< Oweruza 19 >

1 Pa nthawi imeneyo ku Israeli kunalibe mfumu. Mlevi wina ankakhala kutali ku dziko lamapiri la Efereimu. Iyeyu anatenga mzikazi wa ku Betelehemu, mʼdziko la Yuda.
Te vaeng tue ah khaw Israel ah he manghai tal pueng. Te dongah Ephraim tlang hlaep ah aka kuep Levi hlang loh Judah Bethlehem lamkah huta pakhat te yula la a loh.
2 Tsiku lina mzikazi uja anakwiyira mwamuna wake ndipo anamuchokera kupita kwa abambo ake ku Betelehemu mʼdziko la Yuda. Anakakhala kumeneko miyezi inayi.
Tedae anih taengkah a yula tah a cukhalh dongah a va taeng lamloh a napa im Judah Bethlehem la cet tih hla li om.
3 Mwamuna wake anamulondola kuti akayankhule naye mofatsa kumupempha kuti abwerere. Iye anali ndi antchito ake ndi abulu ake awiri. Anafika ku nyumba kwa mkazi uja ndipo iye anamulowetsa mʼnyumba ya abambo ake. Abambo aja atamuona mnyamata uja anamulandira mwachimwemwe.
Te dongah a yuu te ha mael khaw ha mael laeh saeh tila a lungbuei te yam pah ham a va te thoo tih a yuu taengla cet. Te vaengah amah taengkah cadong pakhat neh laak rhoi te a khuen. A va te a napa im a paan puei tih huta kah a napa loh a hmuh hatah anih doe ham a kohoe.
4 Mpongozi wake, yemwe anali abambo a mtsikanayo, anamupempha kuti aswere. Choncho anakhalako masiku atatu. Ankadya, kumwa ndi kugona komweko.
Tedae huta kah a napa, khosoih masae loh a parhaeng. Te dongah hnin thum a om puei hatah a caak a ok uh tih rhaeh uh.
5 Tsiku lachinayi anadzuka mʼmamawa kukonzekera kuti azipita kwawo, koma abambo ake a mtsikanayo anawuza mkamwini wawo uja kuti, “Yambani mwadya chakudya, ndipo kenaka mutha kupita.”
Hnin li a om nen tah mincang ah thoo tih caeh hamla hlah uh bal. Tedae huta kah a napa loh a cava te, “Buh kamat nen khaw na lungbuei duel lamtah a hnuk la cet mai,” a ti nah.
6 Choncho onse awiri anakhala pansi ndi kudya ndi kumwa pamodzi. Atadya, abambo a mtsikanayo anati, “Chonde mugonenso konkuno musangalale.”
Te dongah ngol rhoi tih thikat la a caak a ok rhoi. Te vaengah tekah hlang te huta kah a napa loh, “Ueh mai lamtah na lungbuei voelphoeng la rhaeh rhoi mai dae,” a ti nah.
7 Ndipo pamene mwamunayo anakonzeka kuti azipita, apongozi ake anamuwumirizanso kuti asapite. Choncho anagona komweko usiku umenewo.
Tekah hlang loh caeh hamla thoo bal coeng dae a masae loh a hloep dongah mael tih hnap rhaeh.
8 Mmawa wa tsiku lachisanu, atadzuka kuti azipita abambo ake a mtsikanayo anamuwuza kuti, “Yambani mwadya chakudya ndipo mutandale mpaka madzulo.” Choncho awiriwo anadya pamodzi.
A hnin nga mincang ah caeh hamla thoo bal. Te vaengah huta kah a napa loh, “Na thinko duel rhoi dae lamatah khovoei duela rhing rhoi mai,” a ti nah. Te dongah amih rhoi long te buh koep a caak rhoi bal.
9 Pambuyo pake munthu uja pamodzi ndi mzikazi wake ndiponso mtumiki anakonzeka kuti azipita. Koma abambo a mtsikana uja anatinso kwa iye, “Onani tsopano kukuda. Gonani konkuno pakuti tsiku latha kale. Gonani ndipo musangalale. Mawa mudzuka mʼmamawa ndi kumapita kwanu.”
Te phoeiah caeh hamla a yula neh cadong te a thoh puei hatah hula kah a napa, a napa loh, “Kholaeh ham khohnin loh khum coeng ta, khohnin loh thok coeng tih pahoi rhaeh rhoi mai lamtah na thinko voelphoeng sak rhoi mai, na longpuei te thangvuen ah na thoh thil vetih na dap khaw na paan bitni,” a ti nah.
10 Koma munthuyo sanafune kugonanso tsiku limenelo. Choncho ananyamuka kumapita, ndipo anakafika ku malo oyangʼanana ndi Yebusi (ndiye kuti Yerusalemu). Iyeyo anali atatenga abulu ake awiri okhala ndi zokhalira zake, ndipo mzikazi wake uja anali naye limodzi.
