< Oweruza 6 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
And the sons of Israel did the thing that was wicked, in the sight of Yahweh, —so Yahweh delivered them into the hand of Midian seven years;
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
and the hand of Midian prevailed against Israel, —because of Midian, did the sons of Israel prepare for themselves the hollows which were in the mountains, and the caves, and the strongholds.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
And so it used to be, if Israel had sown, then came up Midian and Amalek and the sons of the east, yea came up against them,
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
and encamped against them, and destroyed the increase of the land, until thou comest unto Gaza, —neither left they sustenance in Israel, nor sheep nor ox, nor ass;
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
for, they with their cattle, used to come up, with their tents—yea they used to come like locusts, for multitude, both they and their cattle, were without number, —so they came into the land, to lay it waste.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
Thus was Israel greatly impoverished, because of Midian, —and the sons of Israel made outcry unto Yahweh.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
And it came to pass, when the sons of Israel cried unto Yahweh, —on account of Midian,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
then sent Yahweh a prophet unto the sons of Israel, —who said unto them—Thus, saith Yahweh, God of Israel, I, led you up out of Egypt, and brought you forth out of the house of servants;
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
Yea I rescued you out of the hand of Egypt, and out of the hand of all who oppressed you, —that I might drive them out from before you, and I gave unto you their land;
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
Yea and I said to you, —I, Yahweh, am your God, Ye must not fear the gods of the Amorites, in whose land ye are about to dwell, —But ye have not hearkened unto my voice.
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
Then came the messenger of Yahweh, and sat down under the oak which was in Ophrah, which belonged to Joash, the Abiezrite; and, Gideon his son, was beating out wheat in the winepress, to escape the notice of the Midianites;
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
so the messenger of Yahweh appeared unto him, —and said unto him, Yahweh, is with thee, thou mighty man of valour!
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
And Gideon said unto him—Pardon, my lord! if Yahweh be with us, then wherefore hath all this befallen us? and where are all his wonders, which our fathers have recounted to us—saying, Was it not, out of Egypt, that Yahweh brought us up? But, now, hath Yahweh abandoned us, and delivered us into the hand of Midian.
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
And Yahweh, turned unto him, and said—Go in this thy might, and thou shalt save Israel, out of the hand of Midian, —have I not sent thee?
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
And he said unto him—Pardon, O my Lord! How, shall I save Israel? Lo! my thousand, is the poorest in Manasseh, and, I, am the youngest in the house of my father.
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
And Yahweh said unto him—I will be with thee, —so shalt thou smite the Midianites, as one man.
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
And he said unto him, If, I beseech thee, I have found favour in thine eyes, then wilt thou work for me a sign, that it is, thou, who art speaking with me.
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
Do not, I beseech thee, withdraw from hence, until I come unto thee, and bring forth my present, and set it before thee. And he said: I, will tarry until thou return.
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
So, Gideon, went in, and made ready a kid of the goats, and, of an ephah of meal, unleavened cakes, the flesh, he put in a basket, and, the broth, he put in a pot, —and brought them forth unto him, under the oak, and presented them.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
And the messenger of God said unto him—Take the flesh and the cakes, and set them on this crag, and, the broth, do thou pour out. And he did so.
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
Then the messenger of Yahweh put forth the end of the staff, that was in his hand, and touched the flesh, and the cakes, —and there came up fire out of the rock, and consumed the flesh, and the cakes, and, the messenger of Yahweh, had departed out of his sight.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
Then saw Gideon that, the messenger of Yahweh, it was, —so Gideon said—Alas, My Lord Yahweh! forasmuch as I have seen the messenger of Yahweh, face to face!
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
And Yahweh said unto him—Peace be unto thee! Do not fear, —thou shalt not die.
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
So Gideon built there an altar unto Yahweh, and called it, Yahweh-shalom. Unto this day, it remaineth, in Ophrah of the Abiezrites.
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
And it came to pass, on that night, that Yahweh said unto him—Take the young bullock that belongeth to thy father, even the second bullock of seven years, —and throw thou down the altar of Baal, that belongeth to thy father, and, the sacred stem that is by it, shalt thou cut down.
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
Then shalt thou build an altar, unto Yahweh thy God, on the top of this fort, with the pile, —and shalt take the second bullock, and cause it to go up as an ascending-sacrifice, with the wood of the sacred stem which thou shalt cut down.
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
So Gideon took ten men from among his servants, and did as Yahweh had spoken unto him, —and so it was that, as he too much feared the house of his father, and the men of the city, to do it by day, he did it by night.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
And the men of the city rose up early in the morning, and lo! the altar of Baal, had been overthrown, and, the sacred stem that was by it, had been cut down, and the second bullock had been caused to ascend upon the altar that had been built.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
So they said, one to another, Who hath done this thing? And they inquired, and made search, and it was said, Gideon son of Joash, hath done this thing.
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
So the men of the city said unto Joash, Bring forth thy son, that he may die, —because he hath overthrown the altar of Baal, and because he hath cut down the sacred stem that was by it.
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
And Joash said unto all who stood by him—Will, ye, plead for Baal, or will, ye, save him? Whoso pleadeth for him, let him be put to death while it is yet morning, —if, a god, he be let him plead for himself, because one hath overthrown his altar.
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
So he was called on that day, Jerubbaal, saying, —Let Baal, plead against him. Because he had overthrown his altar.
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
Now, all the Midianites and the Amalekites and the sons of the east, were gathered together, —and they crossed over and pitched in the vale of Jezreel.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
But, the spirit of Yahweh, clothed Gideon, —so he blew with a horn, and Abiezer was gathered after him.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
Messengers also, sent he throughout all Manasseh, and, they also, were gathered after him, —messengers also, sent he throughout Asher, and throughout Zebulun, and throughout Naphtali, and they came up to meet them.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
And Gideon said unto God, —If thou art about to bring salvation, by my hand, unto Israel, as thou hast spoken,
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
lo! I am placing a woollen fleece, on the threshing-floor, —if, dew, be on the fleece alone and, on all the ground, it be dry, then shall I know that thou wilt bring salvation, by my hand, unto Israel, as thou hast spoken.
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
And it was so, and he rose up early, on the morrow, and pressed together the fleece, —and wrung out the dew from the fleece, a small bowl full of water.
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
Then said Gideon unto God, Let not thine anger kindle upon me, but let me speak, only this once, —Let me, I pray thee, put to the proof, only this once, with the fleece, I pray thee, let it be dry on the fleece alone, while, on all the ground, there be dew.
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
And God did so on that night, —and it was dry on the fleece alone, while, on all the ground, there was dew.

< Oweruza 6 >