< Oweruza 5 >

1 “Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
UDebora loBaraki indodana kaAbinowama basebehlabela ngalolosuku besithi:
2 “Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
Ngenxa yokuphindisela kwezimpindiselo koIsrayeli, nxa abantu bezinikela ngokuzithandela, busisani iNkosi!
3 “Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
Zwanini makhosi, libeke indlebe ziphathamandla, mina, mina ngizahlabela eNkosini, ngihubele iNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
4 “Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
Nkosi, ekuphumeni kwakho eSeyiri, ekunyatheleni kwakho usuka ensimini yeEdoma, umhlaba wazamazama, lamazulu athonta, lamayezi athontisa amanzi.
5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
Izintaba zageleza phambi kweNkosi, iSinayi le phambi kweNkosi, uNkulunkulu kaIsrayeli.
6 “Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Ensukwini zikaShamigari indodana kaAnathi, ensukwini zikaJayeli, izindlela zaphela, lababehamba ezindledlaneni bahamba ngezindlela ezimazombazombe.
7 Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
Izakhamizi zemakhaya zaphela koIsrayeli, zaphela, ngaze ngasukuma mina Debora, ngasukuma, unina koIsrayeli.
8 Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Wakhetha onkulunkulu abatsha, khona kwaba lempi emasangweni. Sabonwa yini isihlangu lomkhonto phakathi kwabazinkulungwane ezingamatshumi amane koIsrayeli?
9 Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
Inhliziyo yami ikubanikimithetho bakoIsrayeli, abazinikela ngokuzithandela phakathi kwabantu. Busisani iNkosi!
10 “Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
Bagadi babobabhemi abamhlophe, bahlali besigcabha, labahambi endleleni, khulumani.
11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
Elizwini labatshoki, phakathi kwezindawo zokukha amanzi, lapho bayalandisa ngemisebenzi elungileyo yeNkosi, imisebenzi elungileyo yezakhamizi zemakhaya zakoIsrayeli. Ngalesosikhathi abantu beNkosi behlela emasangweni.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
Vuka, vuka, Debora! Vuka, vuka, khuluma ingoma! Sukuma Baraki, uthumbe abathunjiweyo bakho, ndodana kaAbinowama.
13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
Khona yayenza insali yabusa phezu kwezinduna ebantwini; iNkosi yangenza ngabusa phezu kwabalamandla.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
Kuvela koEfrayimi impande yabo yayimelene loAmaleki; emva kwakho, Bhenjamini, phakathi kwabantu bakho; kuvela kuMakiri kwehla abanikumthetho, lakoZebuluni abadonsa ngentonga yombhali.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
Leziphathamandla zakoIsakari zaziloDebora; lanjengoIsakari, waba njalo uBaraki; wathunjwa esigodini ngenyawo zakhe. Ekwehlukaneni kukaRubeni izinqumo zenhliziyo zazizinkulu.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
Wahlalelani phakathi kwezibaya ukuzwa umhlanga wokukhaliselwa izimvu? Izifunda zakoRubeni zaba lokuhlolwa okukhulu kwenhliziyo.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
UGileyadi wahlala ngaphetsheya kweJordani. LoDani wahlalelani emikhunjini? UAsheri wahlala ekhunjini lolwandle, wahlala ethekwini.
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
UZebuluni uyisizwe esadela umphefumulo waso kwaze kwaba sekufeni, loNafithali, emiqolweni yensimu.
19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
Amakhosi afika alwa; khona amakhosi eKhanani alwa eThahanakhi ngasemanzini eMegido; kawathathanga impango yesiliva.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
Zisemazulwini zalwa, inkanyezi zisendleleni zazo zalwa loSisera.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
Isifula iKishoni sabakhukhula, isifula sendulo, isifula iKishoni. Mphefumulo wami, unyathela ngamandla!
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
Khona atshaya phansi amasondo amabhiza, ngokumatha, ukumatha kwabalamandla bakhe.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
Qalekisani iMerozi, kutsho ingilosi yeNkosi, qalekisani ngokuqalekisa abakhileyo kuyo, ngoba kabezanga kuncedo lweNkosi, kuncedo lweNkosi, lamaqhawe.
24 “Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
Uzabusiswa phezu kwabesifazana uJayeli umkaHeberi umKeni; ubusisiwe phezu kwabesifazana ethenteni.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
Wacela amanzi, wamnika uchago, waletha amasi ngomganu wobukhosi.
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
Welulela isandla sakhe esikhonkwaneni, lesandla sakhe sokunene esandweni sezisebenzi, wamtshaya uSisera, wachoboza ikhanda lakhe, wahlaba wabhoboza inhlafuno yakhe.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
Phakathi laphakathi kwenyawo zakhe wakhothama wawa walala; phakathi laphakathi kwenyawo zakhe wakhothama wawa, lapho akhothamela khona, wawa lapho efile echithekile.
28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
Unina kaSisera walunguza ngewindi, wanqolonga ngeminxibo yewindi wathi: Kungani inqola yakhe iphuza ukuza? Kungani ephuzile amavili ezinqola zakhe?
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
Izihlakaniphi zamakhosazana akhe zaphendula, yebo yena wazibuyisela impendulo yakhe wathi:
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
Kabatholanga yini bayaba impango, intombazana, amantombazana amabili kuleyo laleyondoda, impango yamalembu aconjiweyo kaSisera, impango yamalembu aconjiweyo afekethisiweyo ngenalithi, amalembu amabili aconjiweyo afekethisiweyo ngenalithi, awentamo zomphangi?
31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.
Ngokunjalo kazibhubhe zonke izitha zakho, Nkosi. Kodwa abayithandayo kababe njengokuphuma kwelanga ngamandla alo. Lelizwe lathula iminyaka engamatshumi amane.

< Oweruza 5 >