< Oweruza 7 >
1 Yeru-Baala (Gideoni) ndi anthu ake onse anadzuka mʼmamawa nakamanga misasa pambali pa kasupe ku Harodi. Misasa ya Amidiyani inali mʼchigwa kumpoto kwa phiri la More.
Tedy vstav ráno Jerobál, (jenž jest Gedeon), i všecken lid, kterýž byl s ním, položili se při studnici Charod, vojska pak Madianských byla jim na půlnoci před vrchem More v údolí.
2 Yehova anati kwa Gideoni, “Anthu uli nawowa andichulukira kwambiri kuti ndigonjetse Amidiyani chifukwa Aisraeli angamadzitukumule pamaso panga ndi kumanena kuti, ‘Tadzipulumutsa ndi mphamvu zathu.’
I řekl Hospodin Gedeonovi: Příliš mnoho jest lidu s tebou, protož nedám Madianských v ruce jejich, aby se nechlubil Izrael proti mně, řka: Ruka má spomohla mi.
3 Tsono lengeza kwa anthu kuti, ‘Aliyense amene akuchita mantha ndi kunjenjemera abwerere kwawo, ndipo achoke kuno ku phiri la Giliyadi.’” Choncho anthu 22,000 anachoka, ndipo anatsalira anthu 10,000.
A protož provolej hned, ať slyší lid, a řekni: Kdo jest strašlivý a lekavý, navrať se zase, a odejdi ráno pryč k hoře Galád. I navrátilo se z lidu dvamecítma tisíců, a deset tisíc zůstalo.
4 Koma Yehova anawuza Gideoni kuti, “Anthuwa achulukabe. Uwatenge upite nawo ku mtsinje ndipo ndikawayesa kumeneko mʼmalo mwako. Ndikadzanena kuti, ‘Uyu apite nawe’ adzapita nawe; koma ndikanena kuti ‘Uyu asapite nawe,’ sadzapita nawe.”
Řekl opět Hospodin Gedeonovi: Ještě jest mnoho lidu; kaž jim sstoupiti k vodám, a tam jej tobě zkusím. I bude, že o komžkoli řeknu: Tento půjde s tebou, ten ať s tebou jde, a o komžkoli řeknu tobě: Tento nepůjde s tebou, ten ať nechodí.
5 Choncho Gideoni anatenga anthuwo ndi kupita nawo ku madzi. Kumeneko Yehova anamuwuza kuti, “Amene amwe madzi mokhathira ndi manja ngati galu uwayike pawokha, ndipo amene amwe atagwada pansi uwayikenso pawokha.”
I kázal sstoupiti lidu k vodám, a řekl Hospodin k Gedeonovi: Každého, kdož chlemtati bude jazykem svým z vody, jako chlemce pes, postavíš obzvláštně, tolikéž každého, kdož se přisehne na kolena svá ku pití.
6 Ndipo anthu 300 anamwa mokhathira, pamene ena onse anagwada pansi pakumwa.
I byl počet těch, kteříž chlemtali, rukama svýma k ústům svým vodu nosíce, tři sta mužů, ostatek pak všeho lidu sehnuli se na kolena svá ku pití vody.
7 Yehova anati kwa Gideoni, “Ndi anthu 300 amene anamwa madzi mokhathira ndi manja awo ndidzakupulumutsani ndipo ndidzapereka Amidiyani mʼmanja mwanu. Koma anthu ena onse apite ku nyumba kwawo.”
I řekl Hospodin Gedeonovi: Ve třech stech mužů, kteříž chlemtali, vysvobodím vás, a vydám Madianské v ruku tvou, ale ostatek všeho lidu nechť se vrátí, jeden každý k místu svému.
8 Choncho analola anthu ena onse kuti apite ku nyumba zawo kupatula anthu 300 osankhika aja. Iwowa anatenga zakudya ndi malipenga a anthuwo. Ndipo misasa ya ankhondo Amidiyani inali kumunsi kwa chigwa.
