< Oweruza 5 >

1 “Tsiku limenelo Debora ndi Baraki mwana wa Abinoamu anayimba nyimbo iyi:
Chiengʼno Debora kod Barak wuod Abinoam nowero wendni:
2 “Popeza kuti atsogoleri anatsogoleradi mʼdziko la Israeli; ndipo anthu anadzipereka okha mwa ufulu, tamandani Yehova:
“Pakuru Jehova Nyasaye nikech jotelo mag Israel okawo loch, kendo ji giwegi ochiwore mar luwogi!
3 “Imvani inu mafumu! Tcherani khutu, atsogoleri inu! Ndidzayimba nyimbo, ndidzayimbira Yehova, Mulungu wa Israeli nyimbo yokoma.
“Winjuru, un ruodhi! Chikuru itu, un jotelo! Abiro pako Jehova Nyasaye ka awerne; anachuog ne Jehova Nyasaye ma Nyasach Israel wer.
4 “Inu Yehova, pamene munkatuluka mu Seiri, pamene mumayenda kuchokera mʼdziko la Edomu, dziko linagwedezeka, mitambo inasungunuka nigwetsa madzi.
“Yaye Jehova Nyasaye, piny noyiengni, kendo polo nogingore, mi koth ochwe kane iwuok Seir e piny Edom.
5 Mapiri anagwedezeka pamaso pa Yehova, Mulungu wa Israeli.
Got Sinai noyiengni e nyim Jehova Nyasaye, ma Nyasach Israel.
6 “Pa nthawi ya Samugara mwana wa Anati, pa nthawi ya Yaeli, misewu inasiyidwa; alendo ankangoyenda mʼtinjira takumbali.
“E ndalo mag Shamgar wuod Anath, kendo e ndalo Jael, yore nojwangʼ, mi jowuoth ne luwo yore matindo.
7 Anthu a ku midzi anathawa; mu Israeli munalibe midzi mpaka pamene iwe Debora unafika; unafika ngati mayi ku Israeli.
Teko mar jolweny e miech Israel norumo, manyaka an Debora nabiro, ma abedo ka min ji e piny Israel.
8 Pamene anasankha milungu ina, nkhondo inabwera ku zipata za mzinda, ndipo chishango kapena mkondo sizinapezeke pakati pa anthu 40,000 mu Israeli.
Kane giyiero nyiseche manyien, lweny nochakore e dhorangeye mag dala maduongʼ, kata mana okumba kod tongʼ ne ok oyudie kind jolwenj jo-Israel alufu piero angʼwen.
9 Mtima wanga uli ndi atsogoleri a Israeli, uli ndi anthu amene anadzipereka okha mwaufulu pakati pa anthu. Tamandani Yehova!
Opak Jehova Nyasaye nikech chunya nigi jotend jo-Israel, kaachiel gi jogo mochiwore!
10 “Inu okwera pa abulu oyera, okhala pa zishalo, ndi inu oyenda pa msewu, yankhulani.
“Un joma oidho punde marochere, kobedo e matandiko molos gi ongede, kendo un joma wuotho e wangʼ yo, winjuru,
11 Ku zitsime, kutali ndi phokoso la a mauta; kumeneko akusimba za kuti Yehova wapambana; akusimba kuti Yehova walipsira anthu ake mu Israeli. “Choncho anthu a Yehova anasonkhana ku zipata za mzinda.
dwond joma wer koa kuonde mamon umboe pi; ka giwero timbe makare mag Jehova Nyasaye, kendo ka gipako timbe makare mag jolweny mage mager man Israel. “Bangʼ mano oganda Jehova Nyasaye nodhi e dhorangeye mag dala maduongʼ.
12 Anati, ‘Tsogolera ndiwe, Debora, tsogolera; tsogolera ndiwe, tsogolera, imba nyimbo. Iwe Baraki! nyamuka Tsogolera akapolo ako, iwe mwana wa Abinoamu.’
Debora, chiew, chiew! ‘Chungi kendo ia malo mondo ichak wer! Aa malo, yaye Barak! Ter jogo miseloyo e twech, yaye wuod Abinoam.’
13 “Kenaka anthu okhulupirika anatsatira atsogoleri awo; anthu a Yehova anapita kukamenyera Yehova nkhondo kulimbana ndi adani amphamvu.
“Eka jogo mane owe nobiro ir ruodhi; oganda Jehova Nyasaye nobiro ira gi teko duto.
14 Anakalowa mʼchigwa kuchokera ku Efereimu; akutsatira iwe Benjamini ndi abale ako. Akulu a ankhondo anachokera ku Makiri, ndipo onyamula ndodo ya udindo anachokera ku Zebuloni.
Jomoko kuomgi nowuok e gode mag Efraim, ogandagi nodak Amalek, kendo joma noa Benjamin noluwo bangʼu. Jotend lweny noa Makir nobiro, kendo joma noa Zebulun notingʼo ludh jatend lweny.
15 Olamulira a Isakara anali pamodzi ndi Debora; inde, anthu ochokera ku Isakara anatsatanso Baraki, ndipo anathamangira ku chigwa akumutsatira. Koma pakati pa mafuko a Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuchita.
Jotend Isakar ne nigi Debora; adier, Isakar ne nigi Barak, koreto bangʼe ka gichiko holo. To e gwenge mag Reuben ne nitiere nono chuny matut.
16 Chifukwa chiyani munangokhala ku makola a nkhosa nʼkumangomvetsera zitoliro zoyitanira nkhosa? Pakati pa anthu a fuko la Rubeni panali kusinkhasinkha mtima kwambiri osadziwa chenicheni choyenera kuti achite.
En angʼo momiyo ne usiko ka uoyo maj jokwath mondo omi uwinj ka jokwath liyo ni rombe? To e gwenge mag Reuben ne nitiere nono chuny matut.
