду отачкога дома матере своје говорећи:
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Кажите свим Сихемљанима: Шта вам је боље, да су вам господари седамдесет људи, сви синови Јеровалови, или да вам је господар један човек? И опомињите се да сам ја кост ваша и тело ваше.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
Тада рекоше браћа матере његове за њ свим Сихемљанима све те речи, и срце њихово приви се к Авимелеху, јер рекоше: Наш је брат.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
И дадоше му седамдесет сикала сребра из дома Вал-Веритовог, за које најми Авимелех људи празнова и скитница, те иђаху за њим.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
И дође у кућу оца свог у Офру, и поби браћу своју, синове Јеровалове, седамдесет људи, на једном камену; али оста Јотам најмлађи син Јеровалов, јер се сакри.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
Тада се скупише сви Сихемљани и сав дом Милов, и отидоше и поставише Авимелеха царем код храста који стоји у Сихему.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
А кад то јавише Јотаму, отиде и стаде наврх горе Гаризина, и подигавши глас свој повика и рече им: Чујте ме, Сихемљани, тако вас Бог чуо!
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Ишла дрвета да помажу себи цара, па рекоше маслини: Буди нам цар.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
А маслина им рече: Зар ја да оставим претилину своју, којом се част чини Богу и људима, па да идем да тумарам за друга дрвета?
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
Потом рекоше дрвета смокви: Ходи ти, буди нам цар.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
А смоква им рече: Зар ја да оставим сласт своју и красни род свој, па да идем да тумарам за друга дрвета?
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
Тада рекоше дрвета виновој лози: Ходи ти, буди нам цар.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
А лоза им рече: Зар ја да оставим вино своје, које весели Бога и људе, па да идем да тумарам за друга дрвета?
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
Тада сва дрвета рекоше трну: Ходи ти, буди нам цар.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
А трн одговори дрветима: Ако доиста хоћете мене да помажете себи за цара, ходите склоните се у хлад мој; ако ли нећете, нека изиђе огањ из трна и спали кедре ливанске.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
Тако сада, јесте ли право и поштено радили поставивши Авимелеха царем? И јесте ли добро учинили Јеровалу и дому његовом? И јесте ли му учинили како вас је задужио?
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
Јер је отац мој војевао за вас и није марио за живот свој, и избавио вас је из руку мадијанских.
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
А ви данас устасте на дом оца мог, и побисте синове његове, седамдесет људи, на једном камену, и постависте царем Авимелеха, сина слушкиње његове, над Сихемљанима зато што је брат ваш.
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
Ако сте право и поштено радили данас према Јеровалу и његовом дому, веселите се с Авимелеха и он нека се весели с вас.
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
Ако ли нисте, нека изиђе огањ од Авимелеха и спали Сихемљане и дом Милов, и нека изиђе огањ од Сихемљана и од дома Миловог и спали Авимелеха.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
Тада побеже Јотам, и побегав дође у Вир, и онде оста бојећи се Авимелеха брата свог.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
И влада Авимелех Израиљем три године.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
Али Бог пусти злу вољу међу Авимелеха и међу Сихемљане; и Сихемљани изневерише Авимелеха.
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
Да би се осветила неправда учињена на седамдесет синова Јеровалових, и крв њихова да би дошла на Авимелеха брата њиховог, који их уби, и на Сихемљане, који укрепише руку његову да убије браћу своју.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
И Сихемљани пометаше му заседе по врховима горским, па плењаху све који пролажаху мимо њих оним путем. И би јављено Авимелеху.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
Потом дође Гал син Еведов са својом браћом, и уђоше у Сихем, и Сихемљани се поуздаше у њ.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
И изишавши у поље браше винограде своје и газише грожђе, и веселише се; и уђоше у кућу бога свог; и једоше и пише, и псоваше Авимелеха.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
И Гал син Еведов рече: Ко је Авимелех и шта је Сихем, да му служимо? Није ли син Јеровалов? А Зевул није ли његов пристав? Служите синовима Емора оца Сихемовог. А што бисмо служили томе?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
О кад би тај народ био под мојом руком, да сметнем Авимелеха! И рече Авимелеху: Прикупи војску своју, и изиђи.
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
А кад чу Зевул, управитељ градски, речи Гала сина Еведовог, разгневи се врло.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
И посла тајно посланике к Авимелеху и поручи му: Ево Гал син Еведов и браћа му дођоше у Сихем, и ево побунише град на те.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
Него устани ноћу ти и народ што је с тобом, и заседи у пољу.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
А ујутро кад сунце огране, дигни се и удари на град; и ево он и народ који је с њим изићи ће преда те, па учини с њим шта ти може рука.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
И Авимелех уста ноћу и сав народ што беше са њим; и заседоше Сихему у четири чете.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
А Гал син Еведов изиђе и стаде пред вратима градским; а Авимелех и народ што беше са њим изиђе из заседе.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
А Гал видевши народ рече Зевулу: Ено народ силази сврх горе. А Зевул му одговори: Од сена горског чине ти се људи.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
Опет проговори Гал и рече: Ено народ силази с виса, и чета једна иде путем к шуми меоненимској.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
А Зевул му рече: Где су ти сада уста, којима си говорио: Ко је Авимелех да му служимо? Није ли то онај народ који си презирао? Изиђи сада, и биј се с њим.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
И изиђе Гал пред Сихемљанима, и поби се с Авимелехом.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
Али Авимелех га потера, и он побеже од њега; и падоше многи побијени до самих врата градских.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
И Авимелех оста у Аруми; а Зевул истера Гала и браћу његову, те не могаху седети у Сихему.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
А сутрадан изиђе народ у поље и би јављено Авимелеху.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
А он узе народ свој и раздели га у три чете, и намести их у заседу у пољу; и кад виде где народ излази из града, скочи на њ их и поби их.
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
Јер Авимелех и чета која беше с њим ударише и стадоше код врата градских; а друге две чете ударише на све оне који беху у пољу, и побише их.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
И Авимелех бијаше град цео онај дан, и узе га, и поби народ који беше у њему, и раскопа град, и посеја со по њему.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
А кад то чуше који беху у кули сихемској, уђоше у кулу куће бога Верита.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
И би јављено Авимелеху да су се онде скупили сви који беху у кули сихемској.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
Тада Авимелех изиђе на гору Салмон, он и сав народ што беху са њим; и узевши Авимелех секиру у руку одсече грану од дрвета и метну је на раме, и рече народу који беше с њим: Шта видесте да сам ја учинио, брзо чините као ја.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
И сваки из народа одсече себи грану, и пођоше за Авимелехом и пометаше гране око куле, и запалише њима град; и изгибоше сви који беху у кули сихемској, око хиљаду људи и жена.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Потом отиде Авимелех на Тевес, и стаде у логор код Тевеса, и узе га.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
А беше тврда кула усред града, и у њу побегоше сви људи и жене и сви грађани, и затворивши се попеше се на кров од куле.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
А Авимелех дође до куле и удари на њу, и дође до врата од куле да је запали огњем.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
Али једна жена баци комад жрвња на главу Авимелеху и разби му главу.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
А он брже викну момка који му ношаше оружје, и рече му: Извади мач свој и уби ме, да не кажу за ме: Жена га је убила. И прободе га слуга његов, те умре.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
А кад видеше Израиљци где погибе Авимелех, отидоше сваки у своје место.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
Тако плати Бог Авимелеху за зло које је учинио оцу свом убивши седамдесет браће своје.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
И све зло људи Сихемљана поврати Бог на њихове главе, и стече им се клетва Јотама сина Јероваловог.

< Oweruza 9 >