< Oweruza 20 >

1 Ndipo Aisraeli onse kuyambira ku dziko la Dani mpaka ku Beeriseba ndiponso ku dziko la Giliyadi ananyamuka ngati munthu mmodzi nakasonkhana pamaso pa Yehova ku Mizipa.
And so all the sons of Israel went out like one man, from Dan to Beersheba, with the land of Gilead, and they gathered together, before the Lord, at Mizpah.
2 Atsogoleri a anthu onse ndi a mafuko onse Aisraeli anali nawo pa msonkhano wa anthu a Mulungu. Onse pamodzi analipo asilikali oyenda pansi 400,000 atanyamula malupanga.
And all the chiefs of the people, and every tribe of Israel, convened as an assembly of the people of God, four hundred thousand foot soldiers for battle.
3 Anthu a fuko la Benjamini anali atamva kuti Aisraeli apita ku Mizipa. Tsono Aisraeli anati, “Tiwuzeni, zinthu zoyipa izi zinachitika bwanji.”
(But it was not hidden from the sons of Benjamin that the sons of Israel had ascended to Mizpah.) And the Levite, the husband of the woman who was killed, being questioned as to how so great a crime had been perpetrated,
4 Choncho Mlevi uja, mwamuna wa mkazi wophedwa uja anayankha nati, “Ine ndinapita ku Gibeya mʼdziko la Benjamini pamodzi ndi mzikazi wanga kuti tikagone kumeneko.
responded: “I went to Gibeah of Benjamin, with my wife, and I diverted to that place.
5 Usiku anthu a ku Gibeya anandiwukira, nazinga nyumba munali ine. Ankafuna kundipha ndipo anagona ndi mzikazi wanga momukakamiza mpaka anafa.
And behold, the men of that city, at night, surrounded the house in which I was staying, intending to kill me. And they abused my wife with such an incredible fury of lust that in the end she died.
6 Ine ndinatenga mzikazi wangayo ndi kumudula nthulinthuli ndikuzitumiza kwa fuko lililonse la Aisraeli. Anthu amenewa, zedi achita chinthu chonyansa kwambiri mʼdziko lino la Israeli.
And taking her up, I cut her into pieces, and I sent the parts into all the borders of your possession. For never before was such a nefarious crime, and so great a sin, committed in Israel.
7 Ndi zimenezotu inu Aisraeli nonse; yankhulaponi mawu ndi kupereka maganizo anu.”
You are all present here, O sons of Israel. Discern what you ought to do.”
8 Anthu onse anayimirira ngati munthu mmodzi nanena kuti, “Palibe mmodzi wa ife amene apite ku nyumba kwake. Palibe amene abwerere ku nyumba kwake.
And all the people, standing, responded as if with the word of one man: “We shall not return to our own tents, nor shall anyone enter into his own house.
9 Koma tsopano chimene ife tichite ndi dziko la Gibeya ndi ichi: Tidzapita kukamenyana nawo potsatira zimene maere anene.
But this we shall do in common against Gibeah:
10 Mʼmafuko onse a Aisraeli tidzasankha anthu khumi pa anthu 100 aliwonse: ndiye kuti anthu 100 pa anthu 1,000 aliwonse kapena anthu 1,000 pa anthu 10,000 aliwonse. Anthu amenewa adzasonkhanitsa zakudya za ankhondo, ndipo ankhondowo adzapita kukalipsira anthu a ku Geba mʼdziko la Benjamini chifukwa chochita chinthu chonyansa chotere mʼdziko la Israeli.”
We shall select ten men out of one hundred from all the tribes of Israel, and one hundred out of one thousand, and one thousand out of ten thousand, so that they may transport supplies for the army, and so that we will be able to fight against Gibeah of Benjamin, and to repay it for its crime as it deserves.”
11 Choncho anthu a ku Israeli anasonkhana pamodzi nagwirizana chimodzi, kukalimbana ndi mzindawo.
And all of Israel convened against the city, like one man, with one mind and one counsel.
12 Mafuko a Israeli anatumiza anthu kwa fuko lonse la Benjamini kukafunsa kuti, “Kodi zoyipa zachitika pakati panuzi ndi zotani?
And they sent messengers to the entire tribe of Benjamin, who said: “Why has so great a wickedness been found among you?
