< Oweruza 9 >

1 Abimeleki mwana wa Yeru-Baala anapita ku Sekemu kwa abale a amayi ake ndi kukawawuza iwowo ndi fuko lonse la banja la abambo a amayi ake kuti,
Abimelech the son of Jerubbaal went to Shechem to his mother's brothers, and spoke with them, and with all the family of the house of his mother's father, saying,
2 “Funsani nzika zonse za ku Sekemu kuno, ‘Chabwino ndi chiyani kwa inu kuti ana onse makumi asanu ndi awiri a Yeru-Baala azikulamulirani, kapena kuti azikulamulirani ndi munthu mmodzi basi?’ Kumbukirani kuti ine ndine mʼbale wanu weniweni.”
"Please speak in the ears of all the lords of Shechem, 'Is it better for you that all the sons of Jerubbaal, who are seventy persons, rule over you, or that one rule over you?' Remember also that I am your bone and your flesh.'"
3 Abale a amayi akewo anamuyankhulira mawu amenewa kwa nzika zonse za ku Sekemu, ndipo mitima ya anthu onse inali pa Abimeleki chifukwa anati, “Uyu ndi mʼbale wathu,”
And his mother's brothers spoke of him in the ears of all the lords of Shechem all these words: and their hearts inclined to follow Abimelech; for they said, "He is our brother."
4 Tsono anamupatsa ndalama zasiliva 70 za mʼnyumba ya chipembedzo ya Baala Beriti. Ndi ndalama zimenezi Abimeleki analemba anthu achabechabe ndi osasamala kuti azimutsatira.
They gave him seventy pieces of silver out of the house of Baal Berith, with which Abimelech hired vain and light fellows, who followed him.
5 Anapita ku Ofiri ku mudzi kwa abambo ake ndipo anapha abale ake makumi asanu ndi awiri, ana a Yeru-Baala pa mwala umodzi. Koma Yotamu yemwe anali wamngʼono mwa onsewo anapulumuka chifukwa anabisala.
He went to his father's house at Ophrah, and killed his brothers the sons of Jerubbaal, being seventy persons, on one stone. But Jotham the youngest son of Jerubbaal was left; for he hid himself.
6 Tsono nzika za ku Sekemu ndi za ku Beti-Milo zinapita kukasonkhana ku mtengo wa thundu pafupi ndi chipilala cha ku Sekemu kuti akalonge Abimeleki ufumu.
And all the lords of Shechem assembled themselves together, and all Beth Millo, and went and made Abimelech king by the oak which is found at the pillar in Shechem.
7 Yotamu atamva izi anapita kukayima pamwamba pa phiri la Gerizimu ndipo anafuwula nati, “Tandimverani inu anthu a ku Sekemu, kuti Mulungu akumvereninso.
And when they told it to Jotham, he went and stood on the top of Mount Gerizim, and lifted up his voice, and cried, and said to them, "Listen to me, you lords of Shechem, that God may listen to you.
8 Tsiku lina mitengo inapita kukadzoza mfumu yawo. Tsono mitengoyo inati kwa mtengo wa olivi, ‘Iwe ukhale mfumu yathu.’”
The trees went forth on a time to anoint a king over them; and they said to the olive tree, 'Reign you over us.'
9 “Koma mtengo wa olivi uja unayankha kuti, ‘Kodi ndisiye mafuta angawa amene amalemekezera nawo milungu ndi anthu omwe, kuti ndizikalamulira mitengo?’”
"But the olive tree said to them, 'Should I leave my fatness, with which by me they honor God and man, and go to wave back and forth over the trees?'
10 Apo mitengo inawuza mtengo wa mkuyu kuti, “Bwera ndiwe ukhale mfumu yathu.”
"The trees said to the fig tree, 'Come, and reign over us.'
11 Koma mtengo wa mkuyu unayankha kuti, “Kodi ndisiye chipatso changa chokoma ndi chozunachi kuti ndizikalamulira mitengo?”
