< Oweruza 9 >
1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
And he went Abimelech [the] son of Jerub-Baal Shechem towards to [the] brothers of mother his and he spoke to them and to all [the] clan of [the] house of [the] father of mother his saying.
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
Speak please in [the] ears of all [the] citizens of Shechem what? [is] good for you ¿ to rule over you seventy man all [the] sons of Jerub-Baal or? to rule over you a man one and you will remember that [am] bone your and flesh your I.
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
And they spoke [the] brothers of mother his on him in [the] ears of all [the] citizens of Shechem all the words these and it turned aside heart their after Abimelech for they said [is] brother our he.
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
And they gave to him seventy silver (from [the] house of Baal-*L(abh)*) Berith and he hired for them Abimelech men unprincipled and undisciplined and they went after him.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
And he went [the] house of father his Ophrah towards and he killed brothers his [the] sons of Jerub-Baal (seventy *L(abh)*) man on stone one and he was left Jotham [the] son of Jerub-Baal young for he hid himself.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
And they gathered all [the] citizens of Shechem and all Beth Millo and they went and they made king Abimelech to king near [the] great tree set up which [was] in Shechem.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
And people told to Jotham and he went and he stood on [the] top of [the] mountain of Gerizim and he lifted up voice his and he called out and he said to them listen to me O citizens of Shechem so he may listen to you God.
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
Certainly they went the trees to anoint over them a king and they said to the olive tree (reign! *Q(k)*) over us.
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
And it said to them the olive tree ¿ will I cease fatness my which by me people honor gods and men and will I go to sway over the trees.
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
And they said the trees to the fig tree come you reign over us.
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
And it said to them the fig tree ¿ will I cease sweetness my and fruit my good and will I go to sway over the trees.
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
And they said the trees to the vine come you (reign *Q(k)*) over us.
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
And it said to them the vine ¿ will I cease new wine my which makes glad gods and men and will I go to sway over the trees.
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
And they said all the trees to the thorn bush come you reign over us.
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
And it said the thorn bush to the trees if in truth you [are] anointing me to king over you come take refuge in shade my and if not let it go out a fire from the thorn bush and let it consume [the] cedars of Lebanon.
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
And now if in faithfulness and in integrity you have acted and you have made king Abimelech and if good you have done with Jerub-Baal and with house his and if according to [the] dealing of hands his you have done to him.
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
That he fought father my on you and he threw life his from in front and he delivered you from [the] hand of Midian.
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
And you you have risen up on [the] house of father my this day and you have killed sons his seventy man on stone one and you have made king Abimelech [the] son of female slave his over [the] citizens of Shechem for [is] brother your he.
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
And if in faithfulness and in integrity you have acted with Jerub-Baal and with house his the day this rejoice in Abimelech so he may rejoice also he in you.
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
And if not let it go out a fire from Abimelech and let it consume [the] citizens of Shechem and Beth Millo and let it go out a fire from [the] citizens of Shechem and from Beth Millo and let it consume Abimelech.
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
And he fled Jotham and he ran away and he went Beer towards and he dwelt there [away] from before Abimelech brother his.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
And he ruled Abimelech over Israel three years.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
And he sent God a spirit evil between Abimelech and between [the] citizens of Shechem and they dealt treacherously [the] citizens of Shechem with Abimelech.
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
To come [the] violence of seventy [the] sons of Jerub-Baal and blood their to put on Abimelech brother their who he killed them and on [the] citizens of Shechem who they strengthened hands his to kill brothers his.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
And they set to him [the] citizens of Shechem ambushers on [the] tops of the mountains and they robbed every [one] who he passed by on them on the road and it was told to Abimelech.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
And he came Gaal [the] son of Ebed and brothers his and they passed on in Shechem and they trusted in him [the] citizens of Shechem.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
And they went out the field and they gathered grapes vineyards their and they trod [them] and they made rejoicings and they went [the] house of god their and they ate and they drank and they cursed Abimelech.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
And he said - Gaal [the] son of Ebed who? [is] Abimelech and who? [is] Shechem that we will serve him ¿ not [is he] [the] son of Jerub-Baal and [is] Zebul? deputy his serve [the] men of Hamor [the] father of Shechem and why? will we serve him we.