13 Tsono tikuti mutipatse anthu achabechabe a ku Gibeya kuti tiwaphe kuti tichotse chinthu choyipachi mʼdziko la Israeli.” Koma fuko la Benjamini silinafune kumvera zimene ananena Aisraeli anzawo.
Deliver the men of Gibeah, who have perpetrated this deplorable act, so that they may die, and so that the evil may be taken away from Israel.” And they were not willing to listen to the command of their brothers, the sons of Israel.
14 Mʼmalo mwake, Abenjaminiwo anatuluka mʼmizinda yawo ku Gibeya kukamenyana ndi Aisraeli.
Instead, out of all the cities that were their lot, they convened at Gibeah, so that they might bring them assistance, and so that they might contend against the entire people of Israel.
15 Tsiku limenelo Abenjamini anasonkhanitsa kuchokera ku mizinda yawo ankhondo 26,000 amalupanga awo, osawerengera anthu ena 700 a ku Gibeya amene anasankhidwa.
And there were found from Benjamin twenty-five thousand who drew the sword, aside from the inhabitants of Gibeah,
16 Mwa onsewa panali ankhondo 70 amanzere amene aliyense anali wodziwa kulasa ngakhale tsitsi limodzi ndi mwala osaphonya.
who were seven hundred very strong men, fighting with the left hand as well as with the right hand, and casting stones from a sling so accurately that they were able to strike even a hair, and the path of the stone would by no means miss to either side.
17 Aisraeli, kupatula fuko la Benjamini, anasonkhanitsa anthu 400,000 a malupanga, onse odziwa bwino nkhondo.
Then too, among the men of Israel apart from the sons of Benjamin, there were found four hundred thousand who drew the sword and who were prepared for battle.
18 Ndipo Aisraeli ananyamuka kupita ku Beteli kukafunsira kwa Mulungu. Iwo anati, “Ndani mwa ife amene angayambe kukamenyana ndi fuko la Benjamini?” Yehova anayankha kuti, “Fuko la Yuda ndilo liyambe.”
And they rose up and went to the house of God, that is, to Shiloh. And they consulted God, and they said, “Who shall be, in our army, the first to contend against the sons of Benjamin?” And the Lord responded to them, “Let Judah be your leader.”
19 Mmawa mwake Israeli ananyamuka nakamanga msasa moyangʼanana ndi Gibeya.
And immediately the sons of Israel, rising up in the morning, made camp near Gibeah.
20 Aisraeli anapita kukachita nkhondo ndi fuko la Benjamini ndipo anandandalika ankhondo awo moyangʼanana ndi Gibeya.
And setting out from there to fight against Benjamin, they began to assault the city.
21 A fuko la Benjamini anatuluka ku Gibeya ndipo tsiku limenelo anapha Aisraeli 22,000 ku nkhondoko.
And the sons of Benjamin, departing from Gibeah, slew twenty-two thousand men from the sons of Israel, on that day.
22 Koma ankhondo a Israeli analimbikitsananso mtima ndipo anasonkhanitsanso kachiwiri ankhondo awo pa malo pamene anawandandalika poyamba paja.
Again the sons of Israel, trusting in both strength and number, set their troops in order, in the same place where they had contended before.
23 Aisraeli anapita kukalira pamaso pa Yehova mpaka madzulo. Iwo anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukamenyana ndi a fuko la Benjamini abale athu?” Yehova anayankha kuti, “Pitani mukalimbane nawo.”
But first they also went up and wept before the Lord, even until night. And they consulted him and said, “Should I continue to go forth, so as to contend against the sons of Benjamin, my brothers, or not?” And he responded to them, “Ascend against them, and undertake the struggle.”
24 Ndipo Aisraeli anayandikiranso pafupi ndi fuko la Benjamini tsiku lachiwiri lake kuti amenyane nawo.
And when the sons of Israel had continued to do battle against the sons of Benjamin on the next day,
25 Pa tsiku lachiwiri lomwelo Abenjamini anatulukanso mu mzinda wa Gibeya ndipo anaphanso ankhondo 18,000. Onse amene anawaphawo anali odziwa kugwiritsa ntchito bwino malupanga.
the sons of Benjamin burst forth from the gates of Gibeah. And meeting them, they made such a frenzied slaughter against them that they struck down eighteen thousand men who drew the sword.
