< Oweruza 7 >
1 Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
И обутренева Иероваал, сей есть Гедеон, и вси людие иже с ним, и ополчишася у источника Арад: и полк Мадиамль и Амаликов бяше ему с севера на холме Мосе Гавааф-Аморе в долине.
2 Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
И рече Господь к Гедеону: мнози людие иже с тобою, сего ради не предам Мадиама в руку их, да не когда похвалится Израиль на Мя, глаголя: рука моя спасе мя:
3 Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
и ныне рцы во ушы людем, глаголя: кто боязлив и ужастив, да возвратится и да отидет от горы Галаадовы. И возвратишася от людий двадесять две тысящы, и десять тысящ осташася.
4 Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
И рече Господь к Гедеону: еще людие мнози суть: сведи я на воду, и искушу тебе их тамо: и будет егоже аще реку тебе, сей да идет с тобою, той да пойдет с тобою: и всяк егоже аще реку тебе, сей да не пойдет с тобою, той да не пойдет с тобою.
5 Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
И сведе люди на воду, и рече Господь к Гедеону: всяк иже полочет языком своим от воды, якоже лочет пес, да поставиши его особь: и всяк иже на колену падет пити, отлучи его особь.
6 Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
И бысть число в горстех локавших языком триста мужей: и вси оставшии людие преклонишася на колена своя пити воду.
7 Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
И рече Господь к Гедеону: треми сты мужей локавшими воду спасу вас, и предам Мадиама в руку твою: и вси людие да пойдут, кийждо на место свое.
8 Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
И взяша себе брашно от людий в руку свою и роги своя: и всякаго мужа Израилтеска отпусти коегождо в кущу свою, а триста мужей удержа: полк же Мадиамль бяше ниже его в долине.
9 Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
И бысть в ту нощь, и рече к нему Господь: востав сниди отсюду скоро в полк, яко предах их в руку твою:
10 Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
и аще боишися ты снити, сниди ты и Фара раб твой в полк,
11 ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
и услышиши, что возглаголют: и по сем укрепятся руце твои, и снидеши в полк. И сниде сам и Фара раб его в часть пятьдесятников, иже быша в полце.
12 Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
И Мадиам и Амалик и вси сынове востоков стояху в долине яко прузи множеством, и велблюдом их не бяше числа, но бяху яко песок на краи морстем множеством.
13 Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
И вниде Гедеон, и се, муж поведаше сон подругу своему, и рече: сей сон егоже видех, и се, тесто хлеба ячна валяющееся в полце Мадиамли, и привалися к кущи Мадиамли, и поби ю, и преврати ю, и паде куща.
14 Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
И отвеща подруг его и рече: несть (сие тесто), но мечь Гедеона сына Иоасова мужа Израилева: предаде Бог в руку его Мадиама и весь полк.
15 Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
И бысть яко услыша Гедеон поведание сна и разсуждение его, и поклонися Господеви, и возвратися в полк Израилев и рече: востаните, яко предаде Господь в руки нашя полк Мадиамль.
16 Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
И раздели триста мужей на три началства, и вдаде роги в руце всем, и водоносы тщы, и свещы среде водоносов,
17 Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
и рече им: мене смотрите, и такожде творите: и се, аз вниду в часть полка, и будет якоже сотворю, такожде сотворите:
18 Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
и аз вострублю рогом, и вси иже со мною, да вострубите и вы в роги окрест всего полка, и да речете: (мечь) Богу и Гедеону.
19 Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
И вниде Гедеон и сто мужей иже с ним в часть полка в начале стражи средния: и убужением возбудиша стрегущих, и вострубиша в роги, и сразиша водоносы иже в руках их.
20 Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
И вострубиша три началства в роги и сокрушиша водоносы, и удержаша в левых руках своих свещы, и в десных руках их роги, в няже трубити: и возопиша: мечь Господеви и Гедеону.
21 Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
И сташа кийждо о себе окрест полка: и смятеся весь полк, и возопиша, и побегоша.
22 Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
И вострубиша в триста рогов: и положи Господь мечь мужа на подруга его во всем полце, и пробеже полк до Вифасетта, и собрася до страны Авелмаула и к Тавафу.
23 Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
И возопиша мужие Израилтестии от Неффалима и от Асира и от всего Манассии, и погнаша вслед Мадиама.
24 Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
И посла послы Гедеон во всю гору Ефремлю, глаголя: снидите во сретение Мадиаму и удержите им воду до Вефира и Иордана. И воззва всяк муж Ефремль, и предотяша воду до Вефира и Иордана,
25 Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.
и яша два князя Мадиамля, Орива и Зива: и убиша Орива в Суре, и Зива убиша во Иакефзиве: и погнаша Мадиама, и главу Орива и Зива принесоша к Гедеону от оноя страны Иордана.