< Oweruza 6 >

1 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova, choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Amidiyani kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
И Израилтяните сториха зло пред Господа; и Господ ги предаде в ръката на Мадиама за седем години.
2 Amidiyani anapondereza Aisraeli. Tsono chifukwa cha Amidiyaniwa, Aisraeli anakonza malo obisalamo mʼmapiri ndi mʼmapanga. Anamanganso malinga.
И ръката на Мадиама преодоля над Израиля; и поради мадиамците, израилтяните си направиха ония ровове, които са по горите, и пещерите и укрепленията.
3 Aisraeli amati akadzala mbewu, Amidiyani, Aamaleki ndi anthu ena akummawa amabwera ndi kudzawathira nkhondo.
И след като Израил посееше, мадиамците, амаличаните и източните жители дохождаха и нападаха против него;
4 Iwo anamanga misasa mʼdzikomo ndi kuwononga zokolola zawo zonse mpaka ku Gaza, ndipo sanawasiyireko chamoyo chilichonse Aisraeliwo, kaya nkhosa kapena ngʼombe ndi bulu yemwe.
и, като разполагаха стан против тях, унищожаваха рожбите на земята чак до Газа, и не оставяха храна за Израиля, нито овца, нито говедо, нито осел.
5 Iwo ankabwera ndi zoweta zawo ndi matenti awo omwe. Ankabwera ambiri ngati dzombe, motero kuti kunali kovuta kuwawerenga anthuwo ndi ngamira zawo. Tsono iwo ankabwera ndi kuwononga dziko lonse.
Защото дохождаха с добитъка си и с шатрите си, и влизаха в страната многобройни като скакалци; безбройни бяха и те и камилите им, и навлизаха в земята, за да я опустошават.
6 Aisraeli anasauka chifukwa cha Amidiyani ndipo analirira kwa Yehova kuti awathandize.
Така Израил изпадна в голямо униние поради мадиамците; затова, израилтяните извикаха към Господа.
7 Pamene Aisraeli analirira kwa Yehova chifukwa cha Amidiyaniwo,
И когато израилтяните извикаха към Господа поради мадиамците,
8 Iye anawatumizira mneneri amene anati, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndine amene ndinakutsogolerani kuchokera ku Igupto. Ndinakutulutsani mʼdziko la ukapolo.
тогава Господ изпрати на израилтяните един пророк, който им каза: Така говори Господ Израилевият Бог: Аз ви изведох от Египет, и ви изведох от дома на робството;
9 Ine ndinakupulumutsani ku ulamuliro wa Igupto komanso mʼmanja mwa amene amakuzunzani. Ndinawathamangitsa adani anu inu mukufika, ndikukupatsani dziko lawo.’
И избавих ви от ръката на египтяните и от ръката на всички, които ви насилваха, и като ги изпъдих от пред вас, дадох ви земята им.
10 Ndipo ndinakuwuzani kuti, ‘Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musapembedze Milungu ya Aamori amene mukukhala mʼdziko lawo.’ Koma inu simunandimvere.”
И рекох ви: Аз съм Господ вашият Бог; да не почитате боговете на аморейците, в чиято земя живеете. Обаче вие не послушахте гласа Ми.
11 Tsiku lina mngelo wa Yehova anabwera ku Ofura ndi kukhala pansi pa tsinde pa mtengo wa thundu umene unali wa Yowasi Mwabiezeri. Tsono Gideoni, mwana wake nʼkuti pa nthawiyo akupuntha tirigu mʼmalo ofinyira mphesa mowabisalira Amidiyani.
И ангелът Господен дойде та седна под дъба, който е в Офра, и принадлежеше на авиезереца Иоас; а син му Гедеон чукаше жито в лина, за да го скрие от мадиамците.
12 Tsono mngelo wa Yehova uja anamuonekera Gideoni nati kwa iye, “Yehova ali nawe, iwe munthu wamphamvu ndi wolimba mtima.”
