< Oweruza 19 >
1 Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
Now in those days, when there was no king in Israel, a certain Levite was living in the inmost parts of the hill-country of Ephraim, and he got for himself a servant-wife from Beth-lehem-judah.
2 Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
And his servant-wife was angry with him, and went away from him to her father's house at Beth-lehem-judah, and was there for four months.
3 Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
Then her husband got up and went after her, with the purpose of talking kindly to her, and taking her back with him; he had with him his young man and two asses: and she took him into her father's house, and her father, when he saw him, came forward to him with joy.
4 Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
And his father-in-law, the girl's father, kept him there for three days; and they had food and drink and took their rest there.
5 Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
Now on the fourth day they got up early in the morning and he made ready to go away; but the girl's father said to his son-in-law, Take a little food to keep up your strength, and then go on your way.
6 Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
So seating themselves they had food and drink, the two of them together; and the girl's father said to the man, If it is your pleasure, take your rest here tonight, and let your heart be glad.
7 Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
And the man got up to go away, but his father-in-law would not let him go, so he took his rest there again for the night.
8 Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
Then early on the morning of the fifth day he got up to go away; but the girl's father said, Keep up your strength; so the two of them had a meal, and the man and his woman and his servant did not go till after the middle of the day.
9 Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
And when they got up to go away, his father-in-law, the girl's father, said to him, Now evening is coming on, so do not go tonight; see, the day is almost gone; take your rest here and let your heart be glad, and tomorrow early, go on your way back to your house.
10 Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
But the man would not be kept there that night, and he got up and went away and came opposite to Jebus (which is Jerusalem); and he had with him the two asses, ready for travelling, and his woman.
11 Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
When they got near Jebus the day was far gone; and the servant said to his master, Now let us go from our road into this town of the Jebusites and take our night's rest there.
12 Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
But his master said to him, We will not go out of our way into a strange town, whose people are not of the children of Israel; but we will go on to Gibeah.
13 Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
And he said to his servant, Come, let us go on to one of these places, stopping for the night in Gibeah or Ramah.
14 Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
So they went on their way; and the sun went down when they were near Gibeah in the land of Benjamin.
15 Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
And they went off the road there with the purpose of stopping for the night in Gibeah: and he went in, seating himself in the street of the town, for no one took them into his house for the night.
16 Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
Now when it was evening they saw an old man coming back from his work in the fields; he was from the hill-country of Ephraim and was living in Gibeah: but the men of the place were Benjamites.
17 Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
And when he saw the traveller in the street of the town, the old man said, Where are you going? and where do you come from?
18 Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
And he said to him, We are on our way from Beth-lehem-judah to the inmost parts of the hill-country of Ephraim: I came from there and went to Beth-lehem-judah: now I am on my way back to my house, but no man will take me into his house.
19 Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
But we have dry grass and food for our asses, as well as bread and wine for me, and for the woman, and for the young man with us: we have no need of anything.
20 Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
And the old man said, Peace be with you; let all your needs be my care; only do not take your rest in the street.
21 Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
So he took them into his house and gave the asses food; and after washing their feet they took food and drink.
22 Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
While they were taking their pleasure at the meal, the good-for-nothing men of the town came round the house, giving blows on the door; and they said to the old man, the master of the house, Send out that man who came to your house, so that we may take our pleasure with him.
23 Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
So the man, the master of the house, went out to them, and said, No, my brothers, do not this evil thing; this man has come into my house, and you are not to do him this wrong.
24 Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
See, here is my daughter, a virgin, and his servant-wife: I will send them out for you to take them and do with them whatever you will. But do no such thing of shame to this man.
25 Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
But the men would not give ear to him: so the man took his woman and sent her out to them; and they took her by force, using her for their pleasure all night till the morning; and when dawn came they let her go.
26 Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
Then at the dawn of day the woman came, and, falling down at the door of the man's house where her master was, was stretched there till it was light.
27 Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
In the morning her master got up, and opening the door of the house went out to go on his way; and he saw his servant-wife stretched on the earth at the door of the house with her hands on the step.
28 Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
And he said to her, Get up and let us be going; but there was no answer; so he took her up and put her on the ass, and went on his way and came to his house.
29 Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
And when he had come to his house, he got his knife, and took the woman, cutting her up bone by bone into twelve parts, which he sent through all Israel.
30 Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”
And he gave orders to the men whom he sent, saying, This is what you are to say to all the men of Israel, Has ever an act like this been done from the day when the children of Israel came out of Egypt to this day? Give thought to it, turning it over in your minds, and give your opinion of it.