< Oweruza 8 >

1 Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
And the men of Ephraim said unto him, What is this thing that thou hast done unto us, not to call for us, when thou wentest to fight with the Midianites? And they quarrelled with him vehemently.
2 Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
And he said unto them, What have I done now in comparison with you? Is not the gleaning of Ephraim better than the vintage of Abi'ezer?
3 Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
Into your hand God delivered the princes of Midian, 'Oreb and Zeeb: and what have I been able to do in comparison with you? Then was their anger abated from him, when he had spoken this speech.
4 Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
And Gid'on came to the Jordan, and passed over, he, and the three hundred men that were with him, faint, and in pursuit.
5 Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
And he said unto the men of Succoth, Give, I pray you, a few loaves of bread unto the people that are in my train; for they are faint, and I am pursuing after Zebach and Zalmunna,' the kings of Midian.
6 Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
And the princes of Succoth said, Is the sole of the foot of Zebach and Zalmunna' now already in thy hand, that we should give unto thy army bread?
7 Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
And Gid'on said, Therefore when the Lord hath delivered Zebach and Zalmunna' into my hand, then will I thresh your flesh with the thorns of the wilderness and with briers.
8 Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
And he went up thence to Penuel, and spoke unto them in the same manner: and the men of Penuel answered him as the men of Succoth had answered.
9 Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
And he said also unto the men of Penuel thus, When I return again in peace, I will break down this tower.
10 Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
Now Zebach and Zalmunna' were in Karkor, and their camps with them, about fifteen thousand men, all that had been left of all the camp of the children of the east; but those who had fallen were one hundred and twenty thousand men that drew the sword.
11 Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
And Gid'on went up by the way of those that dwelt in tents, to the east of Nobach and Yogbehah, and smote the camp; but the camp thought itself secure.
12 Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
And Zebach and Zalmunna' fled; but he pursued after them, and captured the two kings of Midian, Zebach and Zalmunna', and all the camp he discomfited.
13 Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
And Gid'on the son of Joash returned from the battle before the rising of the sun,
14 Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
And he caught a young man of the people of Succoth, and inquired of him: and he wrote down for him the princes of Succoth, and the elders thereof, seventy and seven men.
15 Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
And he came unto the men of Succoth, and said, Behold here are Zebach and Zalmunna', with whom ye derided me, saying, Is the sole of the foot of Zebach and Zalmunna' now already in thy hand, that we should give unto thy weary men bread?
16 Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
And he took the elders of the city, and the thorns of the wilderness and briers, and chastised with them the men of Succoth.
17 Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
And the tower of Penuel he beat down, and slew the men of the city.
18 Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
And he said unto Zebach and Zalmunna', What kind of men were those whom ye slew at Tabor! And they answered, As thou art, so were they; one was in form like that of the children of a king.
19 Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
And he said, They were my brothers, the sons of my mother; as the Lord liveth, if ye had spared them alive, I would not slay you.
20 Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
And he said unto Yether his first-born, Rise up, and slay them. But the youth drew not his sword; for he was afraid, because he was yet a youth.
21 Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
Then said Zebach and Zalmunna', Rise thou, and fall upon us; for as the man is, so is his strength. And Gid'on arose, and slew Zebach and Zalmunna'; and he took away the crescent ornaments that were on the necks of their camels.
22 Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
And the men of Israel said unto Gid'on, Rule thou over us, both thou and thy son, and thy son's son also; for thou hast delivered us out of the hand of Midian.
23 Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
And Gid'on said unto them, I will not rule over you, neither shall my son rule over you: the Lord shall rule over you.
24 Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
And Gid'on said unto them, I would ask one request of you, that ye should give me every man the earring of his booty; for they had had golden earrings, because they were Ishmaelites.
25 Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
And they answered, We will willingly give. And they spread out a garment, and they cast therein every man the earring of his booty.
26 Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
And the weight of the golden earrings that he had requested was a thousand and seven hundred shekels of gold; besides the crescent ornaments, and ear-drops, and purple garments that were on the kings of Midian, and besides the chains that were about their camels' necks.
27 Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
And Gid'on made thereof an ephod, and set it up in his city, in 'Ophrah: and all Israel went astray after it thither; and it became a snare unto Gid'on, and to his house.
28 Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
And Midian was humbled before the children of Israel, so that they lifted not up their head any more. And the country was quiet forty years in the days of Gid'on.
29 Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
And Yerubba'al the son of Joash went and dwelt in his own house.
30 Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
And Gid'on had seventy sons begotten of his body; for he had many wives.
31 Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
And his concubine that was in Shechem, she also bore him a son, and he gave him the name, Abimelech.
32 Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
And Gid'on the son of Joash died in a good old age, and was buried in the sepulchre of Joash his father, in 'Ophrah of the Abi'ezrites.
33 Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
And it came to pass, when Gid'on was dead, that the children of Israel turned again, and went astray after the Be'alim, and made themselves Ba'al-berith for a god.
34 Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
And the children of Israel remembered not the Lord their God, who delivered them out of the hand of all their enemies on every side.
35 Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.
Neither showed they kindness to the house of Yerubba'al, namely, Gid'on, in accordance with all the good which he had done unto Israel.

< Oweruza 8 >