< Oweruza 19 >

1 Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
And it cometh to pass, in those days, when there is no king in Israel, that there is a man a Levite, a sojourner in the sides of the hill-country of Ephraim, and he taketh to him a wife, a concubine, out of Beth-Lehem-Judah;
2 Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
and commit whoredom against him doth his concubine, and she goeth from him unto the house of her father, unto Beth-Lehem-Judah, and is there days — four months.
3 Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
And her husband riseth and goeth after her, to speak unto her heart, to bring her back, and his young man [is] with him, and a couple of asses; and she bringeth him into the house of her father, and the father of the young woman seeth him, and rejoiceth to meet him.
4 Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
And keep hold on him doth his father-in-law, father of the young woman, and he abideth with him three days, and they eat and drink, and lodge there.
5 Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
And it cometh to pass, on the fourth day, that they rise early in the morning, and he riseth to go, and the father of the young woman saith unto his son-in-law, 'Support thy heart with a morsel of bread, and afterward ye go on.'
6 Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
And they sit and eat both of them together, and drink, and the father of the young woman saith unto the man, 'Be willing, I pray thee, and lodge all night, and let thy heart be glad.'
7 Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
And the man riseth to go, and his father-in-law presseth on him, and he turneth back and lodgeth there.
8 Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
And he riseth early in the morning, on the fifth day, to go, and the father of the young woman saith, 'Support, I pray thee, thy heart;' and they have tarried till the turning of the day, and they eat, both of them.
9 Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
And the man riseth to go, he and his concubine, and his young man, and his father-in-law, father of the young woman, saith to him, 'Lo, I pray thee, the day hath fallen toward evening, lodge all night, I pray thee; lo, the declining of the day! lodge here, and let thine heart be glad — and ye have risen early to-morrow for your journey, and thou hast gone to thy tent.'
10 Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
And the man hath not been willing to lodge all night, and he riseth, and goeth, and cometh in till over-against Jebus (It [is] Jerusalem), and with him [are] a couple of asses saddled; and his concubine [is] with him.
11 Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
They [are] near Jebus, and the day hath gone greatly down, and the young man saith unto his lord, 'Come, I pray thee, and we turn aside unto this city of the Jebusite, and lodge in it.'
12 Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
And his lord saith unto him, 'Let us not turn aside unto the city of a stranger, that is not of the sons of Israel, thither, but we have passed over unto Gibeah.'
13 Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
And he saith to his young man, 'Come, and we draw near to one of the places, and have lodged in Gibeah, or in Ramah.'
14 Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
And they pass over, and go on, and the sun goeth in upon them near Gibeah, which is to Benjamin;
15 Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
and they turn aside there to go in to lodge in Gibeah, and he goeth in and sitteth in a broad place of the city, and there is no man gathering them into the house to lodge.
16 Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
And lo, a man, an aged one, hath come from his work from the field in the evening, and the man [is] of the hill-country of Ephraim, and he [is] a sojourner in Gibeah, and the men of the place [are] Benjamites.
17 Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
And he lifteth up his eyes, and seeth the man, the traveller, in a broad place of the city, and the aged man saith, 'Whither goest thou? and whence comest thou?'
18 Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
And he saith unto him, 'We are passing over from Beth-Lehem-Judah unto the sides of the hill-country of Ephraim — thence I [am], and I go unto Beth-Lehem-Judah; and to the house of Jehovah I am going, and there is no man gathering me into the house,
19 Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
and both straw and provender are for our asses, and also bread and wine there are for me, and for thy handmaid, and for the young man with thy servants; there is no lack of anything.'
20 Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
And the old man saith, 'Peace to thee; only, all thy lack [is] on me, only in the broad place lodge not.'
21 Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
And he bringeth him in to his house, and mixeth [food] for the asses, and they wash their feet, and eat and drink.
22 Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
They are making their heart glad, and lo, men of the city, men — sons of worthlessness — have gone round about the house, beating on the door, and they speak unto the old man, the master of the house, saying, 'Bring out the man who hath come unto thine house, and we know him.'
23 Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
And the man, the master of the house, goeth out unto them, and saith unto them, 'Nay, my brethren, do not evil, I pray you, after that this man hath come in unto my house, do not this folly;
24 Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
lo, my daughter, the virgin, and his concubine, let me bring them out, I pray you, and humble ye them, and do to them that which is good in your eyes, and to this man do not this foolish thing.'
25 Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
And the men have not been willing to hearken to him, and the man taketh hold on his concubine, and bringeth [her] out unto them without, and they know her, and roll themselves upon her all the night, till the morning, and send her away in the ascending of the dawn;
26 Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
and the woman cometh in at the turning of the morning, and falleth at the opening of the man's house, where her lord [is], till the light.
27 Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
And her lord riseth in the morning, and openeth the doors of the house, and goeth out to go on his way, and lo, the woman, his concubine, is fallen at the opening of the house, and her hands [are] on the threshold,
28 Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
and he saith unto her, 'Rise, and we go;' and there is none answering, and he taketh her on the ass, and the man riseth and goeth to his place,
29 Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
and cometh in unto his house, and taketh the knife, and layeth hold on his concubine, and cutteth her in pieces to her bones — into twelve pieces, and sendeth her into all the border of Israel.
30 Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”
And it hath come to pass, every one who seeth hath said, 'There hath not been — yea, there hath not been seen like this, from the day of the coming up of the sons of Israel out of the land of Egypt till this day; set your [heart] upon it, take counsel, and speak.'

< Oweruza 19 >