< Oweruza 4 >

1 Ehudi atamwalira, Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova.
and to add: again son: descendant/people Israel to/for to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD and Ehud to die
2 Choncho Yehova anawapereka mʼmanja mwa Yabini, mfumu ya ku Kanaani, imene inkalamulira ku Hazori. Mkulu wa ankhondo ake anali Sisera, amene ankakhala ku Haroseti-Hagoyimu.
and to sell them LORD in/on/with hand: power Jabin king Canaan which to reign in/on/with Hazor and ruler army his Sisera and he/she/it to dwell in/on/with Harosheth (Harosheth)-hagoyim
3 Aisraeli analira kwa Yehova kuti awathandize, chifukwa Sisera anali ndi magaleta achitsulo 900 ndipo anazunza Aisraeli mwankhanza kwa zaka makumi awiri.
and to cry son: descendant/people Israel to(wards) LORD for nine hundred chariot iron to/for him and he/she/it to oppress [obj] son: descendant/people Israel in/on/with force twenty year
4 Debora, mneneri wamkazi, mkazi wake wa Rapidoti ndiye ankatsogolera Israeli nthawi imeneyo.
and Deborah woman: wife prophetess woman: wife Lappidoth he/she/it to judge [obj] Israel in/on/with time [the] he/she/it
5 Iye ankakhala pansi pa mtengo wa mgwalangwa wa Debora, pakati pa Rama ndi Beteli mʼdziko la ku mapiri la Efereimu, ndipo Aisraeli ankapita kwa iye kuti akaweruze milandu yawo.
and he/she/it to dwell underneath: under palm Deborah between [the] Ramah and between Bethel Bethel in/on/with mountain: hill country Ephraim and to ascend: rise to(wards) her son: descendant/people Israel to/for justice: judgement
6 Debora uja anatuma munthu kuti akayitane Baraki mwana wa Abinoamu wa ku Kedesi mʼdziko la Nafutali ndipo anati kwa iye, “Yehova Mulungu wa Israeli akukulamula iwe kuti, ‘Pita kasonkhanitse anthu ku phiri la Tabori. Ubwere nawo anthu 10,000 a fuko la Nafutali ndi a fuko la Zebuloni.
and to send: depart and to call: call to to/for Barak son: child Abinoam from Kedesh (Kedesh)-naphtali and to say to(wards) him not to command LORD God Israel to go: went and to draw in/on/with mountain: mount (Mount) Tabor and to take: take with you ten thousand man from son: descendant/people (Kedesh)-naphtali and from son: descendant/people Zebulun
7 Ine ndidzakokera Sisera mkulu wa ankhondo a Yabini pamodzi ndi magaleta ake ndi asilikali ake kwa inu ku mtsinje wa Kisoni ndipo ndidzamupereka mʼmanja mwanu.’”
and to draw to(wards) you to(wards) torrent: river Kishon [obj] Sisera ruler army Jabin and [obj] chariot his and [obj] crowd his and to give: give him in/on/with hand: power your
8 Baraki anamuyankha kuti, “Mukapita nane limodzi ine ndipita. Koma ngati sitipitira limodzi, inenso sindipita.”
and to say to(wards) her Barak if to go: went with me and to go: went and if not to go: went with me not to go: went
9 Debora anati, “Chabwino, ine ndipita nawe limodzi. Koma mudziwe kuti inu simudzalandirapo ulemu pa zimene mwachitazi popeza Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwa munthu wamkazi.” Choncho Debora ananyamuka kupita ku Kedesi pamodzi ndi Baraki.
and to say to go: went to go: went with you end for not to be beauty your upon [the] way: road which you(m. s.) to go: went for in/on/with hand: power woman to sell LORD [obj] Sisera and to arise: rise Deborah (and to go: went *L(abh)*) with Barak Kedesh [to]
10 Baraki anayitana mafuko a Zebuloni ndi Nafutali kuti abwere ku Kedesi. Anthu 10,000 anamutsatira, ndipo Debora anapita naye pamodzi.
and to cry out Barak [obj] Zebulun and [obj] Naphtali Kedesh [to] and to ascend: rise in/on/with foot his ten thousand man and to ascend: rise with him Deborah
11 Nthawi imeneyo nʼkuti Mkeni wina dzina lake Heberi atalekana ndi Akeni anzake, zidzukulu za Hobabu, mlamu wa Mose, nakamanga tenti yake pafupi ndi mtengo wa thundu ku Zananimu pafupi ndi Kedesi.
and Heber [the] Kenite to separate from Kenite from son: descendant/people Hobab relative Moses and to stretch tent his till terebinth (in/on/with Zaanannim *Q(K)*) which with Kedesh
12 Pamene Sisera anamva kuti Baraki mwana wa Abinoamu wapita ku phiri la Tabori,
and to tell to/for Sisera for to ascend: rise Barak son: child Abinoam mountain: mount (Mount) Tabor
13 anasonkhanitsa magaleta ake achitsulo 900 ndi anthu onse amene anali naye ndipo anachoka ku Haroseti-Hagoyimu kupita ku mtsinje wa Kisoni.