Tedae rhaeh hamla hlang loh a huem pawt dongah thoo tih nong. Te vaengah amah taengah a khih laak rhoi neh a taengkah a yula te Jerusalem kah Jebus dan la a pawk puei.
11 Akuyandikira ku Yebusi nʼkuti kutada ndithu. Tsono mtumiki uja anawuza mbuye wake kuti, “Tiyeni, tipatukire ku mzinda wa Ayebusiwa ndipo tigone.”
Jebus taengah tah khohnin khaw dalh thok tih a boei te cadong loh, “Cet uh sih lamtah Jebusi khopuei la ng'ael phoeiah rhaeh uh sih,” a ti nah.
12 Mbuye wake anamuyankha kuti, “Ayi, tisapatukire ku mzinda wa alendo, anthu amene sali Aisraeli. Koma tipitirire mpaka ku Gibeya.”
Tedae anih te a boei loh, “Kholong kho la ael boel sih, amih te Israel ca moenih, te dongah Gibeah la cet uh mai sih,” a ti nah.
13 Tsono anamuwuza mtumiki wake uja kuti, “Tiye tipite ku amodzi a malo awa, ku Gibeya kapena ku Rama ndipo tikagone kumeneko.”
Te phoeiah cadong te, “Cet sih lamtah a hmuen pakhat te moeh sih, Gibeah ah khaw Ramah ah khaw rhaeh uh mai sih,” a ti nah.
14 Choncho nayenda ulendo wawo, ndipo dzuwa linawalowera akuyandikira ku Gibeya mʼdziko la Benjamini.
Te dongah cet uh tih Benjamin khuikah Gibeah taengah a pha tom ah kho tla coeng.
15 Ndipo anapatukira kumeneko kuti alowe mu mzinda wa Gibeya kukagona usiku umenewo. Anakalowa mu mzindamo ndi kukakhala pabwalo popeza panalibe munthu amene anawalandira ku nyumba kwake kuti akagone.
Te dongah pahoi kun ham neh Gibeah ah rhaeh ham khaw paa uh. Te phoeiah cet uh tih khopuei toltung ah ngol uh. Tedae im khuila pah sak ham amih te hlang loh voek pawh.
16 Pambuyo pake anangoona munthu wina wokalamba akuchokera ku ntchito ya ku munda kwake madzulo. Iyeyu anali wa ku dziko la mapiri ku Efereimu, koma ankakhala ku Gibeya. Koma anthu a kumeneko anali a fuko la Benjamini.
Hlaem vaengah patong pakhat tah lohma lamkah a bibi lamkah lawt halo. Tedae anih khaw Benjamin ca rhoek kah hmuen Gibeah ah aka bakuep Ephraim tlang lamkah hlang van ni.
17 Munthu wokalamba uja anakweza maso ndipo anaona munthu wa paulendo uja atakhala pabwalo la mzindawo, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi mukupita kuti? Nanga mukuchokera kuti?”
Patong loh a mik a huel a sawt hatah khopuei toltung ah yincet hlang pakhat te a hmuh. Te dongah tekah hlang te patong loh, “Me lamkah lae na lo tih melam na caeh eh?,” a ti nah.
18 Iye anayankha kuti, “Tikuchokera ku Betelehemu ku dziko la Yuda ndipo tikupita kutali ku dziko lamapiri la Efereimu kumene ndimakhala. Ndinapita ku Betelehemu mʼdziko la Yuda ndipo tsopano ndikubwerera kwathu. Koma palibe aliyense amene wanditengera ku nyumba yake.
Te dongah, “Kaimih tah Judah Bethlehem lamkah Ephraim tlang hlaep la ka cet uh. Te lamkah te Judah Bethlehem la ka cet uh tih BOEIPA im ka paan. Tedae im khuila kai aka pah sak ham hlang om pawh.
19 Tili ndi udzu ndi chakudya cha abulu athu. Tilinso ndi buledi ndi vinyo wokwanira ifeyo: ine, mdzakazi wanuyu, ndi mtumiki amene ali nafeyu. Palibe chimene tikusowa.”
Tahae ah ka laak ham cangkong neh a kamvuelh khaw om pueng. Kamah ham neh na salnu ham khaw, na sal taengkah cadong ham khaw buh neh misurtui om pueng tih hnopai dongah pakhat khaw a tloelnah om pawh,” a ti nah.
20 Munthu wokalambayo anati, “Mtendere ukhale nanu. Ine ndikuthandizani pa zosowa zanu zonse, koma musagone pabwalo usiku uno.”
Te dongah tekah hlang te patong loh, “Nang taengah ngaimongnah om saeh. Na tloelnah boeih nen khaw kai taengah om mai toltung ah rhaehba boeh,” a ti nah.
