< Oweruza 6 >
1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
And the children of Israel did the evil in the eyes of the Lord: and the Lord delivered them into the hand of Midian seven years.
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
And the hand of Midian prevailed over Israel; and because of the Midianites the children of Israel made for themselves the passes which are in the mountains, and the caves, and the strongholds.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
And it was, when Israel had sown, that the Midianites came up, and the 'Amalekites, and the children of the east, and they went up against them;
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
And they encamped against them, and destroyed the products of the earth, as far as Gazzah, and they left no sustenance for Israel, neither lamb, nor ox, nor ass.
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
For they came up with their cattle and their tents, and came as locusts in multitude; and both they and their camels were without number; and they came into the land to destroy it.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
And Israel was greatly impoverished because of the Midianites; and the children of Israel cried unto the Lord.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
And it came to pass, when the children of Israel had cried unto the Lord because of the Midianites,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
That the Lord sent a prophet unto the children of Israel, and he said unto them, Thus hath said the Lord the God of Israel, I led you forth out of Egypt, and brought you out of the house of slavery;
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
And I delivered you out of the hand of the Egyptians, and out of the hand of all that oppressed you, and I drove them out from before you, and gave you their land;
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
And I said unto you, I am the Lord your God: ye shall not fear the gods of the Emorites, in whose land ye dwell; but ye have not obeyed my voice.
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
And there came an angel of the Lord, and sat down under the oak which was in 'Ophrah, that pertained unto Joash the Abi'ezrite; and Gid'on his son was beating out wheat in the wine-press, to hide it from the Midianites.
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
And the angel of the Lord appeared unto him, and said unto him, The Lord is with thee, thou mighty man of valor.
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
And Gid'on said unto him, Pardon, my lord, if the Lord be indeed with us, why then hath all this befallen us? and where are all his wonders of which our fathers have told us, saying, Did not the Lord bring us up from Egypt! But now the Lord hath forsaken us, and delivered us into the hand of Midian.
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
And the Lord turned toward him, and said, Go in this thy might, and thou shalt save Israel from the hand of the Midianites: behold, I have sent thee.
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
And he said unto him, Pardon my Lord, wherewith shall I save Israel? behold, my family is the weakest in Menasseh, and I am the youngest of my father's house.
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
And the Lord said unto him, Because I will be with thee, and thou shalt smite the Midianites as one man.
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
And he said unto him, If now I have found grace in thy eyes, then give me a sign that thou hast been speaking with me;
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
Depart not hence, I pray thee, until I come unto thee, and bring forth my present, and set it before thee. And he said, I will tarry until thy return.
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
And Gid'on went in, and made ready a kid, and unleavened cakes of an ephah of flour: the flesh he put in a basket, and the broth he put in a pot, and brought it out unto him under the oak, and presented it.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
And the angel of God said unto him, Take the flesh and the unleavened cakes, and lay them upon this rock, and the broth pour out. And he did so.
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
Then the angel of the Lord put forth the end of the staff that was in his hand, and touched the flesh and the unleavened cakes; and there rose up fire out of the rock, and consumed the flesh and the unleavened cakes. And the angel of the Lord departed out of his sight.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
And when Gid'on perceived that it was an angel of the Lord, Gid'on said, Alas, O Lord Eternal! because I have surely seen an angel of the Lord face to face.
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
And the Lord said unto him, Peace be unto thee; fear not: thou shalt not die.
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
And Gid'on built there an altar unto the Lord, and called it Adonay-shalom [[the Eternal of Peace: ]] unto this day it is yet in Ophrah of the Abi'ezrites.
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
And it came to pass in the same night, that the Lord said unto him, Take thy father's young bullock, and the second bullock of seven years old, and throw down the altar of Baal which belongeth to thy father, and the grove that is around it shalt thou cut down.
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
And build an altar unto the Lord thy God upon the top of this rock, on the level place, and take the second bullock, and offer [it as] a burnt-sacrifice with the wood of the grove which thou shalt cut down.
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
And Gid'on took ten men of his servants, and did as the Lord had spoken unto him; but it came to pass, because he feared his father's household, and the men of the city, to do it by day, that he did it by night.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
And when the men of the city arose early in the morning, behold, the altar of Baal was overthrown, and the grove that was around it was cut down, and the second bullock was offered upon the altar which had been built.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
And they said one to another, Who hath done this thing? And they inquired and searched, and then said, Gid'on the son of Joash hath done this thing.
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
Thereupon said the men of the city unto Joash, Bring out thy son, that he may die; because he hath overthrown the altar of Baal, and because he hath cut down the grove that was around it.
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
But Joash said unto all that stood around him, Will ye indeed contend for Baal? will ye assist him? he that will contend for him, shall be put to death; [wait] until morning: if he be a god, let him contend for himself, because one hath overthrown his altar.
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
And the people called him on that day Yerubba'al, saying, Let Baal contend against him, because he hath overthrown his altar.
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
And all the Midianites and 'Amalekites and the children of the east assembled together, and went over and encamped in the valley of Yizre'el.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
But the Spirit of the Lord endued Gid'on, and he blew the cornet: and Abi'ezer assembled and followed him.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
And he sent messengers throughout all Menasseh, who also assembled and followed him; and he sent messengers through Asher, and through Zebulun, and through Naphtali, and they came up to meet them.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
And Gid'on said unto God, If thou wilt save Israel by my hand, as thou hast spoken,
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
Behold, I set up this fleece of wool in the threshing floor: if now there be dew on the fleece alone, and it be dry upon all the ground, then shall I know that thou wilt save Israel by my hand, as thou hast spoken.
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
And it was so; and when he rose up early on the morrow, he squeezed the fleece together, and wrung dew out of the fleece, [making] a bowl full of water.
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
And Gid'on said unto God, Let not thy anger be kindled against me, and I will speak but this once [more]; let me have a proof, I pray thee, but this once more with the fleece; let it, I pray, be dry upon the fleece alone, and upon all the ground let there be dew.
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
And God did so that night; and it was dry upon the fleece alone, and on all the ground there was dew.