< Oweruza 19 >

1 Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
I A manawa, aohe alii ma ka Iseraela, a e noho ana kekahi Levi ma kekahi aoao o ka mauna o Eperaima, lawe ia i haiawahine nana, noloko mai o Betelehemaiuda.
2 Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
Moe kolohe ku e mai la kana haiawahine ia ia, a hele aku, mai ona aku la, a i ka hale o kona makuakane, ma Betelehemaiuda, a malaila no ia i na malama eha.
3 Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
Ku ae la kana kane a hahai aku la ia ia, e olelo lokomaikai aku ia ia, a e hoihoi mai ia ia. Me ia pu no kana kauwa, a me na hoki elua. Hookomo aku la oia ia ia i ka hale o kona makuakane. A ike mai la ka makuakane o ua wahine la ia ia, olioli iho la oia, i ka halawai ana me ia.
4 Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
Kaohi ae la kona makuahonowaikane ia ia, o ka makuakane hoi o ua wahine la; a noho pu iho la oia me ia, i na la ekolu; a ai uo lakou, a inu, a moe iho la malaila.
5 Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
A hiki i ka ha o ka la, i ko lakou ala ana i kakahiaka nui, ku mai la ia e hele. I mai la ka makuakane o ka wahine i kana hunonakane, E hooluolu i kou naau me kahi berena iki, a mahope iho, e hele aku olua.
6 Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
Noho no laua, ai iho la, a inu pu hoi laua; no ka mea, ua olelo mai ka makuakane o ua wahine la i kela kanaka, E lealea mai oe i ka noho i keia po, a e hooluolu i kou naau.
7 Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
A i ke ala ana o ke kanaka e hele, koi mai la kona makuahonowaikane ia ia; nolaila, noho iho la ia ia po.
8 Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
I ka lima o ka la, ala ae la ia i kakahiaka nui, e hele. I mai la ka makuakane o ka wahine, E hooluolu paha oe i kou naau. Kakali iho la laua a auwi ae ka la, a ai iho la laua.
9 Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
A i ke ku ana o ke kanaka e hele, oia a me kana wahine, a me kana kauwa, alaila, olelo mai kona makuahonowaikane ia ia, o ka makuakane hoi o ua wahine la, Aia hoi, ua auwi ae ka la, ke noi aku nei au ia oe, e noho hou i keia po, kokoke po ka la, ea, e moe maanei i lealea kou naau; a apopo e hele oe i kakahiaka nui, a hoi aku i kou halelewa.
10 Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
Aole i ae mai ua kanaka la e moe ia po, aka, ku ae la ia a hele aku la, a hiki ma ke ala o Iebusa, oia hoi o Ierusalema; aia no me ia pu na hoki elua, i paa i na noho lio, a o kana wahine kekahi me ia.
11 Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
A kokoke lakou i Iebusa, ua auwi loa ka la, i ae la ke kauwa i kona haku, E kipa ae kakou i keia kulanakauhale o ko Iebusa, a moe ilaila.
12 Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
I mai la kona haku ia ia, Aole kakou e kipa ae ilaila, i ke kulanakauhale o kanaka e, aole no na mamo a Iseraela; e hele aku kakou, a Gibea.
13 Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
I mai la ia i kana kauwa, Ea, e hele aku kakou e moe i ka po ma Gibea, a i Rama paha.
14 Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
Hele aku la lakou i ko lakou wahi i hele ai; a ua po ka la ia lakou ma Gibea no Beniamina.
15 Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
Kipa ae la lakou e komo ilaila, e moe ai ma Gibea; a hiki aku la ia, noho iho la ma ke alanui o ke kulanakauhale; no ka mea, aohe kanaka nana lakou i hookipa i kona hale e moe ai.
16 Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
Aia hoi i ke ahiahi, hele mai kekahi kanaka elemakule, mai kana hana, mai ke kula mai, he kanaka no ka mauna o Eperaima, a noho iho la ma Gibea. Aka, no Beniamina na kanaka o ia wahi.