26 Tsono Aisraeli onse, gulu lonse la ankhondo, anapita ku Beteli kukalira pamaso pa Yehova. Anakhala pansi nasala zakudya tsiku lonse mpaka madzulo. Anapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pamaso pa Yehova.
As a result, all the sons of Israel went to the house of God, and sitting down, they wept before the Lord. And they fasted that day until evening, and they offered to him holocausts and victims of peace offerings.
27 Bokosi la Chipangano cha Yehova linali kumeneko.
And they inquired about their state. At that time, the ark of the covenant of the Lord was in that place.
28 Finehasi mwana wa Eliezara mwana wa Aaroni ndiye ankatumikira nthawi imeneyo. Tsono Aisraeli anafunsa Yehova kuti, “Kodi tipitenso kukachita nkhondo ndi mʼbale athu Abenjamini, kapena ayi?” Yehova anayankha kuti, “Pitaninso chifukwa mawa ndidzawapereka mʼmanja mwanu.”
And Phinehas, the son of Eleazar, the son of Aaron, was the first ruler of the house. And so, they consulted the Lord, and they said, “Should we continue to go forth in battle against the sons of Benjamin, our brothers, or should we cease?” And the Lord said to them: “Ascend. For tomorrow, I will deliver them into your hands.”
29 Choncho Aisraeli anayika anthu obisalira mozungulira Gibeya.
And the sons of Israel stationed ambushes around the city of Gibeah.
30 Tsiku lachitatu anapita kukamenyana ndi Benjamini ndipo anayika ankhondo mʼmalo mwawo kuti amenyane ndi Gibeya monga anachitira poyamba.
And they brought out their army against Benjamin a third time, just as they had done on the first and second times.
31 Abenjamini anatuluka kukamenyana nawo anthuwo ndipo anapita kutali ndi mzindawo. Iwo anayamba kupha Aisraeli monga poyamba paja, kotero kuti anapha anthu pafupifupi makumi atatu. Mitembo ya ena inali mu misewu yayikulu yopita ku Beteli ndi ku Gibeya, ndipo ina inali kwina poyera.
But the sons of Benjamin again burst forth boldly from the city. And since their enemies were fleeing, they pursued them a long way, so that they might wound or kill some of them, just as they had done on the first and second days. And they turned their backs along two paths, one bringing them toward Bethel, and the other toward Gibeah. And they struck down about thirty men.
32 Abenjamini ankanena kuti, “Tikuwagonjetsa monga poyamba.” Koma Aisraeli ankanena kuti, “Tiyeni tithawe kuti apite ku msewu chapatali ndi mzinda wawo.”
For they thought that they were falling back as they had done before. But instead, skillfully feigning flight, they undertook a plan to draw them away from the city, and by seeming to flee, to lead them along the above stated paths.
33 Choncho Aisraeli onse anachoka mʼmalo mwawo ndi kukandanda ku Baala-Tamara, ndipo Aisraeli obisalira aja anatuluka mʼmalo awo kummawa kwa Geba.
And so all the sons of Israel, rising up from their positions, set their troops in order, in the place which is called Baaltamar. Likewise, the ambushes that encircled the city began, little by little, to reveal themselves,
34 Aisraeli osankhidwa 10,000 ndiwo anabwera kudzalimbana ndi mzinda wa Gibeya. Nkhondoyo inafika poyipa kwambiri mwakuti Abenjamini samadziwa kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
and to advance upon the western part of the city. Moreover, another ten thousand men from all of Israel were provoking a conflict with the inhabitants of the city. And the war grew heavy against the sons of Benjamin. And they did not realize that, on all sides of them, death was imminent.
35 Tsono Yehova anagonjetsa Abenjamini pamaso pa Israeli motero kuti Aisraeli anapha ankhondo a Abenjamini 25,100 tsiku limenelo.
And the Lord struck them down in the sight of the sons of Israel, and they put to death, on that day, twenty-five thousand of them, along with one hundred men, all warriors and those who drew the sword.
36 Choncho Abenjamini anaona kuti agonjetsedwa. Paja Aisraeli anathawa fuko la Benjamini chifukwa ankadalira anthu amene anawayika kuti abisalire mzinda wa Gibeya.
But the sons of Benjamin, when they had seen themselves to be the weaker, began to flee. And the sons of Israel discerning this, gave them room to flee, so that they might arrive at the ambushes that were prepared, which they had positioned near the city.