"But the fig tree said to them, 'Should I leave my sweetness, and my good fruit, and go to wave back and forth over the trees?'
12 Kenaka mitengo ija inawuza mtengo wamphesa kuti, “Bwera ndiwe kuti ukhale mfumu yathu.”
"The trees said to the vine, 'Come, and reign over us.'
13 Koma mtengo wamphesa unayankha kuti, “Kodi ine ndisiye vinyo wangayu, amene amasangalatsa milungu ndi anthu omwe kuti ndizikalamulira mitengo?”
"The vine said to them, 'Should I leave my new wine, which cheers God and man, and go to wave back and forth over the trees?'
14 Pomaliza mitengo yonse inawuza mkandankhuku kuti, “Bwera ndipo ukhale mfumu yathu.”
"Then all the trees said to the bramble, 'Come, and reign over us.'
15 Mkandankhuku uja unayankha kuti, “Ngati mukufunadi kuti mudzoze ine kuti ndikhale mfumu yanu, bwerani mudzabisale mu mthunzi mwangamu, koma ngati simutero, moto utuluka kwa ine ndi kupsereza mikungudza ya ku Lebanoni.”
"The bramble said to the trees, 'If in truth you anoint me king over you, then come and take refuge in my shade; and if not, let fire come out of the bramble, and devour the cedars of Lebanon.'
16 Yotamu anatinso, “Kodi mukuti munaonetsadi kuona mtima ndi kukhulupirika podzoza Abimeleki kukhala mfumu? Kodi mukuti munachitira ulemu Yeru-Baala ndi banja lake poganizira ntchito zimene anachita?
"Now therefore, if you have dealt truly and righteously, in that you have made Abimelech king, and if you have dealt well with Jerubbaal and his house, and have done to him according to the deserving of his hands
17 Kodi suja abambo anga anakumenyerani nkhondo ndi kuyika moyo wawo pa chiswe kuti akupulumutseni mʼmanja mwa Amidiyani?
(for my father fought for you, and risked his life, and delivered you out of the hand of Midian:
18 Koma lero inu mwawukira banja la abambo anga. Mwapha ana ake 70 pa mwala umodzi, ndiponso mwalonga ufumu Abimeleki, mwana wa mdzakazi wake kuti akhale wolamulira anthu a ku Sekemu chifukwa ndi mʼbale wanu.
and you are risen up against my father's house this day, and have slain his sons, seventy persons, on one stone, and have made Abimelech, the son of his female servant, king over the lords of Shechem, because he is your brother).
19 Tsono ngati mukuti zimene mwachitira Yeru-Baala ndi banja lake mwazichita moona mtima ndiponso mokhulupirika, ndiye mukondwere ndi Abimeleki, nayenso akondwere nanu!
If you then have dealt truly and righteously with Jerubbaal and with his house this day, then rejoice in Abimelech, and let him also rejoice in you:
20 Koma ngati sichoncho moto utuluke mwa Abimeleki ndi kupsereza anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndipo moto utulukenso mwa anthu a ku Sekemu ndi Beti-Milo, ndi kupsereza Abimeleki!”
but if not, let fire come out from Abimelech, and devour the lords of Shechem, and Beth Millo; and let fire come out from the lords of Shechem, and from Beth Millo, and devour Abimelech."
21 Kenaka Yotamu anathawira ku Beeri nakakhala komweko chifukwa ankaopa Abimeleki mʼbale wake.
And Jotham escaped and fled and went to Beer and lived there, for fear of Abimelech his brother.
22 Abimeleki atalamulira Israeli zaka zitatu,
Abimelech was prince over Israel three years.
23 Mulungu anayika chidani pakati pa Abimelekiyo ndi anthu a ku Sekemu, motero kuti anthu a ku Sekemu anawukira Abimeleki.