A protož nabral ten lid v ruce své potravy a trouby své; jiné pak muže Izraelské všecky propustil, jednoho každého do stanů jejich, toliko tři sta těch mužů zanechal při sobě. Vojska pak Madianských ležela pod ním v údolí.
9 Usiku umenewo Yehova anati kwa Gideoni, “Dzuka, pita kachite nkhondo ku misasayo, chifukwa ndayipereka mʼmanja mwako.
I stalo se, že noci té řekl jemu Hospodin: Vstana, sstup k vojsku, nebo dal jsem je v ruku tvou.
10 Ngati ukuopa, upite ku msasako ndi Pura wantchito wako,
Pakli nesmíš sjíti sám, sejdi s Půrou služebníkem svým do vojska,
11 ndipo ukamvere zimene akunena ndipo pambuyo pake udzalimba mtima ndi kupita kukayithira nkhondo misasayo.” Choncho iye ndi wantchito wake Pura anapita kumbali ina ya msasawo kumene kunali ankhondo.
A uslyšíš, co mluviti budou; i posilní se z toho ruce tvé, tak že směle půjdeš proti vojsku tomu. Sstoupil tedy on a Půra služebník jeho k kraji oděnců, kteříž byli v vojště.
12 Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena onse akummawa anadzaza chigwa chonse ngati dzombe. Ngamira zawo zinali zambiri zosawerengeka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
Madian pak a Amalech i všecken lid východní leželi v údolí, jako kobylky u velikém množství, ani velbloudů jejich počtu nebylo, jako písek, kterýž jest na břehu mořském v nesčíslném množství.
13 Gideoni atafika anangomva munthu wina akuwuza mnzake maloto ake kuti, “Ine ndinalota nditaona dengu la buledi wa barele likugubuduzika kupita ku misasa ya Amidiyani. Litafika linawomba tenti moti inagwa ndi kuphwasukaphwasuka.”
A když přišel Gedeon, aj, jeden vypravoval bližnímu svému sen, a řekl: Hle, zdálo mi se, že pecen chleba ječmenného valil se do vojska Madianského, a přivaliv se na každý stan, udeřil na něj, až padl, a podvrátil jej svrchu, a tak ležel každý stan.
14 Ndipo mnzakeyo anamuyankha kuti, “Iyi ndi nkhondo ya Gideoni mwana wa Yowasi, wa ku Israeli. Mulungu wapereka Amidiyani pamodzi ndi ankhondo ake onse mʼdzanja mwake.”
Jemužto odpovídaje bližní jeho, řekl: Není to nic jiného, jediné meč Gedeona syna Joasova, muže Izraelského; dalť jest Bůh v ruku jeho Madianské i všecka tato vojska.
15 Gideoni atamva za malotowo ndi kumasulira kwake, anapembedza Mulungu. Kenaka anabwerera ku msasa wa Israeli nawawuza kuti, “Dzukani popeza Yehova wapereka msasa wa Midiyani mʼmanja mwanu.”
Stalo se pak, že když uslyšel Gedeon vypravování snu i vyložení jeho, poklonil se Bohu, a vrátiv se k vojsku Izraelskému, řekl: Vstaňte, nebo dal Hospodin v ruku vaši vojska Madianská.
16 Anawagawa anthu 300 aja magulu atatu, nawapatsa malipenga mʼmanja mwawo ndi mbiya zimene mʼkati mwake munali nsakali zoyaka.
Rozdělil tedy tři sta mužů na tři houfy, a dal trouby v ruku každému z nich a báně prázdné, a v prostředku těch bání byly pochodně.
17 Anawuza anthuwo kuti, “Muzikayangʼana ine ndi kuchita zimene ndizikachita. Ndikakafika kumalire a msasa, mukachite zomwe ndikachita ine.
I řekl jim: Jakž na mně uzříte, tak učiníte; nebo hle, já vejdu na kraj vojska, a jakž já tehdáž budu dělati, tak uděláte.