И ангелът Господен му се яви и му каза: Господ е с тебе, мъжо силни и храбри.
13 Gideoni anayankha, “Koma mbuye wanga, ngati Yehova ali nafedi, nʼchifukwa chiyani zonsezi zationekera? Nanga ntchito zake zodabwitsa zimene makolo athu anatiwuza pamene anati, ‘Yehova anatitulutsa ku dziko la Igupto,’ zili kuti? Koma tsopano Yehova watitaya ndi kutipereka mʼmanja mwa Amidiyani.”
А Гедеон ме рече: О господине, ако Господ е с нас, то защо ни постигна всичко това? и къде са всичките Му чудеса, за които бащите ни ни разказваха, като думаха: Не изведе ли ни Господ от Египет? Но сега Господ ни е оставил и ни е предел в ръката на мадиамците.
14 Yehova anamuyangʼana namuwuza kuti, “Pita ndi mphamvu zomwe uli nazo, ukapulumutse Aisraeli mʼmanja mwa Amidiyani. Kodi si ndine amene ndakutuma?”
И Господ погледна към него и му каза: Иди с тая твоя сила, и ще освободиш Израиля от ръката на мадиамците; не те ли изпратих Аз?
15 Koma Gideoni anafunsa kuti, “Kodi Ambuye anga ine ndingapulumutse bwanji Israeli? Mbumba yanga ndi yopanda mphamvu mu fuko la Manase, ndiponso ine ndine wamngʼono kwambiri mʼbanja mwa abambo anga.”
А той Му рече: О Господи! с какво ще освобадя аз Израиля? Ето, моето семейство е най-долно между Манасия, и аз съм най-малък в бащиния си дом.
16 Yehova anamuyankha kuti, “Ine ndidzakhala nawe, ndipo Amidiyaniwo udzawagonjetsa ngati munthu mmodzi.”
Но Господ му рече: Непременно Аз ще бъда с тебе; и ти ще поразиш мадиамците като един човек.
17 Gideoni anati, “Ngati tsopano mwandikomera mtima, ndionetseni chizindikiro kusonyeza kuti ndinudi mukuyankhula ndi ine.
Сетне той му каза: Моля Ти се, ако съм придобил Твоето благоволение, покажи ми знамение, за да зная Кой си Ти, Който говориш с мене;
18 Chonde musachoke msanga mpaka nditabwerera kwa inu ndi chopereka changa cha chakudya kudzachipereka kwa inu.” Ndipo Yehova anamuwuza kuti, “Ine ndikudikira mpaka utabweranso.”
моля Ти се, не си отивай от тук, докато не дойда при Тебе и изнеса приноса си и го положа пред Тебе. И Той ме рече: Ще чакам догдето се върнеш.
19 Gideoni analowa mʼnyumba, ndipo anakakonza mwana wambuzi, nakonzanso makeke wopanda yisiti a ufa wa makilogalamu khumi. Nayika nyamayo mʼdengu ndipo msuzi wake anawuthira mu mʼphika. Anabwera nazo ndi kukazipereka kwa mngelo uja pa tsinde pa mtengo wa thundu paja.
Тогава Гедеон слезе та приготви яре и пресни пити от една ефа брашно; месото тури в кошница, а чорбата тури в гърне, и изнесе ги вън при него под дъба, та го представи.
20 Mngelo wa Mulungu anamuwuza iye kuti, “Tenga nyamayi pamodzi ndi makekewa, uziyike pa mwala uwu ndi kuthirapo msuziwu.” Ndipo Gideoni anatero.
И ангелът Божия му каза: Вземи месото и пресните пити та ги сложи на тоя камък, а чорбата излей. И стори така.
21 Mngelo wa Yehova anatenga msonga ya ndodo imene inali mʼmanja mwake nakhudza nayo nyama ndi makeke aja. Nthawi yomweyo moto unabuka pa thanthwepo ndi kupsereza nyama yonse ndi makeke aja. Ndipo mngelo wa Yehova sanaonekenso.