And God sent a spirit of hostility between Abimelech and the lords of Shechem; and the lords of Shechem dealt treacherously with Abimelech:
24 Mulungu anachita zimenezi kuti zoyipa zimene anachitira ana aamuna 70 a Yeru-Baala aja zimubwerere, ndi kuti magazi awo akhale pa Abimeleki mʼbale wawo ndi pa anthu a ku Sekemu amene anamulimbikitsa mtima kuti aphe abale akewo.
that the violence done to the seventy sons of Jerubbaal might come, and that their blood might be laid on Abimelech their brother, who killed them, and on the men of Shechem, who strengthened his hands to kill his brothers.
25 Choncho anthu a ku Sekemu anayika anthu omubisalira pamwamba pa mapiri. Tsono iwo ankalanda anthu odutsa mʼnjira imeneyo zinthu zawo ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
And the lords of Shechem set an ambush for him on the tops of the mountains, and they robbed all who came along that way by them. And it was told to Abimelech.
26 Gaali mwana wa Ebedi anasamukira ku Sekemu ndi abale ake, ndipo anthu a ku Sekemuko anamukhulupirira iye.
And Gaal the son of Ebed came with his brothers, and went over to Shechem; and the lords of Shechem put their trust in him.
27 Anthuwo anapita ku munda kukathyola mphesa ndi kuzifinya, ndipo anachita chikondwerero mʼnyumba ya milungu yawo. Anthuwo akudya ndi kumwa, ankatemberera Abimeleki.
They went out into the field, and gathered their vineyards, and trod the grapes, and held festival, and went into the house of their god, and did eat and drink, and cursed Abimelech.
28 Ndipo Gaali mwana wa Ebedi anati “Kodi Abimeleki ndi ndani, ndipo nʼchifukwa chiyani akutilamulira ife Asekemu? Kodi iyeyu si mwana wa Yeru-Baala ndipo womuthandiza wake si Zebuli? Tiyeni titumikire anthu a ku Hamori, kholo la fuko la Sekemu! Nanga nʼchifukwa chiyani tikutumikira Abimeleki?
Gaal the son of Ebed said, "Who is Abimelech, and who is Shechem, that we should serve him? Isn't he the son of Jerubbaal, and Zebul his officer? Serve the men of Hamor the father of Shechem. But why should we serve him?
29 Anthu a mu mzindawo akanakhala pansi pa ulamuliro wanga, ndikanamuchotsa Abimelekiyu. Ndikanamuwuza Abimeleki kuti, ‘Wonjeza ankhondo ako ndipo ubwere tidzamenyane!’”
Would that this people were under my hand. Then I would remove Abimelech. I would say to Abimelech, "Increase your army, and come out."
30 Zebuli amene ankalamulira mzindawo atamva zimene Gaali mwana wa Ebadi ananena, anakwiya kwambiri.
When Zebul the ruler of the city heard the words of Gaal the son of Ebed, his anger was kindled.
31 Anatumiza amithenga kwa Abimeleki, kukanena kuti, “Gaali mwana wa Ebedi ndi abale ake abwera ku Sekemu ndipo akuwutsa mitima ya anthu a mu mzindawo kuti akuwukireni inu.
He sent messengers to Abimelech in Arumah, saying, "Look, Gaal the son of Ebed and his brothers have come to Shechem; and look, they constrain the city to take part against you.
32 Nʼchifukwa chake usiku womwe uno inu ndi anthu anu mupite, mukabisale mʼminda.
Now therefore, rise up by night, you and the people who are with you, and lie in wait in the field.
33 Mmawa dzuwa likutuluka, mudzuke ndi kukathira nkhondo mzindawo. Gaali ndi anthu amene ali naye akamadzabwera kuti alimbane ndi inu, inu mudzathane nawo monga mmene mungachitire.”
And it shall be that in the morning, as soon as the sun is up, you shall rise early, and rush on the city. And look, when he and the people who are with him come out against you, then do whatever you can to them."