18 Ndikadzaliza lipenga ndi onse amene ali ndi ine, inunso mukalize malipenga kumbali zonse za misasa yonse ndi kufuwula kuti, ‘Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.’”
Nebo troubiti budu já v troubu i všickni, jenž se mnou budou, tehdy vy také troubiti budete v trouby vůkol všeho vojska, a řeknete: Meč Hospodinův a Gedeonův.
19 Choncho Gideoni pamodzi ndi amuna 100 omwe anali nawo anafika ku malire a msasa pakati pa usiku, alonda atangosinthana kumene. Iwo analiza malipenga awo ndi kuphwanya mbiya zimene zinali mʼmanja mwawo.
Všel tedy Gedeon a sto mužů, kteříž s ním byli, na kraj vojska při začátku bdění prostředního, jen že byli proměnili stráž; i troubili v trouby, a roztřískali báně, kteréž měli v rukou svých.
20 Magulu awiri ena aja anayimbanso malipenga ndi kuswa mbiya zawo. Aliyense ananyamula nsakali ya moto ku dzanja lamanzere ndi lipenga ku dzanja lamanja ndipo anafuwula kuti, “Lupanga la Yehova ndi la Gideoni.”
Tedy ti tři houfové troubili v trouby, rozstřískavše báně, a drželi v ruce své levé pochodně, v pravé pak ruce své trouby, aby troubili, i křičeli: Meč Hospodinův a Gedeonův.
21 Aliyense anayima pa malo pake kuzungulira misasa. Ankhondo a mʼmisasa muja anadzuka nayamba kuthawa akufuwula.
A postavili se každý na místě svém vůkol ležení; i zděšena jsou všecka vojska, a křičíce, utíkali.
22 Anthu 300 aja ataliza malipenga, Yehova anawasokoneza ankhondo a Midiyani aja motero kuti ankamenyana okhaokha. Ankhondowo anathawira ku Beti-Sita cha ku Zerera mpaka ku malire a Abeli-Mehola pafupi ndi Tabati.
Když pak troubilo v trouby těch tři sta mužů, obrátil Hospodin meč jednoho proti druhému, a to po všem ležení. Utíkalo tedy vojsko až k Betseta do Zererat, a až ku pomezí Abelmehula u Tebat.
23 Aisraeli a fuko la Nafutali, fuko la Aseri, ndi fuko lonse la Manase anayitanidwa, ndipo iwo anathamangitsa Amidiyaniwo.
Shromáždivše se pak muži Izraelští z Neftalím a z Asser a ze všeho pokolení Manassesova, honili Madianské.
24 Gideoni anatumiza amithenga ku dziko lonse la ku mapiri la Efereimu kukanena kuti, “Tsikani mumenyane ndi Amidiyani ndipo mulande madooko awo owolokera mpaka ku Beti-Bara.” Choncho anthu onse a fuko la Efereimu anasonkhana ndipo analanda madooko awo owolokera mpaka ku Betibaala.
I rozeslal Gedeon posly na všecky hory Efraimské, řka: Vyjděte v cestu Madianským, a zastupte jim vody až k Betabaře a Jordánu. Tedy shromáždivše se všickni muži Efraim, zastoupili vody až k Betabaře a Jordánu.
25 Iwo anagwiranso atsogoleri awiri a nkhondo a Amidiyani, Orebu ndi Zeebu. Anapha Orebu ku thanthwe la Orebu, koma Zeebu anamuphera ku malo ofinyira mphesa ku Zeebu pothamangitsa Amidiyani. Mitu ya Orebu ndi Zeebu anabwera nayo kwa Gideoni kutsidya kwa Yorodani.
A chytili dvé knížat Madianských, Goréba a Zéba. I zabili Goréba na skále Goréb a Zéba zabili v lisu Zéb, a honili Madianské, hlavu pak Gorébovu a Zébovu přinesli k Gedeonovi za Jordán.