17 Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
Alawa ae la kona mau maka iluna, ike iho la i ke kanaka, he malihini ma ke alanui o ke kulanakauhale. I ae la ua kanaka elemakule nei, E hele ana oe ihea? a mai hea mai oe i hele mai ai?
18 Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
I mai la kela ia ia, E hele ana makou mai Betelehemaiuda a i na mokuna o ka mauna o Eperaima, nolaila hoi au, a hele aku au i Betelehemaiuda; a ke hoi aku nei au i ka hale o Iehova, aole hoi kanaka nana wau i hookipa ae i ka hale.
19 Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
He mauu no, a me ka ai na na hoki a makou, a he berena no a me ka waina na'u, a na kau kauwawahine, a na ke kanaka hou o kau mau kauwa nei; aohe mea e hemahema ai.
20 Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
I ae la ke kanaka elemakule, Aloha oe, aka, maluna o'u kou nele a pau; mai moe hoi ma ke alanui.
21 Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
Hookomo iho la oia ia ia i kona hale, hanai iho la i na hoki; a holoi no hoi lakou i ko lakou wawae, ai iho la, a inu hoi.
22 Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
A i ko lakou hoolealea ana i ko lakou naau, aia hoi na kanaka o ke kulanakauhale, he poe kanaka hewa, hoopuni mai la lakou i ka hale, a kikeke i ka puka, olelo mai i ka mea hale, i ua kanaka elemakule nei, i mai la, E lawe mai iwaho nei i ke kanaka i hele mai i kou hale, i ike makou ia ia.
23 Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
A o ke kanaka, ka haku o ka hale, hele aku la ia iwaho io lakou la, i aku la ia lakou, Ua oki, e na hoahanau, mai hana hewa oukou pela. Ua hele mai keia kanaka i ko'u hale, mai hana hoi oukou i keia mea lapuwale.
24 Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
Eia hoi ka'u kaikamahine, he puupaa, a me kana wahine no hoi, o laua ka'u e lawe mai iwaho nei, e hoohaahaa oukou ia laua, a e hana hoi ia laua i ka mea i pono i ko oukou mau maka; aka, mai hana ia mea lapuwale i keia kanaka.
25 Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
Aole hoolohe ia poe kanaka ia ia, Nolaila, lalau iho la ke kanaka i kana haiawahine, a lawe ia ia iwaho io lakou la, a ike mai la lakou ia ia, a hana ino lakou ia ia ia po a pau, a kakahiaka; a i ke ao ana ae, kuu mai la ia ia.
26 Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
I ka puka ana o ka malamalama, hele mai ua wahine la, a hina iho la ma ka puka o ka hale o ua kanaka la, ma kahi a kona haku, a malamalama ae la.
27 Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
Ala mai la kona haku i kakahiaka, a wehe ae la i ka puka o ka hale, a puka aku e hele ma kona ala; aia hoi, ua hina ka wahine ana ma ka puka o ka hale, aia hoi kona mau lima iluna o ka paepae.
28 Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
I aku la keia ia ia, E ala mai, e hele kaua. Aohe mea pane mai, Alaila, hapai ae la ua kanaka la ia ia, a kau iho la iluna o ka hoki Ku ae la ke kanaka a hoi aku la i kona wahi.
29 Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
A hiki aku la ia i kona hale, lawe ae la ia i ka pahi, a lalau aku la i kana haiawahine, a okioki iho la ia ia, a me kona mau iwi, i umikumamalua apana, a hoouna aku la ia mea, i na mokuna a pau o ka Iseraela.
30 Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”
Eia hoi, o ka poe a pau i ike ia mea, i ae la lakou, Aohe mea i hanaia e like me neia, aole hoi i ikeia, mai ka la i hele mai ai na mamo a Iseraela, mai ka aina o Aigupita mai, a hiki mai i neia la. E noonoo oukou ia mea, a e kukakuka iho, a e olelo mai.

< Oweruza 19 >