34 Choncho Abimeleki ndi ankhondo ake onse anadzuka usiku nakabisalira mzinda wa Sekemu mʼmagulu anayi.
Abimelech rose up, and all the people who were with him, by night, and they lay in wait against Shechem in four companies.
35 Gaali mwana wa Ebedi anatuluka nakayima pa khomo pa chipata cha mzinda pamene Abimeleki ndi ankhondo ake anatuluka ku malo kumene anabisala kuja.
And it happened early in the morning that Gaal the son of Ebed went out, and stood in the entrance of the gate of the city. And Abimelech rose up, and the people who were with him, from the ambush.
36 Gaaliyo atawaona, anawuza Zebuli kuti, “Taona anthu akutsika kuchoka pamwamba pa mapiri.” Koma Zebuli anayankha kuti, “Zimene mukuonazo ndi zithunzi za mapiri chabe osati anthu.”
When Gaal saw the people, he said to Zebul, "Look, there are people coming down from the tops of the mountains." Zebul said to him, "You see the shadow of the mountains as if they were men."
37 Koma Gaaliyo anayankhulanso kuti, “Taona anthu akutsika kuchokera pakati pa phiri, ndipo gulu lina likubwera kuchokera ku mtengo wa thundu wa owombeza mawula.”
Gaal spoke again and said, "Look, there are people coming down by the central part of the land, and one company comes by the way of the Diviners' Oak."
38 Ndipo Zebuli anamufunsa iye kuti, “Pakamwa pako paja pali kuti tsopano, iwe amene umanena kuti, Abimeleki ndaninso kuti ife timutumikire? Kodi amenewa si anthu aja umawanyozawa? Tsopano tuluka ukamenyane nawo.”
Then Zebul said to him, "Where is now your mouth, that you said, 'Who is Abimelech, that we should serve him?' Is not this the people that you have despised? Please go out now and fight with them."
39 Choncho Gaaliyo anatuluka akutsogolera anthu a ku Sekemu kukamenyana ndi Abimeleki.
And Gaal went out before the lords of Shechem, and fought with Abimelech.
40 Koma Abimeleki anamuthamangitsa ndipo Gaala anathawa. Ambiri a ankhondo ake anagwa napwetekeka njira yonse mpaka ku chipata cha mzinda.
Abimelech chased him, and he fled before him, and there fell many wounded, even to the entrance of the gate of the city.
41 Abimeleki anakhala ku Aruma, ndipo Zebuli anathamangitsa Gaali pamodzi ndi abale ake, kuwatulutsa mu Sekemu.
And Abimelech returned to Arumah; and Zebul drove out Gaal and his brothers, so that they could not dwell in Shechem.
42 Mmawa mwake anthu a ku Sekemu anapangana zopita ku minda, ndipo Abimeleki anamva zimenezi.
It happened on the next day, that the people went out into the field; and they told Abimelech.
43 Tsono Abimeleki anatenga anthu ake, nawagawa magulu atatu ndi kukabisala mʼminda. Ataona anthu akutuluka mu mzindawo, iye anapita kukalimbana nawo ndipo onsewo anawapha.
He took the people, and divided them into three companies, and waited in ambush in the field; and he looked, and look, the people came forth out of the city. He rose up against them, and struck them.
44 Abimeleki pamodzi ndi magulu ake anathamangira kutsogolo nakawakhalira pa chipata cha mzinda. Ndipo magulu awiri ena aja anathamangira anthu amene anali mʼminda ndi kuwapha onse.
Abimelech, and the companies that were with him, rushed forward, and stood in the entrance of the gate of the city: and the two companies rushed against all who were in the field, and struck them.
45 Abimeleki anawuthira nkhondo mzindawo tsiku lonse. Kenaka anawulanda ndi kupha nzika zonse za mu mzindamo. Anawuwonongeratu mzindawo nawuwaza mchere.
Abimelech fought against the city all that day; and he took the city, and killed the people who were in it. And he destroyed the city, and sowed it with salt.
