< Oweruza 3 >
1 Iyi ndi mitundu ya anthu yomwe Yehova anayisiya kuti ayese nayo Aisraeli amene sanadziwe kumenya nkhondo mu Kanaani
Now these are the nations which the LORD left, to prove Israel by them, even as many as had not known all the wars of Canaan;
2 (Yehova anachita izi kuti Aisraeli onse aphunzire kumenya nkhondo; makamaka amene nʼkale lonse sanadziwe kumenya nkhondo.
only that the generations of the children of Israel might know, to teach them war, at the least such as beforetime knew nothing thereof;
3 Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
namely, the five lords of the Philistines, and all the Canaanites, and the Zidonians, and the Hivites that dwelt in mount Lebanon, from mount Baal-hermon unto the entrance of Hamath.
4 Iwowa Yehova anawasiya kuti aziyesa nawo Aisraeli kuti aone ngati angamvere malamulo a Yehova, amene anapatsa makolo awo kudzera mwa Mose.
And they were there, to prove Israel by them, to know whether they would hearken unto the commandments of the LORD, which He commanded their fathers by the hand of Moses.
5 Choncho Aisraeli anakhala pakati pa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
And the children of Israel dwelt among the Canaanites, the Hittites, and the Amorites, and the Perizzites, and the Hivites, and the Jebusites;
6 Tsono Aisraeli aja amalola ana awo aamuna ndi aakazi kuti azikwatira ndi kukwatiwa ndi anthu amitundu ina. Kenaka anayamba kupembedza milungu yawo.
and they took their daughters to be their wives, and gave their own daughters to their sons, and served their gods.
7 Aisraeli anachita zinthu zoyipira Yehova. Iwowa anayiwala Yehova Mulungu wawo ndi kumatumikira Abaala ndi Asera.
And the children of Israel did that which was evil in the sight of the LORD, and forgot the LORD their God, and served the Baalim and the Asheroth.
8 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeliwo ndipo anawagulitsa kwa Kusani-Risataimu mfumu ya ku Mesopotamiya. Choncho Aisraeli anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zisanu ndi zitatu.
Therefore the anger of the LORD was kindled against Israel, and He gave them over into the hand of Cushan-rishathaim king of Aram-naharaim; and the children of Israel served Cushan-rishathaim eight years.
9 Koma pamene Aisraeliwo analirira kwa Yehova, Iye anawawutsira mpulumutsi, Otanieli mwana wamwamuna wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe. Iyeyu ndiye anawapulumutsa.
And when the children of Israel cried unto the LORD, the LORD raised up a saviour to the children of Israel, who saved them, even Othniel the son of Kenaz, Caleb's younger brother.
10 Mzimu wa Yehova unatsika pa iye, choncho anasanduka mtsogoleri wa Israeli. Iye anapita kukamenya nkhondo, ndipo Yehova anapereka Kusani-Risataimu mfumu ya Aaramu mʼmanja mwake. Choncho anayigonjetsa.
And the spirit of the LORD came upon him, and he judged Israel; and he went out to war, and the LORD delivered Cushan-rishathaim king of Aram into his hand; and his hand prevailed against Cushan-rishathaim.
11 Ndipo mʼdzikomo munakhala mtendere zaka makumi anayi. Kenaka Otanieli mwana wa Kenazi anamwalira.
And the land had rest forty years. And Othniel the son of Kenaz died.
12 Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Tsono Yehova anapatsa mphamvu Egiloni, mfumu ya Mowabu kuti alimbane ndi Aisraeli aja popeza anachita zinthu zoyipira Yehova.
And the children of Israel again did that which was evil in the sight of the LORD; and the LORD strengthened Eglon the king of Moab against Israel, because they had done that which was evil in the sight of the LORD.
13 Egiloniyo anamemeza Aamori ndi Aamaleki kupita kukamenyana ndi Israeli, ndipo analanda Yeriko, mzinda wa migwalangwa.
And he gathered unto him the children of Ammon and Amalek; and he went and smote Israel, and they possessed the city of palm-trees.
14 Aisraeli anatumikira ngati akapolo Egiloni mfumu ya Mowabu kwa zaka 18.
And the children of Israel served Eglon the king of Moab eighteen years.
15 Aisraeli analiranso kwa Yehova, ndipo Iye anawawutsira mpulumutsi, Ehudi. Iyeyu anali mwana wa Gera, munthu wamanzere, wa fuko la Benjamini. Aisraeli ankatumiza msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, kudzera kwa Ehudi.
But when the children of Israel cried unto the LORD, the LORD raised them up a saviour, Ehud the son of Gera, the Benjamite, a man left-handed; and the children of Israel sent a present by him unto Eglon the king of Moab.
16 Ndipo Ehudi anapanga lupanga lakuthwa kuwiri lotalika masentimita makumi asanu, ndipo anamangirira lupangalo pa ntchafu yake ya kumanja mʼkati mwa zovala zake.
