< Oweruza 2 >

1 Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
and to ascend: rise messenger: angel LORD from [the] Gilgal to(wards) [the] Bochim and to say to ascend: establish [obj] you from Egypt and to come (in): bring [obj] you to(wards) [the] land: country/planet which to swear to/for father your and to say not to break covenant my with you to/for forever: enduring
2 ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
and you(m. p.) not to cut: make(covenant) covenant to/for to dwell [the] land: country/planet [the] this altar their to tear [emph?] and not to hear: obey in/on/with voice my what? this to make: do
3 Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
and also to say not to drive out: drive out [obj] them from face: before your and to be to/for you to/for side and God their to be to/for you to/for snare
4 Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
and to be like/as to speak: speak messenger: angel LORD [obj] [the] word [the] these to(wards) all son: descendant/people Israel and to lift: loud [the] people [obj] voice their and to weep
5 ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
and to call: call by name [the] place [the] he/she/it Bochim and to sacrifice there to/for LORD
6 Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
and to send: depart Joshua [obj] [the] people and to go: went son: descendant/people Israel man: anyone to/for inheritance his to/for to possess: take [obj] [the] land: country/planet
7 Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
and to serve: minister [the] people [obj] LORD all day Joshua and all day [the] old: elder which to prolong day after Joshua which to see: see [obj] all deed: work LORD [the] great: large which to make: do to/for Israel
8 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
and to die Joshua son: child Nun servant/slave LORD son: aged hundred and ten year
9 Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
and to bury [obj] him in/on/with border: boundary inheritance his in/on/with Timnath-heres Timnath-heres in/on/with mountain: hill country Ephraim from north to/for mountain: mount Gaash
10 Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
and also all [the] generation [the] he/she/it to gather to(wards) father his and to arise: rise generation another after them which not to know [obj] LORD and also [obj] [the] deed: work which to make: do to/for Israel
11 Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
and to make: do son: descendant/people Israel [obj] [the] bad: evil in/on/with eye: seeing LORD and to serve: minister [obj] [the] Baal
12 Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
and to leave: forsake [obj] LORD God father their [the] to come out: send [obj] them from land: country/planet Egypt and to go: follow after God another from God [the] people which around them and to bow to/for them and to provoke [obj] LORD
13 Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
and to leave: forsake [obj] LORD and to serve: minister to/for Baal and to/for Ashtaroth
14 Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
and to be incensed face: anger LORD in/on/with Israel and to give: give them in/on/with hand: to to plunder and to plunder [obj] them and to sell them in/on/with hand: power enemy their from around and not be able still to/for to stand: stand to/for face: before enemy their
15 Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
in/on/with all which to come out: come hand: power LORD to be in/on/with them to/for distress: harm like/as as which to speak: promise LORD and like/as as which to swear LORD to/for them and be distressed to/for them much
16 Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
and to arise: raise LORD to judge and to save them from hand: power to plunder them
17 Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
and also to(wards) to judge them not to hear: obey for to fornicate after God another and to bow to/for them to turn aside: turn aside quickly from [the] way: conduct which to go: walk father their to/for to hear: obey commandment LORD not to make: do so
18 Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
and for to arise: raise LORD to/for them to judge and to be LORD with [the] to judge and to save them from hand: power enemy their all day [the] to judge for to be sorry: comfort LORD from groan their from face: because to oppress them and to crowd them
19 Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
and to be in/on/with to die [the] to judge to return: turn back and to ruin from father their to/for to go: follow after God another to/for to serve: minister them and to/for to bow to/for them not to fall: fall from deed their and from way: conduct their [the] severe
20 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
and to be incensed face: anger LORD in/on/with Israel and to say because which to pass: trespass [the] nation [the] this [obj] covenant my which to command [obj] father their and not to hear: obey to/for voice my
21 Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
also I not to add: again to/for to possess: take man: anyone from face: before their from [the] nation which to leave: forsake Joshua and to die
22 Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
because to test in/on/with them [obj] Israel to keep: careful they(masc.) [obj] way: conduct LORD to/for to go: walk in/on/with them like/as as which to keep: obey father their if not
23 Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.
and to rest LORD [obj] [the] nation [the] these to/for lest to possess: take them quickly and not to give: give them in/on/with hand: power Joshua

< Oweruza 2 >