< Oweruza 21 >
1 Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
Or les hommes d'Israël avaient juré à Mitspa, en disant: Nul de nous ne donnera sa fille pour femme à un Benjamite.
2 Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
Puis le peuple vint à Béthel, et resta là jusqu'au soir en la présence de Dieu. Ils élevèrent la voix et répandirent des larmes en abondance,
3 Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
Et ils dirent: O Éternel, Dieu d'Israël, pourquoi ceci est-il arrivé en Israël, qu'il manque aujourd'hui une tribu d'Israël?
4 Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
Et le lendemain le peuple se leva de bon matin; et ils bâtirent là un autel, et ils offrirent des holocaustes et des sacrifices de prospérité.
5 Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
Alors les enfants d'Israël dirent: Qui est celui d'entre toutes les tribus d'Israël qui n'est point monté à l'assemblée, vers l'Éternel? Car on avait fait un grand serment contre celui qui ne monterait point vers l'Éternel, à Mitspa, en disant: Il sera puni de mort!
6 Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
Car les enfants d'Israël se repentaient de ce qui était arrivé à Benjamin, leur frère, et disaient: Aujourd'hui une tribu a été retranchée d'Israël.
7 Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
Que ferons-nous pour ceux qui sont demeurés de reste, pour leur donner des femmes, puisque nous avons juré par l'Éternel que nous ne leur donnerions point de nos filles pour femmes?
8 Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
Ils dirent donc: Y a-t-il quelqu'un d'entre les tribus d'Israël qui ne soit point monté vers l'Éternel, à Mitspa? Et voici, personne de Jabès de Galaad n'était venu au camp, à l'assemblée;
9 Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
Quand on fit le dénombrement du peuple, nul ne s'y trouva des habitants de Jabès de Galaad.
10 Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
Alors l'assemblée y envoya douze mille hommes des plus vaillants, et leur donna cet ordre: Allez et faites passer au fil de l'épée les habitants de Jabès de Galaad, tant les femmes que les petits enfants.
11 Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
Voici donc ce que vous ferez: Vous vouerez à l'interdit tout mâle, et toute femme qui a connu la couche d'un homme.
12 Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
Et ils trouvèrent, parmi les habitants de Jabès de Galaad, quatre cents filles vierges, qui n'avaient point connu la couche d'un homme, et ils les amenèrent au camp, à Silo, qui est au pays de Canaan.
13 Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
Alors toute l'assemblée envoya parler aux Benjamites, qui étaient au rocher de Rimmon, et on leur annonça la paix.
14 Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
En ce temps-là, les Benjamites revinrent, et on leur donna les femmes à qui on avait laissé la vie parmi les femmes de Jabès de Galaad; mais il ne s'en trouva pas assez pour eux.
15 Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
Et le peuple se repentait au sujet de Benjamin, car l'Éternel avait fait une brèche aux tribus d'Israël.
16 Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
Et les anciens de l'assemblée dirent: Que ferons-nous pour donner des femmes à ceux qui restent? car les femmes des Benjamites ont été exterminées.
17 Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
Et ils dirent: Ceux qui sont réchappés, posséderont ce qui appartenait à Benjamin, afin qu'une tribu ne soit pas retranchée d'Israël.
18 Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
Cependant, nous ne pouvons pas leur donner des femmes d'entre nos filles; car les enfants d'Israël ont juré, en disant: Maudit soit celui qui donnera une femme à Benjamin!
19 Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
Et ils dirent: Voici, il y a chaque année une fête de l'Éternel à Silo, qui est au nord de Béthel, et à l'orient du chemin qui monte de Béthel à Sichem, et au midi de Lébona.
20 Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
Et ils donnèrent cet ordre aux enfants de Benjamin: Allez, et placez-vous en embuscade dans les vignes;
21 ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
Et quand vous verrez que les filles de Silo sortiront pour danser au son des flûtes, alors vous sortirez des vignes, et vous enlèverez chacun pour vous une femme, d'entre les filles de Silo, et vous vous en irez au pays de Benjamin.
22 Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
Et quand leurs pères ou leurs frères viendront se plaindre auprès de nous, nous leur dirons: Ayez pitié d'eux pour l'amour de nous; parce que nous n'avons point pris de femme pour chacun d'eux dans cette guerre. Car ce n'est pas vous qui les leur avez données; en ce cas vous auriez été coupables.
23 Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
Les enfants de Benjamin firent ainsi, et prirent des femmes, selon leur nombre, d'entre les danseuses qu'ils enlevèrent; puis, ils partirent et retournèrent dans leur héritage; ils rebâtirent des villes, et y habitèrent.
24 Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
Dans le même temps les enfants d'Israël s'en retournèrent de là, chacun en sa tribu et dans sa famille; ils s'en allèrent de là chacun dans son héritage.
25 Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.
En ces jours-là il n'y avait point de roi en Israël, mais chacun faisait ce qui lui semblait bon.