< Oweruza 21 >

1 Aisraeli anali atalumbira ku Mizipa kuti, “Palibe mmodzi wa ife adzapereke mwana wake wamkazi kuti akwatiwe ndi mwamuna wa fuko la Benjamini.”
Now the men of Israel had sworn in Mizpah, saying, Not any of us shall give his daughter unto Benjamin for wife.
2 Anthu anapita ku Beteli kumene anakakhala pansi pamaso pa Mulungu mpaka madzulo. Iwo anakweza mawu nalira kwambiri.
And the people came to Beth-el, and abode there till the evening, before God, and they lifted up their voices, and wept with a great lamentation;
3 Iwo ankanena kuti, “Yehova Mulungu wa Israeli, nʼchifukwa chiyani izi zachitika mʼdziko la Israeli kuti lero fuko limodzi lisowe mu Israeli?”
And they said, Wherefore, O Lord, God of Israel, is this come to pass in Israel, that there should be lacking this day out of Israel one tribe?
4 Mmawa mwake anthu anadzuka namanga guwa lansembe ndi kupereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano.
And it came to pass on the morrow, that the people rose early, and built there an altar, and offered burnt-offerings and peace-offerings.
5 Kenaka Aisraeli anafunsa kuti, “Kodi ndani pakati pa mafuko a Israeli sanafike ku msonkhano wa Yehova?” Anatero chifukwa anachita malumbiro aakulu okhudza munthu amene alephere kupita ku Mizipa ndi kuti woteroyo ayenera kuphedwa.
And the children of Israel said, Who is there among all the tribes of Israel that came not up with the congregation unto the Lord? For there had been taken the great oath concerning him that came not up to the Lord to Mizpah, saying, He shall surely be put to death.
6 Tsono Aisraeli anamva chisoni chifukwa cha abale awo, Abenjamini. Iwo anati, “Lero fuko limodzi lachotsedwa mu Israeli.
And the children of Israel felt regret for Benjamin their brother, and they said, One tribe hath this day been cut down from Israel.
7 Kodi tingawapezere bwanji anthu otsalawa akazi woti awakwatire? Paja ife tinalumbira kwa Yehova kuti sitidzapereka ana anthu aakazi kuti awakwatire.
What shall we do as respecteth wives for those that remain, since we have sworn by the Lord that we will give none of our daughters unto them for wives?
8 Kenaka anafunsa kuti, ‘Kodi mu fuko la Israeli ndani amene sanabwere pamaso pa Yehova ku Mizipa?’” Tsono panapezeka kuti panalibe ndi mmodzi yemwe wochokera ku Yabesi Giliyadi amene anapita ku msonkhano ku misasa kuja.
And they said, what one is there of the tribes of Israel that came not up unto the Lord to Mizpah? And, behold, there had not come to the camp a man from Yabesh-gil'ad to the assembly.
9 Pamene anthu anawerengana anangoona kuti anthu a ku Yabesi Giliyadi palibe.
For the people were numbered, and, behold, there was not present a man of the inhabitants of Yabesh-gil'ad.
10 Choncho msonkhano unatumiza anthu ankhondo 12,000 ndi kuwalamula kuti, “Mukaphe anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi, kuphatikizapo akazi ndi ana.”
And the congregation sent thither twelve thousand persons of the valiant men, and commanded them, saying, Go and smite the inhabitants of Yabesh-gil'ad with the edge of the sword, with the women and the children.
11 Izi ndi zimene mukachite. “Mukaphe mwamuna aliyense ndi mkazi aliyense amene anadziwapo mwamuna.”
And this is the thing that ye shall do, every male, and every woman that hath known [man] by lying with him, shall ye devote.
12 Iwo anapeza atsikana 400 pakati pa anthu okhala mu Yabesi Giliyadi amene anali asanadziwepo mwamuna ndipo anabwera nawo ku misasa ku Silo mʼdziko la Kanaani.
And they found among the inhabitants of Yabesh-gil'ad four hundred young virgins that had not known man by lying with any male: and they brought them unto the camp to Shiloh, which is in the land of Canaan.
13 Kenaka msonkhano wonse unatumiza uthenga kwa Abenjamini amene ankakhala ku thanthwe la Rimoni kuwawuza kuti nkhondo yatha.
And the whole congregation sent and spoke to the children of Benjamin that were on the rock Rimmon, and offered them peace.