Тогава ангелът Господен простря края на жезъла, който беше в ръката му, та досегна месото и пресните пити; и излезе огън из камъка та пояде месото и пресните пити; а след това ангелът Господен си отиде отпред очите му.
22 Apo Gideoni anazindikira kuti analidi mngelo wa Ambuye, ndipo anati, “Kalanga ine Yehova Wamphamvuzonse! Ine ndaona mngelo wa Yehova ndi maso!”
И като видя Гедеон, че това бе ангел Господен, Гедеон каза: Горко ми, Господи Иеова! защото видях ангела Господен лице с лице.
23 Koma Yehova anamuwuza kuti, “Mtendere ukhale ndi iwe! Usachite mantha, sufa ayi.”
А Господ му каза: Мир на тебе, не бой се; няма да умреш.
24 Choncho Gideoni anamanga guwa lansembe la Yehova pamenepo ndipo analitcha kuti, Yehova ndiye mtendere. Kufikira lero lino guwali lilipo ku Ofura wa Mwabiezeri.
И Гедеон издигна там олтар на Господа и нараче го Иеовашалом; той е до днес в Офра на авиезерците.
25 Usiku womwewo Yehova anati kwa Gideoni, “Tenga ngʼombe ya mphongo ya abambo ako, ngʼombe ina yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri ndipo ugwetse guwa la Baala limene abambo ako ali nalo, ndi kugwetsanso fano la Asera limene lili pafupi pake.
И в същата нощ Господ му каза: Вземи бащиния си вол, втория вол седемгодишния, та съсипи Вааловия жертвеник, който се намира у баща ти, и съсечи ашерата, която е при него.
26 Kenaka umangire Yehova Mulungu wako guwa lansembe ndi miyala yoyala bwino pamwamba pa chiwunda chimenecho. Utenge ngʼombe ya mphongo yachiwiri ija ndipo uyipereke ngati nsembe yopsereza pogwiritsa ntchito mitengo ya fano la Asera imene udule ngati nkhunizo.”
После на върха на тая скала издигни олтар на Господа твоя Бог, според наредбата, и вземи втория вол та го принеси за всеизгаряне с дървата на ашерата, която ще съсечеш.
27 Choncho Gideoni anatenga antchito ake khumi nachita monga Yehova anamuwuzira. Ndipo popeza ankaopa anthu a pa banja lake ndiponso anthu a mʼmudzimo sanachite zimenezi masana koma usiku.
И тъй, Гедеон взе десетина души от слугите си та стори както Господ му каза; а, понеже се боеше от бащиния си дом и от градските жители, затова не го стори денем, но го стори нощем.
28 Anthu a mu mzindamo atadzuka mʼmamawa anangoona guwa la Baala litagwetsedwa ndi fano la Asera limene linali pamwamba pake litadulidwa ndiponso ngʼombe yamphongo yachiwiri ija itaperekedwa ngati nsembe yopsereza pa guwa limene linamangidwa lija.
А когато градските жители станаха на утринта, ето, Вааловият жертвеник беше съборен, и ашерата, която беше при него, съсечена, и вторият вол цял изгорен на издигнатия олтар.
29 Iwo anafunsana wina ndi mnzake, “Wachita zimenezi ndani?” Atafufuza ndi kufunsafunsa, analingalira kuti, “Gideoni mwana wa Yowasi ndiye wachita zimenezi.”
И казаха си един на друг: Кой е извършил тая работа? И като разпитаха и издириха, рекоха: Гедеон Иоасовият син е извършил тая работа.
30 Ndipo anthuwo anawuza Yowasi kuti, “Tulutsa mwana wako, ayenera kufa chifukwa wagumula guwa lansembe la Baala ndipo wadula fano la Asera lomwe linali pamwamba pake.”
Тогава градските жители казаха на Иоаса: Изведете сина си да се умъртви, понеже той е съборил Вааловия жертвеник, и понеже е съсякъл ашерата, която беше при него.
