< Oweruza 7 >

1 Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
And Jerubba‘al (he [is] Gideon) rises early, and all the people who [are] with him, and they encamp by the well of Harod, and the camp of Midian has been on the south of him, on the height of Moreh, in the valley.
2 Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
And YHWH says to Gideon, “The people who [are] with you [are] too many for My giving Midian into their hand, lest Israel beautify itself against Me, saying, My hand has given salvation to me;
3 Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
and now, please call in the ears of the people, saying, Whoever [is] afraid and trembling, let him turn back and go early from Mount Gilead”; and there return twenty-two thousand of the people, and ten thousand have been left.
4 Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
And YHWH says to Gideon, “The people [are] yet too many; bring them down to the water, and I refine him for you there; and it has been, he of whom I say to you, This goes with you—he goes with you; and any of whom I say to you, This does not go with you—he does not go.”
5 Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
And he brings the people down to the water, and YHWH says to Gideon, “Everyone who laps of the water with his tongue as the dog laps—you set him apart; also everyone who bows on his knees to drink.”
6 Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
And the number of those lapping with their hand to their mouth is three hundred men, and all the rest of the people have bowed down on their knees to drink water.
7 Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
And YHWH says to Gideon, “I save you by the three hundred men who are lapping, and have given Midian into your hand, and all the people go, each to his place.”
8 Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
And the people take the provision in their hand, and their horns, and he has sent every man of Israel away, each to his tents; and he has kept hold on the three hundred men, and the camp of Midian has been by him at the lower part of the valley.
9 Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
And it comes to pass, on that night, that YHWH says to him, “Rise, go down into the camp, for I have given it into your hand;
10 Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
and if you are afraid to go down—go down, you and your young man Phurah, to the camp,
11 ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
and you have heard what they speak, and afterward your hands are strengthened, and you have gone down against the camp.” And he goes down, he and his young man Phurah, to the extremity of the fifties who [are] in the camp;
12 Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
and Midian, and Amalek, and all the sons of the east are lying in the valley, as the locust for multitude, and of their camels there is no number, as sand which [is] on the seashore for multitude.
13 Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
And Gideon comes in, and behold, a man is recounting a dream to his companion, and says, “Behold, I have dreamed a dream, and behold, a cake of barley-bread is turning itself over into the camp of Midian, and it comes to the tent, and strikes it, and it falls, and turns it upwards, and the tent has fallen.”
14 Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
And his companion answers and says, “This is nothing except the sword of Gideon son of Joash, a man of Israel; God has given Midian and all the camp into his hand.”
15 Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
And it comes to pass, when Gideon hears the narration of the dream and its interpretation, that he bows himself, and turns back to the camp of Israel, and says, “Rise, for YHWH has given the camp of Midian into your hand.”
16 Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
And he divides the three hundred men [into] three detachments, and puts horns into the hand of all of them, and empty pitchers, and lamps within the pitchers.
17 Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
And he says to them, “Look at me, and thus do; and behold, I am coming into the extremity of the camp—and it has been—as I do so you do;
18 Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
and I have blown with a horn—I and all who [are] with me, and you have blown with horns, even you, around all the camp, and have said, For YHWH and for Gideon!”
19 Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
And Gideon comes—and the hundred men who [are] with him—into the extremity of the camp, [at] the beginning of the middle watch (they had just posted watchmen), and they blow with horns—also dashing in pieces the pitchers which [are] in their hand;
20 Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
and the three detachments blow with horns, and break the pitchers, and keep hold with their left hand on the lamps, and with their right hand on the horns to blow, and they cry, “The sword of YHWH and of Gideon!”
21 Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
And they each stand in his place, around the camp, and all the camp runs, and they shout, and flee;
22 Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
and the three hundred blow the horns, and YHWH sets the sword of each against his companion, even through all the camp; and the camp flees to Beth-Shittah, at Zererath, to the border of Abel-Meholah, by Tabbath.
23 Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
And the men of Israel are called from Naphtali, and from Asher, and from all Manasseh, and pursue after Midian.
24 Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
And Gideon has sent messengers into all the hill-country of Ephraim, saying, “Come down to meet Midian, and capture the waters from them as far as Beth-Barah, and the Jordan”; and every man of Ephraim is called, and they capture the waters as far as Beth-Barah, and the Jordan,
25 Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.
and they capture two of the heads of Midian, Oreb and Zeeb, and slay Oreb at the rock of Oreb, and they have slain Zeeb at the wine-vat of Zeeb, and they pursue into Midian; and they have brought the heads of Oreb and Zeeb to Gideon beyond the Jordan.

< Oweruza 7 >