37 Tsono anthu amene anabisala aja anachita changu kuwuthira nkhondo mzinda wa Gibeyawo. Ndipo anapha anthu onse a mu mzindawo ndi lupanga.
And after they had risen up suddenly from hiding, and those of Benjamin had turned their backs to those who cut them down, they entered the city, and they struck it with the edge of the sword.
38 Chizindikiro chimene Aisraeli anapangana ndi anthu obisalira aja chinali chakuti obisalira aja akangofukiza utsi wambiri ngati mtambo mu mzindamo,
Now the sons of Israel had given a sign to those whom they had stationed in ambushes, so that, after they had seized the city, they would light a fire, and by the smoke ascending on high, they would show that the city was captured.
39 ndiye kuti Aisraeli enawo abwerere ku nkhondo. Pa nthawiyo nʼkuti Abenjamini atayamba kale kumenya Aisraeliwo kwambiri ndi kupha pafupifupi anthu makumi atatu. Ndipo iwo ankanena kuti, “Ndithu tawapha monga poyamba paja.”
And then, the sons of Israel discerned this sign during the battle (for the sons of Benjamin had thought that they fled, and they pursued them forcefully, cutting down thirty men from their army).
40 Koma pamene utsi wa chizindikiro uja unayamba kukwera tolotolo mmwamba kuchoka mu mzindamo, Abenjamini anayangʼana mʼmbuyo ndipo anangoona utsi mu mzinda onse uli tolotolo kukwera mmwamba.
And they saw something like a pillar of smoke ascending from the city. Likewise, Benjamin, looking back, discerned that the city was captured, for the flames were being carried on high.
41 Kenaka Aisraeli anabwerera ndipo Abenjamini anachita mantha, chifukwa anaona kuti zoopsa zili pafupi kuwagwera.
And those who before had pretended to flee, turning their faces, withstood them more strongly. And when the sons of Benjamin had seen this, they turned their backs in flight,
42 Choncho anathawa pamaso pa Aisraeli kudzera njira ya ku chipululu, koma nkhondo inawapeza. Ndipo anaphedwa kumeneko ndi Aisraeli amene anachokera mu mzindamo.
and they began to go toward the way of the desert, with the adversary pursuing them to that place also. Moreover, those who had set fire to the city also met them.
43 Anawazungulira Abenjaminiwo, nawathamangitsa ndi kuwagonjetseratu osawachitira chifundo mpaka ku dera la kummawa kwa Gibeya.
And so it happened that they were cut down on both sides by the enemies, nor was there any respite for the dying. They were killed and struck down on the eastern side of the city of Gibeah.
44 Abenjamini 18,000 olimba mtima anaphedwa.
Now those who were put to death in the same place were eighteen thousand men, all very robust fighters.
45 Koma ena anatembenuka nathawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni. Mwa iwowa Aisraeli anapha Abenjamini 5,000 mʼmisewu yayikulu. Anawapitikitsabe Abenjaminiwo mpaka kufika ku Gidomu ndi kuphanso ena 2,000.
And when those who remained of Benjamin had seen this, they fled into the wilderness. And they were traveling toward the rock which is called Rimmon. In that flight also, among those who were scattering in different directions, they slew five thousand men. And though they scattered all the more, they continued to pursue them, and then they put to death another two thousand.
46 Pa tsiku limenelo Abenjamini olimba mtima okhala ndi malupanga okwana 25,000 anafa.
And so it happened that all of those who were slain from Benjamin, in various places, were twenty-five thousand fighters, very willing to go to war.
47 Koma anthu 700 anabwerera ndi kuthawira ku chipululu ku thanthwe la Rimoni kumene anakhalako miyezi inayi.
And so there remained from the entire number of Benjamin six hundred men who were able to escape and to flee into the wilderness. And they settled at the rock of Rimmon, for four months.
48 Aisraeli anabwerera kukamenyana ndi Abenjamini otsala ndi kuwapha ndi lupanga kuphatikizapo ziweto ndi zonse anali nazo. Ndipo anayatsa moto mizinda yonse anayipeza.
But the sons of Israel, returning, had struck with the sword all that remained in the city, from men even to cattle. And all the cities and villages of Benjamin were consumed with devouring flames.

< Oweruza 20 >