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
And who? will he give the people this in hand my and I will remove Abimelech and he said of Abimelech make numerous army your and come out!
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
And he heard Zebul [the] official of the city [the] words of Gaal [the] son of Ebed and it burned anger his.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
And he sent messengers to Abimelech in treachery saying here! Gaal [the] son of Ebed and brothers his [are] coming Shechem towards and here they [are] shutting up the city on you.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
And therefore arise night you and the people which [is] with you and lie in wait in the field.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
And it will be in the morning when rises the sun you will rise early and you will make a raid on the city and there! he and the people which [is] with him [are] going out against you and you will do to him just as it will find hand your.
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
And he arose Abimelech and all the people which [was] with him night and they lay in wait on Shechem four companies.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
And he went out Gaal [the] son of Ebed and he stood [the] entrance of [the] gate of the city and he arose Abimelech and the people which [was] with him from the ambush.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
And he saw Gaal the people and he said to Zebul there! a people [is] coming down from [the] tops of the mountains and he said to him Zebul [the] shadow of the mountains you [are] seeing like men.
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
And he repeated again Gaal to speak and he said there! a people [are] coming down from with [the] center of the land and a company one [is] coming from [the] direction of [the] great tree of [the] soothsayer.
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
And he said to him Zebul where? then [is] mouth your O [you] who you said who? [is] Abimelech that we will serve him ¿ not [is] this the people which you rejected it go out please now and fight against him.
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
And he went out Gaal before [the] citizens of Shechem and he fought against Abimelech.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
And he pursued him Abimelech and he fled from before him and they fell [those] fatally wounded many to [the] entrance of the gate.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
And he dwelt Abimelech at Arumah and he drove out Zebul Gaal and brothers his from dwelling at Shechem.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
And it was from [the] next day and it went out the people the field and people told to Abimelech.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
And he took the people and he divided them into three companies and he lay in wait in the field and he saw and there! the people [was] going out from the city and he rose up on them and he struck down them.
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
And Abimelech and the companies which [were] with him they made a raid and they stood [the] entrance of [the] gate of the city and [the] two the companies they made a raid on all [those] who [were] in the field and they struck down them.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
And Abimelech [was] fighting against the city all the day that and he captured the city and the people which [was] in it he killed and he pulled down the city and he sowed it salt.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
And they heard all [the] citizens of [the] tower of Shechem and they went into [the] underground chamber of [the] house of El-Berith.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
And it was told to Abimelech that they had gathered together all [the] citizens of [the] tower of Shechem.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
And he went up Abimelech [the] mountain of Zalmon he and all the people which [was] with him and he took Abimelech the axes in hand his and he cut off a branch of wood and he lifted up it and he put [it] on shoulder his and he said to the people which [was] with him whatever you have seen I have done hurry do like me.
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
And they cut off also all the people everyone own branch his and they went after Abimelech and they put [them] over the underground chamber and they set on fire over them the underground chamber with fire and they died also all [the] men of [the] tower of Shechem about a thousand man and woman.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
And he went Abimelech to Thebez and he encamped at Thebez and he captured it.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
And a tower of strength it was in [the] middle of the city and they fled there towards all the men and the women and all [the] citizens of the city and they shut [the] door behind them and they went up on [the] roof of the tower.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
And he came Abimelech to the tower and he fought against it and he drew near to [the] entrance of the tower to burn it with fire.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
And she threw a woman one a mill-stone of an upper mill-stone on [the] head of Abimelech and it crushed skull his.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
And he called quickly to the young man - [who] carried armor his and he said to him draw sword your and kill me lest people should say of me a woman she killed him and he pierced through him young man his and he died.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
And they saw [the] man of Israel that he was dead Abimelech and they went everyone to own place his.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
And he repaid God [the] evil of Abimelech which he had done to father his by killing seventy brothers his.
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
And all [the] evil of [the] men of Shechem he repaid God on head their and it came to them [the] curse of Jotham [the] son of Jerub-Baal.