14 Choncho Abenjamini anabwera nthawi imeneyo ndipo Aisraeli anawapatsa akazi a ku Yabesi Giliyadi amene sanaphedwe. Koma sanapezeke owakwanira.
And Benjamin returned at that time: and they gave unto them the wives whom they had saved alive out of the women of Yabesh-gil'ad; but they found not sufficient for them in this way.
15 Aisraeli anamvera chisoni Abenjamini, chifukwa Yehova anachita ngati waligwerula dzino fuko la Israeli.
And the people felt regret for Benjamin; because that the Lord had made a breach in the tribes of Israel.
16 Choncho akuluakulu a msonkhano anati, “Kodi tikawapezera kuti akazi anthu otsalirawa kuti awakwatire popeza kuti akazi a fuko la Benjamini anaphedwa?”
And the elders of the congregation said, What shall we do for those that remain as respecteth wives; because the women have been destroyed out of Benjamin?
17 Iwo anati, “Abenjamini amene anapulumukawa ayenera kukhala ndi zidzukulu, kuti mtundu wa Israeli usafafanizike.
And they said, Their inheritance must be secured for Benjamin, that not a tribe may be blotted out from Israel.
18 Ife sitingathe kuwapatsa ana anthu aakazi kuti akwatire. Paja tinalumbira kuti, ‘Akhale wotembereredwa aliyense amene adzapereka mwana wake wamkazi kwa mwamuna wa fuko la Benjamini kuti akwatire.’
Nevertheless we ourselves are not able to give them wives of our daughters; for the children of Israel have sworn, saying, Cursed be he that giveth a wife to Benjamin.
19 Ndipo anati, ‘Paja ku Silo kuli chikondwerero cha chaka ndi chaka cholemekeza Yehova. Tsono Silo ali kumpoto kwa Beteli, kummawa kwa msewu wochokera ku Beteli kupita ku Sekemu, ndiponso kummwera kwa Lebona.’”
And they said, Behold, there is a feast of the Lord in Shiloh from year to year [at a place] which is on the north side of Beth-el, on the east side of the highway that goeth up from Beth-el to Shechem, and on the south of Lebonah.
20 Choncho anawalamulira Abenjamini aja kuti, “Pitani mukabisale mʼminda ya mpesa
And they commanded the children of Benjamin, saying, Go ye and lie in wait in the vineyards;
21 ndipo mukakhale tcheru. Ana aakazi a ku Silo akadzatulukira kudzavina nawo magule, pomwepo inu mutuluke minda ya mpesa ndi kukawagwira aliyense wake ndi kupita nawo ku dziko la Benjamini.
And look out, and, behold, if the daughters of Shiloh go out to dance in dances: then come ye forth out of the vineyards, and snatch you every man his wife from the daughters of Shiloh, and go then to the land of Benjamin.
22 Ngati abambo awo kapena alongo awo adzabwera kudzadandaula kwa ife, tidzawawuza kuti, ‘Chonde, tikomereni mtima powalola kuti atenga ana anu aakaziwo popeza kuti ife sitinawapezere akazi pomenya nkhondo. Inunso simunachite kuwapatsa. Mukanatero ndiye mukanapalamula.’”
And it shall be, when their fathers or their brothers come to contend with us, that we will say unto them, Be favorable unto them for our sakes; because we took not for each man his wife in the war; [and] because ye yourselves did not give them unto them, that ye should at this time be guilty.
23 Abenjamini anachitadi zimenezi. Mwa akazi amene ankavina aja anagwirapo ena, malingana ndi chiwerengero chawo, nawatenga kuti akhale akazi awo. Kenaka ananyamuka kubwerera ku dziko la kwawo, nakamanganso mizinda yawo ndi kumakhalamo.
And the children of Benjamin did so, and took themselves wives, according to their number, from the dancers whom they had stolen away; and they went and returned unto their inheritance, and rebuilt the cities, and dwelt in them.
24 Pambuyo pake Aisraeli anachoka kumeneko ndi kubwerera kwawo, ku mafuko ndi ku mabanja awo, aliyense ku dera la cholowa chake.
And the children of Israel departed thence at that time, every man to his tribe and to his family, and they went out from there every man to his inheritance.
25 Masiku amenewo kunalibe mfumu ku Israeli. Aliyense ankangochita zimene zomukomera yekha.
In those days there was no king in Israel: every man did what was right in his own eyes.

< Oweruza 21 >