< Oweruza 2 >
1 Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
L’ange de Yahweh monta de Galgala à Bokim, et dit: « Je vous ai fait monter hors d’Égypte et je vous ai amenés dans le pays que j’ai juré à vos pères de vous donner. J’ai dit: Jamais je ne romprai mon alliance avec vous;
2 ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
et vous, vous ne ferez, pas alliance avec les habitants de ce pays, vous renverserez leurs autels. Mais vous n’avez pas obéi à ma voix. Pourquoi avez-vous fait cela?
3 Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
Et moi aussi, j’ai dit: Je ne les chasserai pas devant vous; ils seront à vos côtés, et leurs dieux vous seront un piège. »
4 Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
Comme l’ange de Yahweh disait ces paroles à tous les enfants d’Israël, le peuple éleva la voix et pleura.
5 ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
Ils donnèrent à ce lieu le nom de Bokim, et ils y offrirent des sacrifices à Yahweh.
6 Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
Josué renvoya le peuple, et les enfants d’Israël s’en allèrent chacun dans son héritage pour prendre possession du pays.
7 Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
Le peuple servit Yahweh pendant toute la vie de Josué, et pendant toute la vie des anciens qui survécurent à Josué et qui avaient vu toute la grande œuvre que Yahweh avait accomplie en faveur d’Israël.
8 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
Josué, fils de Nun, serviteur de Yahweh, mourut âgé de cent dix ans.
9 Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
On l’ensevelit dans le territoire qu’il avait eu en partage, à Thamnath-Hérès, dans la montagne d’Ephraïm, au nord du mont Gaas.
10 Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
Toute cette génération fut aussi recueillie auprès de ses pères, et il s’éleva après elle une autre génération qui ne connaissait pas Yahweh, ni l’œuvre qu’il avait faite en faveur d’Israël.
11 Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
Les enfants d’Israël firent ce qui est mal aux yeux de Yahweh, et ils servirent les Baals.
12 Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
Ils abandonnèrent Yahweh, le Dieu de leurs pères, qui les avait fait sortir du pays d’Égypte, et ils allèrent après d’autres dieux, d’entre les dieux des peuples qui les entouraient; ils se prosternèrent devant eux et ils irritèrent Yahweh.
13 Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
Abandonnant Yahweh, ils servirent Baal et les Astartés.
14 Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
La colère de Yahweh s’enflamma contre Israël; il les livra aux mains des pillards qui les pillèrent, et il les vendit entre les mains de leurs ennemis d’alentour, et ils ne purent plus tenir devant leurs ennemis.
15 Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
Partout où ils allaient, la main de Yahweh était contre eux pour leur malheur, comme Yahweh l’avait dit, comme Yahweh le leur avait juré, et ils en vinrent à une grande détresse.
16 Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
Yahweh suscitait des juges qui les délivraient de la main de ceux qui les pillaient.
17 Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
Mais ils n’écoutèrent pas leurs juges, car ils se prostituèrent à d’autres dieux et se prosternèrent devant eux. Ils se détournèrent promptement de la voie qu’avaient suivie leurs pères en obéissant aux commandements de Yahweh; ils ne firent pas de même.
18 Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
Lorsque Yahweh leur suscitait des juges, Yahweh était avec le juge et il les délivrait de la main de leurs ennemis, tant que le juge vivait; car Yahweh se repentait à cause de leurs gémissements devant ceux qui les opprimaient et les tourmentaient.
19 Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
Mais, à la mort du juge, ils se corrompaient de nouveau plus que leurs pères, en allant après d’autres dieux pour les servir et se prosterner devant eux; ils n’abandonnaient pas leurs errements et leur opiniâtreté.
20 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
Alors la colère de Yahweh s’enflamma contre Israël, et il dit: « Puisque cette nation a transgressé mon alliance que j’avais prescrite à ses pères, et puisqu’ils n’ont pas obéi à ma voix,
21 Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
moi, je ne chasserai plus devant eux une seule des nations que Josué a laissées quand il est mort,
22 Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
afin de mettre par elles Israël à l’épreuve, pour voir s’ils seront attentifs, ou non, à suivre la voie de Yahweh, comme leurs pères y ont été attentifs. »
23 Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.
Et Yahweh laissa en repos, sans se hâter de les chasser, ces nations qu’il n’avait pas livrées entre les mains de Josué.