< Oweruza 6 >
1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Les enfants d'Israël firent ce qui est mal aux yeux de l'Éternel, et l'Éternel les livra entre les mains de Madian pendant sept ans.
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
La main de Madian l'emporta sur Israël, et les enfants d'Israël se firent, à cause de Madian, des repaires dans les montagnes, des cavernes et des forteresses.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
Lorsqu'Israël eut semé, les Madianites, les Amalécites et les fils de l'Orient montèrent contre eux.
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
Ils campèrent contre eux et détruisirent les produits de la terre, jusqu'à ce que tu arrives à Gaza. Ils ne laissèrent en Israël aucune subsistance, ni brebis, ni bœuf, ni âne.
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
Car ils sont montés avec leur bétail et leurs tentes. Ils sont entrés comme des sauterelles pour la multitude. Ils étaient innombrables, eux et leurs chameaux, et ils sont entrés dans le pays pour le détruire.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
Israël fut très humilié à cause de Madian, et les enfants d'Israël crièrent à l'Éternel.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
Lorsque les enfants d'Israël crièrent à Yahvé à cause de Madian,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
Yahvé envoya un prophète aux enfants d'Israël, qui leur dit: « Yahvé, le Dieu d'Israël, dit: Je vous ai fait monter d'Égypte et je vous ai fait sortir de la maison de servitude.
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
Je vous ai délivrés de la main des Égyptiens et de la main de tous ceux qui vous opprimaient, je les ai chassés devant vous et je vous ai donné leur pays.
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
Je t'ai dit: « Je suis Yahvé, ton Dieu. Tu ne craindras pas les dieux des Amoréens, dans le pays desquels tu habites. » Mais vous n'avez pas écouté ma voix.'"
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
L'ange de Yahvé vint s'asseoir sous le chêne qui était à Ophra, et qui appartenait à Joas, l'Abiézerite. Son fils Gédéon battait le blé dans le pressoir, pour le cacher aux Madianites.
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
L'ange de Yahvé lui apparut et lui dit: « Yahvé est avec toi, vaillant homme! »
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
Gédéon lui dit: « Oh, mon seigneur, si Yahvé est avec nous, pourquoi donc tout cela nous est-il arrivé? Où sont passées toutes les merveilles dont nos pères nous ont parlé, en disant: « Yahvé ne nous a-t-il pas fait monter d'Égypte? Mais maintenant, Yahvé nous a rejetés et nous a livrés entre les mains de Madian. »
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
L'Éternel le regarda et dit: « Va avec ta force, et sauve Israël de la main de Madian. Ne t'ai-je pas envoyé? »
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
Il lui dit: « Seigneur, comment sauverai-je Israël? Voici, ma famille est la plus pauvre de Manassé, et je suis le plus petit dans la maison de mon père. »
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
Yahvé lui dit: « Je serai avec toi, et tu frapperas les Madianites comme un seul homme. »
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
Il lui dit: « Si maintenant j'ai trouvé grâce à tes yeux, montre-moi un signe que c'est toi qui me parles.
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
Ne t'en va pas, je te prie, jusqu'à ce que je vienne à toi, que j'apporte mon cadeau et que je le dépose devant toi. » Il a dit: « Je vais attendre que tu reviennes. »
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
Gédéon entra et prépara un chevreau et des gâteaux sans levain d'un épha de farine. Il mit la viande dans un panier et il mit le bouillon dans un pot; il l'apporta sous le chêne et le présenta.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
L'ange de Dieu lui dit: « Prends la viande et les gâteaux sans levain, pose-les sur ce rocher, et verse le bouillon. » Il fit ainsi.
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
Et l'ange de Yahvé étendit l'extrémité du bâton qu'il avait à la main, et toucha la viande et les gâteaux sans levain; et le feu monta du rocher et consuma la viande et les gâteaux sans levain. Puis l'ange de Yahvé s'en alla hors de sa vue.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
Gédéon vit que c'était l'ange de Yahvé; et Gédéon dit: « Hélas, Seigneur Yahvé! Car j'ai vu l'ange de Yahvé face à face! »
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
Yahvé lui dit: « Que la paix soit avec toi! N'aie pas peur. Tu ne mourras pas. »
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
Et Gédéon y construisit un autel à Yahvé et l'appela « Yahvé est paix ». Aujourd'hui encore, il se trouve à Ophra, chez les Abiézrites.
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
Cette même nuit, Yahvé lui dit: « Prends le taureau de ton père, le second taureau âgé de sept ans, et jette l'autel de Baal que ton père a, et coupe l'ashère qui est à côté.
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
Puis tu construiras un autel à Yahvé, ton Dieu, sur le sommet de cette forteresse, de façon ordonnée, et tu prendras le second taureau, et tu offriras un holocauste avec le bois de l'ashère que tu abattras. »
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
Alors Gédéon prit dix hommes parmi ses serviteurs et fit ce que Yahvé lui avait dit. Comme il craignait la maison de son père et les hommes de la ville, il ne put le faire de jour, mais il le fit de nuit.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
Les gens de la ville se levèrent de bon matin, et voici, l'autel de Baal était démoli, l'idole d'Astarté qui était près de lui était coupée, et le second taureau était offert sur l'autel qui avait été bâti.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
Ils se dirent les uns aux autres: « Qui a fait cela? » Quand ils se sont renseignés et ont demandé, ils ont dit: « Gédéon, fils de Joash, a fait cette chose. »
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
Alors les gens de la ville dirent à Joas: « Fais sortir ton fils, et qu'il meure, parce qu'il a démoli l'autel de Baal et qu'il a abattu l'ashère qui était près de lui. »
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
Joas dit à tous ceux qui s'opposaient à lui: « Allez-vous lutter pour Baal? Ou le sauverez-vous? Que celui qui le défendra soit mis à mort dès demain matin! Si c'est un dieu, qu'il se défende lui-même, car on a démoli son autel! »
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
C'est pourquoi, ce jour-là, il lui donna le nom de Jerub-Baal, en disant: « Que Baal conteste contre lui, car il a démoli son autel. »
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
Et tous les Madianites et les Amalécites et les fils de l'Orient se rassemblèrent; et ils passèrent et campèrent dans la vallée de Jizréel.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
Mais l'Esprit de Yahvé vint sur Gédéon, et il sonna de la trompette; et Abiezer se rassembla pour le suivre.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
Il envoya des messagers dans tout Manassé, et eux aussi se rassemblèrent pour le suivre. Il envoya des messagers à Aser, à Zabulon et à Nephtali, et ils montèrent à leur rencontre.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
Gédéon dit à Dieu: « Si tu veux sauver Israël par ma main, comme tu l'as dit,
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
voici, je mettrai une toison de laine sur l'aire de battage. S'il y a de la rosée sur la toison seulement, et qu'il y ait du sec sur tout le sol, alors je saurai que tu sauveras Israël par ma main, comme tu l'as dit. »
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
Il en fut ainsi, car il se leva de bonne heure le lendemain, pressa la toison et en tira la rosée, une coupe pleine d'eau.
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
Gédéon dit à Dieu: « Que ta colère ne s'enflamme pas contre moi, et je ne parlerai que cette fois-ci. Laisse-moi, je t'en prie, faire l'épreuve de la toison pour cette fois seulement. Qu'il n'y ait de sec que sur la toison, et sur toute la terre, qu'il y ait de la rosée. »
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
Dieu fit ainsi cette nuit-là, car il faisait sec sur la toison seulement, et il y avait de la rosée sur toute la terre.