< Oweruza 21 >

1 Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
و مردان اسرائیل در مصفه قسم خورده، گفتند که «احدی از ما دختر خود را به بنیامینیان به زنی ندهند.»۱
2 Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
و قوم به بیت ئیل آمده، در آنجا به حضور خدا تا شام نشستند و آواز خودرا بلند کرده، زار‌زار بگریستند.۲
3 Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
و گفتند: «ای یهوه، خدای اسرائیل، این چرا در اسرائیل واقع شده است که امروز یک سبط از اسرائیل کم شود؟»۳
4 Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
و در فردای آن روز قوم به زودی برخاسته، مذبحی در آنجا بنا کردند، وقربانی های سوختنی و ذبایح سلامتی گذرانیدند.۴
5 Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
و بنی‌اسرائیل گفتند: «کیست از تمامی اسباطاسرائیل که در جماعت نزد خداوند بر نیامده است.» زیرا قسم سخت خورده، گفته بودند که هرکه به حضور خداوند به مصفه نیاید، البته کشته شود.۵
6 Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
و بنی‌اسرائیل درباره برادر خود بنیامین پشیمان شده، گفتند: «امروز یک سبط از اسرائیل منقطع شده است.۶
7 Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
برای بقیه ایشان درباره زنان چه کنیم؟ زیرا که ما به خداوند قسم خورده‌ایم که از دختران خود به ایشان به زنی ندهیم.»۷
8 Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
و گفتند: «کدام‌یک از اسباط اسرائیل است که به حضور خداوند به مصفه نیامده است؟» و اینک از یابیش جلعاد کسی به اردو و جماعت نیامده بود.۸
9 Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
زیرا چون قوم شمرده شدند اینک ازساکنان یابیش جلعاد احدی در آنجا نبود.۹
10 Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
پس جماعت دوازده هزار نفر از شجاع ترین قوم را به آنجا فرستاده، و ایشان را امر کرده، گفتند: «بروید و ساکنان یابیش جلعاد را با زنان و اطفال به دم شمشیر بکشید.۱۰
11 Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
و آنچه باید بکنید این است که هر مردی را و هر زنی را که با مرد خوابیده باشد، هلاک کنید.»۱۱
12 Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
و در میان ساکنان یابیش جلعادچهارصد دختر باکره که با ذکوری نخوابیده ومردی را نشناخته بودند یافتند، و ایشان را به اردو در شیلوه که در زمین کنعان است، آوردند.۱۲
13 Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
و تمامی جماعت نزد بنی بنیامین که درصخره رمون بودند فرستاده، ایشان را به صلح دعوت کردند.۱۳
14 Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
و در آن وقت بنیامینیان برگشتند و دخترانی را که از زنان یابیش جلعادزنده نگاه داشته بودند به ایشان دادند، و باز ایشان را کفایت نکرد.۱۴
15 Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
و قوم برای بنیامین پشیمان شدند، زیراخداوند در اسباط اسرائیل شقاق پیدا کرده بود.۱۵
16 Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
و مشایخ جماعت گفتند: «درباره زنان به جهت باقی ماندگان چه کنیم چونکه زنان از بنیامین منقطع شده‌اند؟۱۶
17 Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
و گفتند: میراثی به جهت نجات‌یافتگان بنیامین باید باشد تا سبطی ازاسرائیل محو نشود.۱۷
18 Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
اما ما دختران خود را به ایشان به زنی نمی توانیم داد زیرا بنی‌اسرائیل قسم خورده، گفته‌اند ملعون باد کسی‌که زنی به بنیامین دهد.۱۸
19 Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
و گفتند: «اینک هر سال در شیلوه که به طرف شمال بیت ئیل و به طرف مشرق راهی که ازبیت ئیل به شکیم می‌رود، و به سمت جنوبی لبونه است، عیدی برای خداوند می‌باشد.»۱۹
20 Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
پس بنی بنیامین را امر فرموده، گفتند: «بروید درتاکستانها در کمین باشید،۲۰
21 ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
و نگاه کنید و اینک اگر دختران شیلوه بیرون آیند تا با رقص کنندگان رقص کنند، آنگاه از تاکستانها درآیید، و ازدختران شیلوه هرکس زن خود را ربوده، به زمین بنیامین برود.۲۱
22 Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
و چون پدران و برادران ایشان آمده، نزد ما شکایت کنند، به ایشان خواهیم گفت: «ایشان را به‌خاطر ما ببخشید، چونکه مابرای هر کس زنش را در جنگ نگاه نداشتیم، وشما آنها را به ایشان ندادید، الان مجرم می‌باشید.»۲۲
23 Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
پس بنی بنیامین چنین کردند، و ازرقص کنندگان، زنان را برحسب شماره خودگرفتند، و ایشان را به یغما برده، رفتند، و به ملک خود برگشته، شهرها را بنا کردند و در آنها ساکن شدند.۲۳
24 Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
و در آن وقت بنی‌اسرائیل هر کس به سبط خود و به قبیله خود روانه شدند، و از آنجاهرکس به ملک خود بیرون رفتند.۲۴
25 Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.
و در آن ایام در اسرائیل پادشاهی نبود وهرکس آنچه در نظرش پسند می‌آمد، می‌کرد.۲۵

< Oweruza 21 >