< Oweruza 8 >

1 Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
OLELO aku la na kanaka o Eperaima ia ia, Heaha keia mea au i hana mai ai ia makou, i kou hea ole ana mai ia makou, i kou wa i hele aku ai e kaua me ko Midiana? Ikaika loa ko lakou hoopaapaa ana ia ia.
2 Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
Olelo ae la oia ia lakou, Heaha ka'u i hana'i me ka oukou? Aole anei i oi ke koena ai no Eperaima mamua o ka hoiliili ana o ka Abiezera?
3 Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
Ua haawi mai ke Akua i ko oukou lima i na'lii o Midiana, o Oreba, a me Zeeba. Heaha ka mea i hiki ia'u ke hana e like me ka oukou? Alaila, i kana olelo ana pela, maha ae la ko lakou huhu ia ia.
4 Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
Hele mai la o Gideona i Ioredane, a maalo ae la i kela aoao, oia a me ia mau haneri kanaka ekolu pu me ia, ua makaponiuniu, e hahai ana nae.
5 Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
I ae la ia i kanaka o Sukota, Ke nonoi aku nei au ia oukou, e haawi mai i mau popo berena na ka poe e hahai ana ia u; no ka mea, ua makaponiuniu lakou, a e hahai ana au ia Zeba, a me Zalemuna, i na'lii o ko Midiana.
6 Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
I mai la na'lii o Sukota, Ua loaa anei na lima o Zeba, laua o Zalemuna i kou lima, i haawi aku ai makou i berena na kou poe kaua?
7 Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
I ae la o Gideona, No ia mea, i ka wa e haawi mai ai o Iehova ia Zeba, laua o Zalemuna, i ko'u lima, alaila e kahi au i ko oukou io i ke kakalaioa a me na mea ooi o ka nahelehele.
8 Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
Pii aku la ia, mai laila aku, a i Penuela, a olelo aku la ia lakou pela. I mai la na kanaka o Penuela ia ia, e like me ka na kanaka o Sukota i i mai ai.
9 Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
Olelo ae la ia i na kanaka o Penuela, i aku la, A hoi mai au me ka malu, alaila, e wawahi au i keia halekiai.
10 Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
E noho ana o Zeba, laua o Zalemuna ma Karekora, a o ko laua mau puali pu me laua, he umikumamalima tausani paha, o ka poe a pau i koe o na puali o ka poe i noho ma ka hikina. Ua haule hookahi haneri me ka iwakalua tausani kanaka, unuhi pahi.
11 Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
Pii aku la o Gideona ma ke ala o ka poe noho ma na halelewa, ma ka hikina o Noba, a me Iogebeha, a luku aku la i ka puali; no ka mea, e noho makau ole ana ka puali.
12 Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
Hee aku la o Zeba, laua o Zalemuna, a hahai aku la ia ia laua, a pio iho la ia ia na'lii elua o Midiana, o Zeba a me Zalemuna, a auhee aku la ka puali a pau.
13 Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
Hoi mai la o Gideona, ke keiki a Ioasa, mai ke kaua ana mai, mamua o ka hiki ana a ka la.
14 Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
Paa iho la ia ia kekahi kanaka ui o Sukota, a ninau aku la ia ia, a hoike mai la oia ia ia i na'lii o Sukota a me kolaila poe lunakahiko, he kanahikukumamahiku kanaka.
15 Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
Hele mai la ia i kanaka o Sukota, i ae la, Eia hoi o Zeba, laua o Zalemuna, na mea a oukou i hoowahawaha mai ai ia'u, i ka i ana mai, Ua loaa anei na lima o Zeba laua o Zalemuna i kou lima, i haawi aku ai makou i ka berena na kou poe kanaka makaponiuniu?
16 Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
Lalau iho la ia i na lunakahiko o ia kulanakauhale, a me ke kakalaioa, a me na mea oioi o ka nahelehele, a me ia mau mea no ia i ao aku ai i na kanaka o Sukota.
17 Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
Wawahi iho la no hoi ia i ka halekiai o Penuela, a luku aku la i kanaka o ia kulanakauhale.