21 Choncho anapita nawo ku nyumba yake, ndipo anawapatsa abulu ake chakudya. Alendo aja anasamba mapazi awo, nalandira chakudya ndi chakumwa.
Yin te a im khuila a khuen tih laak a vuelh pah, a kho a silh pah phoeiah a caak a ok uh.
22 Pamene ankadya mosangalala, anangoona anthu ena achabechabe a mu mzindawo azungulira nyumba ija nʼkumamenya chitseko. Tsono anawuza mwini nyumbayo, munthu wokalamba uja kuti, “Mutulutse munthu amene wabwera mʼnyumba yakoyu kuti tigone naye.”
A lungbuei a voelphoeng uh li vaengah khopuei hlang khui hlang muen ca rhoek loh im te tarha a vael uh tih thohkhaih te a tum uh. Im kung patong te khaw a doek uh uh tih, “Na im la aka pawk hlang te hang khuen lamtah anih ka hmat uh lah eh,” a ti nah.
23 Koma mwini nyumba uja anatuluka ku bwalo nawawuza kuti, “Ayi, abale anga musachite zoyipa zotere. Popeza munthu uyu walowa mʼnyumba mwanga muno, musachite chinthu chonyansa chotere.
Tedae im kung te amih taengla ha moe tih, “Ka manuca rhoek nang te tlam moenih, hekah hlang he ka im khuila ha kun coeng dongah thaehuet uh boel mai, boethae halang he tah saii uh boeh.
24 Onani, pano pali mwana wanga wamkazi wosadziwa mwamuna pamodzi ndi mzikazi wa mlendoyu. Ndikutulutsirani amenewa tsopano ndipo atengeni ndi kuchita nawo chomwe chikukomerani. Koma musachite chinthu chonyansa ndi munthuyu.”
Ka canu, oila neh ka yula kang khuen mai eh. Amih phaep uh lamtah na mik dongah then na ti uh bangla amih rhoi taengah saii uh. Tedae hekah hlang taengah boethae halang hno te saii uh boeh,” a ti nah.
25 Koma anthuwo sanafune kumumvera. Choncho mlendo uja anagwira mzikazi wake namutulutsa kuja kumene kunali iwo. Tsono iwowo anagona naye ndi kuchita naye zonyansa usiku wonse mpaka mmawa. Mʼbandakucha anamulola kuti apite.
Tedae hlang loh hnatun ham a huem uh pawt dongah khosoih loh a yula te a mawt tih amih taengah poeng la a thak pah. Te vaengah anih te a tholh puei uh tih khoyin khing te mincang duela a poelyoe uh. Khothaih a pha daengah huta te a hlah uh.
26 Ndipo mmawa kukucha mzikazi uja anabwerera nakagwa pansi pa khomo pa nyumba imene mwamuna wake anali, ndipo anakhala pomwepo mpaka kunayera.
Mincang a pha vaengah tah huta te cet tih a boei a om nah im kah thohka ah khosae duela hmawk sop uh.
27 Mwamuna wake anadzuka mʼmamawa, natsekula chitseko cha nyumba kuti atuluke ndi kumapita. Koma anangoona mzikazi wake uja ali thapsa pa khomo la nyumbayo, manja ake ali pa khonde.
A boei te mincang ah thoo tih im thohkhaih te a ong. Amah kho long ah voei ham ha moe phai hatah a yula te im thohka kah cingkhaa dongah kut a tloeng tih lawt ana bakop pah.
28 Iye anati kwa mkaziyo, “Dzuka tizipita.” Koma sanayankhe kanthu. Kenaka anamukweza pa bulu wake ndipo ananyamuka kumapita kwawo.
Te dongah anih te, “Thoo lamtah cet pawn sih,” a ti nah. Tedae a doo voel pawt dongah laak dongla a khueh. Te phoeiah tekah hlang te thoo tih a hmuen a paan.
29 Atafika ku nyumba yake, anatenga mpeni, nagwira mzikazi wake uja ndi kuduladula thupi lake nthuli khumi ndi ziwiri. Kenaka anazitumiza ku zigawo zonse za Israeli.
Amah im la a pawk vaengah tah tumcaca a loh tih a yula te a tloeng. Te phoeiah a rhuh te maehpoel hlai nit la a tloek tih Israel khorhi takuem ah a pat.
30 Aliyense amene anaona zimenezi ankanena kuti, “Zoterezi sizinaonekepo kuyambira pamene Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto mpaka lero lino. Ganizirani bwino chinthu chimenechi ndipo tiwuzeni zoyenera kuchita!”
Te tla aka om te boeih a hmuh uh vaengah, “Egypt kho lamkah n'thoo uh hnin lamkah loh tihnin duela te bang te Israel ca rhoek taengah om pawt tih hmuh noek bal moenih. He he nangmih loh dueh uh, anih he dawtlet uh lamtah thui uh,” a ti nah.

< Oweruza 19 >