< Oweruza 2 >

1 Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
And an angel of the Lord went up from Galgal to the place of weepers, and said: I made you go out of Egypt, and have brought you into the land for which I swore to your fathers: and I promised that I would not make void my covenant with you for ever:
2 ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
On condition that you should not make a league with the inhabitants of this land, but should throw down their altars: and you would not hear my voice: why have you done this?
3 Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
Wherefore I would not destroy them from before your face: that you may have enemies, and their gods may be your ruin.
4 Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
And when the angel of the Lord spoke these words to all the children of Israel, they lifted up their voice, and wept.
5 ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
And the name of that place was called, The place of weepers, or of tears: and there they offered sacrifices to the Lord.
6 Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
And Josue sent away the people, and the children of Israel went every one to his own possession to hold it:
7 Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
And they served the Lord all his days, and the days of the ancients, that lived a long time after him, and who knew all the works of the Lord, which he had done for Israel.
8 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
And Josue the son of Nun, the servant of the Lord, died, being a hundred and ten years old,
9 Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
And they buried him in the borders of his possession in Thamnathsare in mount Ephraim, on the north side of mount Gaas.
10 Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
And all that generation was gathered to their fathers: and there arose others that knew not the Lord, and the works which he had done for Israel.
11 Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
And the children of Israel did evil in the sight of the Lord, and they served Baalim.
12 Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
And they left the Lord the God of their fathers, who had brought them out of the land of Egypt: and they followed strange gods, and the gods of the people that dwelt round about them, and they adored them: and they provoked the Lord to anger.
13 Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
Forsaking him, and serving Baal and Astaroth.
14 Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
And the Lord being angry against Israel, delivered them into the hands of plunderers: who took them and sold them to their enemies, that dwelt round about: neither could they stand against their enemies:
15 Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
But whithersoever they meant to go, the hand of the Lord was upon them, as he had said, and as he had sworn to them: and they were greatly distressed.
16 Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
And the Lord raised up judges, to deliver them from the hands of those that oppressed them: but they would not hearken to them,
17 Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
Committing fornication with strange gods, and adoring them. They quickly forsook the way, in which their fathers had walked: and hearing the commandments of the Lord, they did all things contrary.
18 Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
And when the Lord raised them up judges, in their days he was moved to mercy, and heard the groanings of the afflicted, and delivered them from the slaughter of the oppressors.
19 Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
But after the judge was dead, they returned, and did much worse things than their fathers had done, following strange gods, serving them and adoring them. They left not their own inventions, and the stubborn way, by which they were accustomed to walk.
20 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
And the wrath of the Lord was kindled against Israel, and he said: Behold this nation hath made void my covenant, which I had made with their fathers, and hath despised to hearken to my voice:
21 Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
I also will not destroy the nations which Josue left, when he died:
22 Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
That through them I may try Israel, whether they will keep the way of the Lord, and walk in it, as their fathers kept it, or not.
23 Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.
The Lord therefore left all these nations, and would not quickly destroy them, neither did he deliver them into the hands of Josue.

< Oweruza 2 >