17 Agiliyadi anatsala pa tsidya la Yorodani. Ndipo nʼchifukwa chiyani anthu afuko la Dani anatsarira mʼsitima za pa madzi? Aseri anali pa gombe la Nyanja; anangokhala mʼmadooko mwawo.
Gilead nodongʼ loka Jordan. To angʼo momiyo Dan nogalore but meli? Asher to nodongʼ e dho nam mi gidak e dho wedhe kuma yiedhi gowe.
18 Azebuloni ndi anthu amene anayika moyo wawo mʼzoopsa. Nawonso anthu a fuko la Nafutali anayika miyoyo yawo pa chiswe pomenya nkhondo pamwamba pa mapiri.
Jo-Zebulun nochiwo ngimagi ne tho; kamano bende Naftali noketo mare e kuonde kedo.
19 “Mafumu anabwera, anachita nkhondo; mafumu Akanaani anachita nkhondo ku Tanaki pafupi ndi madzi a ku Megido, koma sanatengeko zofunkha zasiliva.
“Ruodhi mag Kanaan nobiro, mokedo; Tanak machiegni gi pige mag Megido, to ne ok gidhi gi fedha, kata kawo gimoro amora moyako.
20 Ngakhalenso nyenyezi zakumwamba zinachita nkhondo, zinathira nkhondo Sisera, zikuyenda mʼnjira zake.
Koa e polo, sulwe nokedo, koa kama gichakore negikedo gi Sisera.
21 Mtsinje wa Kisoni unawakokolola, chigumula cha mtsinje wa Kisoni chinawakokolola. Mtima wanga, yenda mwamphamvu, limbika!
Aora Kishon noywoyogi, aora ma hike ngʼeny, aora Kishon. Dhi nyime, chunya; bed motegno!
22 Ndipo ziboda za ngʼombe zazimuna zinachita phokoso lalikulu, akavalo ali pa liwiro, akuthamanga kwambiri.
Bangʼ mano mor mar tiende farese nowinji kachikore gi teko mangʼeny.
23 Mngelo wa Yehova anati ‘Tembererani Merozi.’ ‘Tembererani nzika zake mwaukali, chifukwa sanabwere kudzathandiza Yehova, kulimbana ndi adani ake amphamvu.’
Malaika mar Jehova Nyasaye nowacho ni, ‘Okwongʼ Meroz kaachiel gi joge gi kwongʼ malit, nikech ne ok gibiro mondo gikony Jehova Nyasaye e lwet joma tek.’
24 “Akhale wodala kupambana akazi onse, Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni; inde mwa akazi onse okhala mʼdziko, akhale wodala iyeyu.
“Jael ma chi Heber ja-Keni en dhako mogwedhi kuom mon duto, kendo ogwedhe moloyo mon duto modak e hema.
25 Munthu uja anapempha madzi akumwa, koma iye anamupatsa mkaka; anamupatsa chambiko mʼchikho cha wolemekezeka.
Nokwayo pi modho, to nomiye chak; nokelone chak mopwo e bakul moromo ruoth chiemoe.
26 Anatenga chikhomo cha tenti mʼdzanja lake, anatenganso nyundo ndi dzanja lake lamanja. Ndipo anakhoma nacho Sisera, anamuphwanya mutu wake, ndi kumubowola mu litsipa mwake.
Norieyo lwete mondo okaw sigingi mar hema, ka lwete korachwich nokawogo twor. Nogoyo Sisera, motoyo wiye, kendo nopowo lela wangʼe.
27 Anathifukira ku mapazi a mkaziyo nagwa, anagwa; iye anagona pamenepo. Anagwera pa mapazi a mkaziyo, iye anagwa; pamene anagwera, pamenepo anaferapo.
Nopodho e tiende, mogore piny; kendo kanyo ema nothoe. Adier, nopodho e tiende, mogore piny; kendo kama nopodhoeno, ema nogore piny motho.
28 “Amayi ake a Sisera anasuzumira pa zenera; nafuwula mokweza kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani galeta lake lachedwa kufika? Nʼchifukwa chiyani phokoso la magaleta ake silikumveka?’
“Min Sisera ne ngʼicho gie dirisa; kaywak kama: ‘Angʼo momiyo gache odeko kapok obiro? Angʼo momiyo mor mar gechene ok winjre?’
29 Amayi ake anzeru kwambiri anamuyankha, ndithudi, mwiniwake anadziyankha yekha kuti,
Achiel kuom jotichne ma nyiri mariek nodwoke; kawuoyo kende kama:
30 ‘Kodi iwo sakufunafuna zofunkha kuti agawane; akugawana wankhondo aliyense mtsikana mmodzi kapena awiri. Sisera akumupatsa zofunkha: zovala zonyikidwa mu utoto, zoti ndizivala mʼkhosi zovala zopeta zonyika mu utoto, ndi zopeta zomavala mʼkhosi?’
‘Donge gipogo gik moyaki ka ngʼato ka ngʼato yudo nyako achiel kata ariyo, kendo imiyo Sisera lewni mabeyo kaachiel gi lewni mabeyo motwangʼ mongʼith, monego arwaki?’
31 “Choncho Yehova! adani anu onse awonongeke, koma iwo amene amakukondani inu akhale ngati dzuwa pamene lituluka ndi mphamvu zake.” Ndipo dziko linakhala pa mtendere zaka makumi anayi.
“Omiyo mad wasikgi duto rum, yaye Jehova Nyasaye! To mad joma oheri chal gi chiengʼ, mawuok gi teko.” Bangʼ mano piny Israel nobedo gi kwe kuom higni piero angʼwen.

< Oweruza 5 >