< Oweruza 2 >

1 Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
Vstoupil pak anděl Hospodinův z Galgala do Bochim a řekl: Vyvedl jsem vás z Egypta a uvedl jsem vás do země, kterouž jsem s přísahou zaslíbil otcům vašim, a řekl jsem: Nezruším smlouvy své s vámi na věky.
2 ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
Vy také nečiňte smlouvy s obyvateli země této, oltáře jejich rozkopejte; ale neposlechli jste hlasu mého. Co jste to učinili?
3 Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
Pročež také jsem řekl: Nevyhladím jich před tváří vaší, ale budou vám jako trní, a bohové jejich budou vám osídlem.
4 Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
I stalo se, když mluvil anděl Hospodinův slova tato všechněm synům Izraelským, že pozdvihl hlasu svého lid a plakal.
5 ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
I nazvali jméno místa toho Bochim, a obětovali tu Hospodinu.
6 Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
Rozpustil pak byl Jozue lid, a rozešli se synové Izraelští, jeden každý do dědictví svého, aby vládli zemí.
7 Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
I sloužil lid Hospodinu po všecky dny Jozue, a po všecky dny starších, kteříž dlouho živi byli po Jozue, jenž viděli všecky skutky veliké Hospodinovy, kteréž učinil Izraelovi.
8 Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
Ale když umřel Jozue syn Nun, služebník Hospodinův, jsa ve stu a desíti letech,
9 Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
A pochovali ho v krajině dědictví jeho, v Tamnatheres, na hoře Efraim, k straně půlnoční hory Gás;
10 Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
Také když všecken věk ten připojen jest k otcům svým, a povstal jiný věk po nich, kteříž neznali Hospodina, ani skutků, kteréž učinil Izraelovi:
11 Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
Tedy činili synové Izraelští to, což jest zlého před očima Hospodinovýma, a sloužili modlám,
12 Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
Opustivše Hospodina Boha otců svých, kterýž je vyvedl z země Egyptské, a odešli za bohy cizími, bohy těch národů, kteříž byli vůkol nich, a klaněli se jim; pročež popudili Hospodina.
13 Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
Nebo opustivše Hospodina, sloužili Bálovi i Astarotům.
14 Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
I rozpálila se prchlivost Hospodinova na Izraele, a vydal je v ruku loupežníků, kteříž je zloupili; vydal je, pravím, v ruku nepřátel jejich vůkol, tak že nemohli více ostáti před nepřátely svými.
15 Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
Kamžkoli vycházeli, ruka Hospodinova byla proti nim ke zlému, jakož byl mluvil Hospodin, a jakož byl zapřisáhl jim Hospodin; i ssouženi byli náramně.
16 Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
Vzbuzoval pak Hospodin soudce, kteříž vysvobozovali je z rukou zhoubců jejich.
17 Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
Ale ani soudců svých neposlouchali, nebo smilnili, odcházejíce za bohy cizími, a klaněli se jim. Odcházeli rychle s cesty, po kteréž chodili otcové jejich, tak že poslouchati majíce přikázaní Hospodinových, nečinili toho.
18 Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
A když vzbuzoval jim Hospodin soudce, býval Hospodin s každým soudcím, a vysvobozoval je z ruky nepřátel jejich po všecky dny soudce; (nebo želel Hospodin naříkání jejich, k němuž je přivodili ti, kteříž je ssužovali a utiskali).
19 Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
Po smrti pak soudce navracejíce se zase, pohoršovali cest svých více nežli otcové jejich, odcházejíce za bohy cizími, a sloužíce i klanějíce se jim; nic neulevili z skutků jejich zlých a cesty jejich převrácené.
20 Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
Protož rozpálila se prchlivost Hospodinova proti Izraelovi, a řekl: Proto že přestoupil národ tento smlouvu mou, kterouž jsem učinil s otci jejich, a neposlouchali hlasu mého:
21 Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
Já také více nevyhladím žádného od tváři jejich z národů, kterýchž zanechal Jozue, když umřel,
22 Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
Abych skrze ně zkušoval Izraele, budou-li ostříhati cesty přikázaní Hospodinových, chodíce v nich, jakož ostříhali otcové jejich, čili nic.
23 Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.
I zanechal Hospodin národů těch, a nevyhnal jich rychle, aniž dal jich v ruku Jozue.

< Oweruza 2 >