18 Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
Alaila, ninau aku la oia ia Zeba laua o Zalemuna, Heaha ke ano o na kanaka a olua i pepehi ai ma Tabora? I mai la laua, E like me oe nei, pela lakou. Ua like lakou a pau me na keiki alii.
19 Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
I aku la keia, he poe hoahanau lakou no'u, he poe keiki na ko'u makuwahine. Me Iehova e ola nei, ina i hoola olua ia lakou, ina aole au e pepehi aku ia olua.
20 Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
I mai la ia ia Ietera, i kana hiapo, E ku iluna, a pepehi ia laua. Aole unuhi ua keiki la i kana pahikaua; ua makau, no ka mea, he keiki ia.
21 Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
Alaila, olelo mai o Zeba laua o Zalemuna, E ku mai oe, a e pepehi mai ia maua, no ka mea, e like me ke kanaka, pela kona ikaika. Ku ae la o Gideona, a pepehi iho la ia Zeba, laua o Zalemuna, a lawe oia i na lei o na a-i o ka laua mau kamelo.
22 Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
Alaila, olelo aku la na kanaka o ka Iseraela ia Gideona, I alii oe maluna o makou, o oe a me kau keiki, a me ke keiki a kau keiki; no ka mea, ua hoola mai oe ia makou, mailoko ae o ka lima o ko Midiana.
23 Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
I mai la o Gideona ia lakou, aole au e lilo i alii maluna o oukou, aole e lilo ka'u keiki i alii maluna o oukou. E lilo no o Iehova i alii maluna o oukou.
24 Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
I mai la o Gideona ia lakou, He manao nonoi aku ko'u e nonoi aku ai ia oukou, e haawi mai kela kanaka keia kanaka o oukou ia'u, i na apo pepeiao o kona mea pio. (He apo pepeiao gula ko lakou, no ka mea, no ka Isemaela lakou.)
25 Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
I mai la lakou, E haawi io no makou. Hohola iho la lakou i lole, a hoolei iho la kela kanaka keia kanaka i na apo pepeiao o kona pio maluna iho.
26 Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
O ke kaumaha o ia mau apo pepeiao, ana i noi aku ai, hookahi ia tausani ehiku haueri sekela gula; a keu aku na lei, a me na momi pepeiao, a me ka lole poni mahana o na'lii o ko Midiana, a me na lei ma na a-i o ka laua mau kamelo.
27 Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
Hana iho la o Gideona ia mea, i epoda, a waiho iho la ma kona kulanakauhale, ma Opera. Hahai aku la ilaila ka Iseraela a pau, e kuko ana mamuli o ia mea; a lilo iho la ia i mea e hihia'i no Gideona, a me ko kona hale.
28 Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
Pela i pio ai ko Midiana imua o na mamo a Iseraela, aole lakou i hoala hou i ko lakou poo. Kuapapanui iho la ka aina hookahi kanaha makahiki, i ke kau ia Gideona.
29 Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
Hele aku la o Ierubaala ke keiki a Ioasa, a noho iho la ma kona hale iho.
30 Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
He kanahiku ka Gideona mau keikikane, mailoko aku o kona puhaka, no ka mea, ua nui loa kana poe wahine.
31 Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
A o kana haiawahine ma Se kema, oia kekahi i hanau mai i keikikane nana, a kapa aku la oia i kona inoa o Abimeleka.
32 Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
Make iho la o Gideona ke keiki a Ioasa, ua elemakule maikai, a kanuia oia ma ka ilina o kona makuakane, ma Opera, no ka Abiezara.
33 Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
A mahope iho o ka make ana o Gideona, huli hou aku la na mamo a Iseraela, a moe kolohe iho la me Baalima, a hoolilo iho la ia Baalaberita, i akua no lakou.
34 Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
Aole hoomanao na mamo a Iseraela ia Iehova, i ko lakou Akua, i ka mea i hoola'e ia lakou mai ka lima aku o ko lakou poe enemi, ma na aoao a puni.
35 Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.
Aole lakou i lokomaikai aku i ko ka hale o Ierubaala, oia hoi o Gideona, e like me na mea maikai a pau ana i hana mai ai i ka Iseraela.

< Oweruza 8 >