< Oweruza 5 >

1 “Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
Tad Debora un Baraks, Abinoama, dēls, tai dienā dziedāja un sacīja:
2 “Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
Ka Israēla varenie spēcīgi rādījušies, ka ļaudis labprātīgi cēlušies, teiciet To Kungu!
3 “Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
Klausāties, ķēniņi, ņemiet vērā, lielie kungi! Tam Kungam es dziedāšu, Tam Kungam, Israēla Dievam, es dziedāšu dziesmas.
4 “Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
Kungs, kad Tu izgāji no Seīra un atnāci no Edoma lauka, tad zeme drebēja, un debesis pilēja, un padebeši pilēja ar ūdeni.
5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
Kalni izkusa Tā Kunga priekšā, pats Sinaī Tā Kunga, Israēla Dieva, priekšā.
6 “Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
Zamgara, Anata dēla, dienās, Jaēles dienās, ceļi bija klusi, un ceļa ļaudis gāja aplinkus.
7 Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
Klusi bija ciemi iekš Israēla, tie bija klusi, kamēr es, Debora, cēlos, kamēr es cēlos, māte iekš Israēla.
8 Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Jaunus dievus izredzējās, tad radās karš vārtos. Vai gan redzēja bruņas, vai šķēpus pie četrdesmit tūkstošiem iekš Israēla?
9 Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
Mana sirds pieder Israēla valdniekiem, tiem ļaudīm, kas labprātīgi cēlušies. Teiciet To Kungu!
10 “Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
Kas jājat uz baltām ēzelienēm, kas sēžat uz audumiem, kas staigājat pa ceļu, dziedājiet!
11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
Kur strēlnieku balss skanēja pie ūdens akām, tur slavē Tā Kunga taisnos darbus, tos taisnos darbus pie Viņa ciemiem iekš Israēla. Tad Tā Kunga ļaudis pārgāja savos vārtos.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
Modies, modies, Debora! modies, modies, dziedi dziesmu! Celies, Barak, un ved savus gūstītos, Abinoama dēls.
13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
Tad nonāca atlikums no tiem tautas vareniem; Tas Kungs nonāca man līdz starp tiem spēcīgiem.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
No Efraīma tie, kam sakne ir iekš Amaleka, aiz tevis Benjamins starp taviem ļaudīm; no Mahira valdnieki nāca un no Zebulona, kas tur (nes) vadoņa zizli.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
Un Īsašara virsnieki bija ar Deboru, un Īsašars tā kā Baraks, lejā nesti savām kājām. Pie Rūbena upēm bija lieli sirds padomi.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
Kāpēc tu paliki pie laidariem, klausīties stabules pie ganāmiem pulkiem? Pie Rūbena upēm bija lieli sirds spriedumi.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
Gileāds palika viņpus Jardānes, un kāpēc Dans mīt pie laivām? Ašers sēž jūrmalā un paliek savos līčos.
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
Zebulons, tā ir tauta, kas savu dvēseli nodod nāvē, un Naftalus arīdzan augstos klajumos.
19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
Ķēniņi nāca, tie karoja, tad Kanaāna ķēniņi karoja pie Taānakas, pie Meģidus ūdeņiem; naudas peļņu tie nedabūja.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
No debesīm karoja, zvaigznes no saviem ceļiem karoja pret Siseru.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
Ķizonas upe viņus aizrāva, tā veclaiku upe, Ķizonas upe. Celies, mana dvēsele, ar spēku!
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
Rībēt rībēja apakš zirgu kājām, jājot, viņu vareniem jājot.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
Lādiet Merosu, saka Tā Kunga eņģelis, lādiet lādēdami viņa iedzīvotājus, tāpēc ka tie nav nākuši palīgā Tam Kungam, palīgā Tam Kungam ar stiprajiem.
24 “Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
Svētīta pār sievām lai ir Jaēle, Hebera, tā Kenieša, sieva, svētīta pār sievām teltīs.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
Ūdeni tas prasīja, tā deva pienu; dārgā kausā tā atnesa kreimu(krējumu).
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
Savu roku tā izstiepa pēc naglas, un savu labo roku pēc strādnieku vesera, un sita Siseram, sašķēla viņa galvu, satrieca un izurba viņa deniņus.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
Apakš viņas kājām tas locījās, krita zemē, gulēja; apakš viņas kājām tas locījās, krita; tur, kur locījās, tas gāzās un bija pagalam.
28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
Pa logu skatījās Siserus māte un kliedza caur skadriņiem: kāpēc viņa rati kavējās, ka tie nenāk? Kāpēc viņa zirgu soļi tik lēni?
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
Tās gudrās no viņas cienīgām tai atbild, un arī (viņa) pati tā atbild uz saviem vārdiem:
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
“Vai tad tie neatradīs un neizdalīs laupījumu, vienu, divas sievietes uz vīra galvu, raibas drēbes Siserum par laupījumu, raibas rakstītas drēbes par laupījumu, raibu drēbi, divas rakstītas raibas drēbes ap kaklu laupītajām.
31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.
Tā lai, Kungs, iet bojā visi Tavi ienaidnieki! Bet kas Viņu mīļo, lai ir, tā kā saule uzlec savā spēkā.” - Un tai zemei bija miers četrdesmit gadus.

< Oweruza 5 >