31 Koma Yowasi anawuza anthu amene anamuzungulirawo kuti, “Kodi inu mukuti mukhale woyankhulira Baala mlandu? Kodi ndinu amene mukuti mumupulumutse? Amene akufuna kumumenyera nkhondo Baala akhala atafa pofika mmawa! Ngati Baalayo ndi mulungudi, musiyeni adzimenyere yekha nkhondo popeza munthu wina wamugwetsera guwa lansembe lake.”
А Иоас рече на всички, които бяха се дигнали против него: Вие ли ще защитите делото на Ваала? или вие ще го спасите? Който защити неговото дело, нека бъде умъртвен докато е още заран. Ако той е бог, нека сам защити делото си, като са съборили жертвеника му
32 Choncho tsiku limenelo Gideoni anatchedwa, Yeru-Baala, kutanthauza kuti, “Baala alimbana naye, popeza anagwetsa guwa lake la nsembe.”
За това в същия ден той нарече сина си Ероваал, като казваше: Нека се съди Ваал с него, като е съборил жертвеника му.
33 Tsopano Amidiyani, Amaleki ndi anthu ena akummawa anasonkhana ndipo atawoloka Yorodani anakamanga zinthando za nkhondo ku chigwa cha Yezireeli.
Тогава всичките мадиамци и амаличани и източните жители се събраха заедно та преминаха и разположиха стан в долината Езраел.
34 Ndipo Mzimu wa Yehova unatsikira pa Gideoni, ndipo anayimba lipenga kuyitana Abiezeri kuti amutsatire iye.
А Господният Дух дойде на Гедеона, и той засвири с тръба; и авиезерците се събраха да го последват.
35 Iye anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Manase kuti akamenye nkhondo ndipo Amanase anayitanidwanso kuti amutsate. Anatumanso amithenga kwa Aseri, Azebuloni ndi Anafutali, ndipo onsewo anapita kukakumana naye.
После изпрати вестители до целия Манасия, та и той се събра да го последва; прати вестители и до Асира, до Завулона и до Нефталима, а те дойдоха та ги посрещнаха.
36 Gideoni anati kwa Mulungu, “Ngati mudzapulumutsa Israeli ndi dzanja langa monga mwalonjezeramu,
И Гедеон рече на Бога: Ако искаш да освободиш Израиля с моята ръка, според както си казал.
37 onani, ine ndiyala ubweya wankhosa pa malo opunthira tirigu. Ngati mame adzagwera pa ubweya wankhosa pokhapa, pa nthaka ponse pakhala powuma, ndiye ndidziwa kuti mudzapulumutsadi Israeli ndi dzanja langa monga mwanenera.”
ето, аз ще туря руно вълна на гумното; ако падне роса само на руното, а цялата почва остане суха, тогаз ще позная, че ще освободиш Израиля с моята ръка, според както си казал.
38 Ndipo zimenezi zinachitikadi. Gideoni atadzuka mʼmamawa ndi kuwufinya ubweya uja, anafinya madzi odzaza mtsuko.
Така биде; защото, като стана рано на утринта, той изстиска руното, и роса потече из руното, пълен леген вода.
39 Kenaka Gideoni anati kwa Mulungu, “Musandikwiyire. Mundilole ndiyankhule kamodzi kokhaka. Ndiyeseko kamodzi kokha ndi ubweyawu kuti pa ubweya pokhapa pakhale powuma koma pa nthaka ponse pakhale ponyowa ndi mame.”
И Гедеон рече на Бога: Да не пламне гневът Ти против мене, и аз ще продумам само тоя път; да опитам моля Ти се, само тоя път с руното: сега нека остане сухо само руното, а по цялата почва нека падне роса.
40 Ndipo Mulungu anachita zomwezo usiku umenewo. Pa ubweya pokha panali powuma, koma pa nthaka ponse panagwa mame.
И Бог стори така през оная нощ: само руното остана сухо, а по цялата почва падна роса.

< Oweruza 6 >