And Ehud made him a sword which had two edges, of a cubit length; and he girded it under his raiment upon his right thigh.
17 Iye anakapereka msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, amene anali munthu wonenepa kwambiri.
And he offered the present unto Eglon king of Moab — now Eglon was a very fat man.
18 Ehudi atapereka msonkhowo, anawuza anthu amene ananyamula msonkhowo kuti azipita.
And when he had made an end of offering the present, he sent away the people that bore the present.
19 Iye mwini anabwerera pamalo a miyala yozokotedwa ku Giligala ndipo anati, “Zikomo mfumu, ine ndili ndi mawu achinsinsi kuti ndikuwuzeni.” Mfumuyo inawuza onse amene amayitumikira kuti akhale chete, ndipo kenaka anawatulutsa.
But he himself turned back from the quarries that were by Gilgal, and said: 'I have a secret errand unto thee, O king.' And he said: 'Keep silence.' And all that stood by him went out from him.
20 Kenaka Ehudi anayandikira pafupi ndi mfumuyo, ndipo iyo inakhala yokha mʼchipinda chapamwamba, mozizira bwino. Tsono Ehudi anati, “Ndili ndi mawu ochokera kwa Mulungu woti ndikuwuzeni.” Mfumuyo itadzuka pa mpando wake waufumu,
And Ehud came unto him; and he was sitting by himself alone in his cool upper chamber. And Ehud said: 'I have a message from God unto thee.' And he arose out of his seat.
21 Ehudi ndi dzanja lake lamanzere, anasolola lupanga pa ntchafu yake ya kumanja ndi kubaya nalo mfumuyo pa mimba.
And Ehud put forth his left hand, and took the sword from his right thigh, and thrust it into his belly.
22 Lupanga linalowa mʼmimba pamodzi ndi chogwirira chake. Mafuta anaphimba lupangalo popeza silinatulutsidwe mʼmimbamo. Ndiponso matumbo anatuluka.
And the haft also went in after the blade; and the fat closed upon the blade, for he drew not the sword out of his belly; and it came out behind.
23 Kenaka Ehudi anatuluka panja pa khonde, atatseka ndi kukhoma zitseko za chipinda chapamwambacho.
Then Ehud went forth into the porch, and shut the doors of the upper chamber upon him, and locked them.
24 Ehudi atachoka, atumiki a mfumu aja anabwera, ndipo ataona kuti zitseko za chipinda chapamwamba zinali zokhoma anaganiza kuti mwina mfumu ikudzithandiza mʼkatimo.
Now when he was gone out, his servants came; and they saw, and, behold, the doors of the upper chamber were locked; and they said: 'Surely he is covering his feet in the cabinet of the cool chamber.'
25 Iwo anadikira nthawi yayitali koma popanda chochitika. Koma ataona kuti mfumuyo sikutsekulabe zitseko za chipindacho, iwo anatenga makiyi ndi kutsekula zitsekozo, ndipo anangoona mbuye wawo atagwera pansi, ali wakufa.
And they tarried till they were ashamed; and, behold, he opened not the doors of the upper chamber; therefore they took the key, and opened them; and, behold, their lord was fallen down dead on the earth.
26 Ehudi anathawa pamene iwo ankadikira. Iye anadzera ku malo a miyala yozokotedwa kuja ndi kuthawa kupita ku Seiri.
And Ehud escaped while they lingered, having passed beyond the quarries, and escaped unto Seirah.
27 Atafika kumeneko, anayimba lipenga ku dziko la ku mapiri la Efereimu. Iye akutsogolera, Aisraeli onse anatsika naye pamodzi kuchoka ku mapiriko.
And it came to pass, when he was come, that he blew a horn in the hill-country of Ephraim, and the children of Israel went down with him from the hill-country, and he before them.
28 Iye anawawuza kuti, “Nditsatireni, chifukwa Yehova wapereka Amowabu, adani anu mʼmanja mwanu.” Choncho anthuwo anamutsatira, nalanda madooko a Yorodani opita ku Mowabu. Iwo sanalole kuti wina aliyense awoloke.
And he said unto them: 'Follow after me; for the LORD hath delivered your enemies the Moabites into your hand.' And they went down after him, and took the fords of the Jordan against the Moabites, and suffered not a man to pass over.
29 Nthawi imeneyo anapha Amowabu pafupifupi 10,000. Ophedwawo anali anthu amphamvu komanso odziwa kumenya nkhondo, ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anathawa.
And they smote of Moab at that time about ten thousand men, every lusty man, and every man of valour; and there escaped not a man.
30 Tsiku limenelo Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Israeli, ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 80.
So Moab was subdued that day under the hand of Israel. And the land had rest fourscore years.
31 Ehudi atamwalira, panabwera Samugara mwana wa Anati. Iye anapha Afilisti 600 ndi ndodo yomenyera ngʼombe. Nayenso anapulumutsa Israeli.
And after him was Shamgar the son of Anath, who smote of the Philistines six hundred men with an ox-goad; and he also saved Israel.