and to cry out Sisera [obj] all chariot his nine hundred chariot iron and [obj] all [the] people: soldiers which with him from Harosheth (Harosheth)-hagoyim to(wards) torrent: river Kishon
14 Debora anawuza Baraki kuti, “Dzukani! Paja ndi lero limene Yehova wapereka Sisera mʼmanja mwako. Kodi Yehova sanakhale akukutsogolerani?” Choncho Baraki anatsika phiri la Tabori, anthu 10,000 akumutsata.
and to say Deborah to(wards) Barak to arise: rise for this [the] day which to give: give LORD [obj] Sisera in/on/with hand: power your not LORD to come out: come to/for face: before your and to go down Barak from mountain: mount (Mount) Tabor and ten thousand man after him
15 Yehova anasokoneza Sisera ndi magaleta ake pamodzi ndi ankhondo ake onse. Baraki ndi anthu ake anawapirikitsa ndipo Sisera anatsika pa galeta yake nayamba kuthawa pansi.
and to confuse LORD [obj] Sisera and [obj] all [the] chariot and [obj] all [the] camp to/for lip: edge sword to/for face: before Barak and to go down Sisera from upon [the] chariot and to flee in/on/with foot his
16 Baraki analondola magaletawo pamodzi ndi ankhondo onse mpaka ku Haroseti-Hagoyimu, ndipo ankhondo onse a Sisera anaphedwa ndi lupanga. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe anatsala.
and Barak to pursue after [the] chariot and after [the] camp till Harosheth (Harosheth)-hagoyim and to fall: kill all camp Sisera to/for lip: edge sword not to remain till one
17 Komabe Sisera anathawa pansi mpaka anakafika ku tenti ya Yaeli mkazi wa Heberi Mkeni uja, chifukwa panali mtendere pakati pa Yabini mfumu ya Hazori ndi banja la Heberi, Mkeni uja.
and Sisera to flee in/on/with foot his to(wards) tent Jael (woman: wife *L(abh)*) Heber [the] Kenite for peace between Jabin king Hazor and between house: household Heber [the] Kenite
18 Yaeli anatuluka kukachingamira Sisera ndipo anati, “Bwerani mbuye wanga, lowani momwemo musaope.” Choncho analowa mʼtenti muja, ndipo anamufunditsa chofunda.
and to come out: come Jael to/for to encounter: meet Sisera and to say to(wards) him to turn aside: turn aside [emph?] lord my to turn aside: turn aside [emph?] to(wards) me not to fear and to turn aside: turn aside to(wards) her [the] tent [to] and to cover him in/on/with rug
19 Anati, “Ndili ndi ludzu, chonde patseniko madzi pangʼono akumwa, ndili ndi ludzu.” Mkaziyo anatsekula thumba la chikopa mmene munali mkaka, namupatsa kuti amwe, ndipo anamufunditsanso.
and to say to(wards) her to water: drink me please little water for to thirst and to open [obj] wineskin [the] milk and to water: drink him and to cover him
20 Kenaka anawuza mkaziyo kuti, “Muyime pa khomo la tentili, ndipo munthu wina akabwera kudzakufunsani kuti, ‘Kodi kwafika munthu wina kuno?’ Inu muyankha kuti, ‘Ayi.’”
and to say to(wards) her to stand: stand entrance [the] tent and to be if man: anyone to come (in): come and to ask you and to say there here man: anyone and to say nothing
21 Koma Yaeli mkazi wa Heberi, anatenga chikhomo cha tenti ndi hamara ndi kupita mwakachetechete kwa Sisera uja. Tsono Sisera ali mtulo chifukwa chotopa, mkazi uja anamukhomera chikhomo chija mʼmutu mwake. Chinatulukira kwinaku mpaka kulowa mʼnthaka, ndipo anafa pomwepo.
and to take: take Jael woman: wife Heber [obj] peg [the] tent and to set: take [obj] [the] hammer in/on/with hand her and to come (in): come to(wards) him in/on/with secret and to blow [obj] [the] peg in/on/with temple his and to descend in/on/with land: soil and he/she/it to sleep and be faint and to die
22 Baraki atafika akulondola Sisera, Yaeli anatuluka kukamuchingamira namuwuza kuti, “Lowani mudzaone munthu amene mukumufunafuna.” Tsono atalowa anangoona Sisera ali thapsa pansi wakufa ndi chikhomo chili mʼmutu mwake.
and behold Barak to pursue [obj] Sisera and to come out: come Jael to/for to encounter: meet him and to say to/for him to go: come and to see: see you [obj] [the] man which you(m. s.) to seek and to come (in): come to(wards) her and behold Sisera to fall: kill to die and [the] peg in/on/with temple his
23 “Choncho pa tsiku limenelo Mulungu anagonjetsa Yabini mfumu ya Akanaani, pamaso pa Aisraeli.
and be humble God in/on/with day [the] he/she/it [obj] Jabin king Canaan to/for face: before son: descendant/people Israel
24 Ndipo Aisraeli anapanikizabe Yabini, mfumu ya Akanaani, mpaka kumuwonongeratu.
and to go: continue hand: power son: descendant/people Israel to go: continue and severe upon Jabin king Canaan till which to cut: eliminate [obj] Jabin king Canaan

< Oweruza 4 >