46 Anthu a mu nsanja ya Sekemu atamva zimenezi, anakalowa mu linga la nyumba yopembedzeramo Baala-Beriti.
And when all the lords of the Tower of Shechem heard of it, they entered into the stronghold of the house of El Berith.
47 Abimeleki anamva kuti anthu ena asonkhana kumeneko.
And it was told Abimelech that all the lords of the Tower of Shechem were gathered together.
48 Choncho Abimeleki pamodzi ndi anthu ake onse anapita ku phiri la Zalimoni. Kumeneko anatenga nkhwangwa nadula nthambi za mitengo. Ananyamula nthambi zija pa phewa pake. Tsono anawuza anthu aja kuti, “Zimene mwaona ine ndikuchita, inunso mufulumire kuchita monga ndachitiramu.”
So Abimelech went up to Mount Zalmon, he and all the people who were with him; and Abimelech took an axe in his hand, and cut down a branch from the trees, and took it up, and laid it on his shoulder. And he said to the people who were with him, "What you have seen me do, do quickly, and do as I have done."
49 Tsono aliyense anadula nthambi zake, natsatira Abimeleki. Anakawunjika nthambi zija pa linga paja, kenaka ndi kuliyatsa moto. Choncho anthu onse a ku nsanja ya Sekemu anafa. Analipo anthu pafupifupi 1,000, amuna ndi akazi.
All the people likewise cut down his branch and followed Abimelech, and put them on the stronghold, and set the stronghold on fire on them; so that all the men of the Tower of Shechem died also, about a thousand men and women.
50 Kenaka Abimeleki anapita ku Tebezi. Anakawuzungulira mzindawo ndi kuwulanda.
Then Abimelech went to Thebez, and camped against Thebez, and took it.
51 Koma mu mzindamo munali nsanja yolimba. Anthu onse a mu mzindamo amuna ndi akazi anathawira mu nsanjayo, nadzitsekera mʼkati. Ndipo anakwera ku denga la nsanjayo.
But there was a strong tower within the city, and all the men and women fled, and all the lords of the city, and shut themselves in, and got them up to the roof of the tower.
52 Abimeleki anapita ku nsanjayo nathira nkhondo. Anafika pafupi ndi chitseko cha nsanja ija kuti ayitenthe.
Abimelech came to the tower, and fought against it, and drew near to the door of the tower to burn it with fire.
53 Koma mkazi wina anaponya mwala wa mphero pa mutu wa Abimeleki ndi kuswa chibade cha mutuwo.
A certain woman threw down an upper millstone on Abimelech's head, and broke his skull.
54 Mwamsanga Abimeleki anayitana mnyamata womunyamulira zida za nkhondo namuwuza kuti, “Solola lupanga lako undiphe kuti anthu asadzanene kuti, ‘Mkazi ndiye anamupha.’” Choncho wantchito wake anamubayadi mpaka kutulukira kunja lupangalo ndipo anafa.
Then he called quickly to the young man his armor bearer, and said to him, "Draw your sword, and kill me, that men not say of me, 'A woman killed him.'" So the young man thrust him through, and he died.
55 Aisraeli ataona kuti Abimeleki wafa, anapita kwawo.
When the men of Israel saw that Abimelech was dead, they departed every man to his place.
56 Mmenemu ndi mmene Mulungu analipsirira tchimo la Abimeleki limene anachitira abambo ake pakupha abale ake 70 aja.
Thus God requited the wickedness of Abimelech, which he did to his father, in killing his seventy brothers;
57 Mulungu anawalanganso anthu a ku Sekemu chifukwa cha kuyipa kwawo konse. Ndipo matemberero a Yotamu mwana wa Yeru-Baala anawagweradi.
and all the wickedness of the men of Shechem did God return on their heads, and on them came the curse of Jotham the son of Jerubbaal.

< Oweruza 9 >