< Oweruza 18 >

1 Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
Того ча́су не було царя в Ізраїлі, і того ча́су Данове пле́м'я шукало собі наді́лу на оселю, бо до того дня не випало йому жеребка́ на наді́л серед Ізраїлевих племе́н.
2 Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
І Данові сини послали зо свого ро́ду п'ятеро люда з загалу́ людей військо́вих, щоб вони вивідали Край та дослідили його. І сказали до них: „Ідіть, дослідіть цей Край“. І вони зійшли на Єфремові гори аж до Михиного дому, і переночували там.
3 Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
Коли вони були біля Михиного дому, то вони пізнали голос того юнака Левита, та й зайшли туди й сказали йому: „Хто тебе привів сюди, і що́ ти тут робиш? І що́ ти тут маєш?“
4 Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
І сказав він до них: „Так і так зробив мені Миха, — і він найняв мене, і я став йому за священика“.
5 Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
А вони сказали йому: „Запитай же Бога, і нехай ми пізнаємо, чи пощаститься наша дорога, якою ми йдемо́“.
6 Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
І сказав їм священик: „Ідіть із ми́ром, — перед Господом ваша дорога, якою ви пі́дете“.
7 Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
І пішли ті п'ятеро людей, і прийшли в Лаїш та й побачили той народ, що в ньому, — він сидить безпечно, за зви́чаєм сидо́нян, спокійний та безпечний. І не було ніко́го, хто робив би їм щось зле в Краю́, посів би вла́ду над ними, і вони дале́ко від сидо́нян, і нема їм ді́ла ні до кого.
8 Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
І прийшли вони до братів своїх у Цор'у та в Ештаол. І сказали їм брати їх: „Що́ ви прине́сли?“
9 “Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
А вони відказали: „Устаньте, і пі́демо на них, бо ми бачили той Край, і ось — дуже він добрий. А ви мовчите́? Не лініться, щоб піти, щоб прийти та посісти той Край.
10 Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
Як ви пі́дете, то ввійдете до народу безпечного, а Край той широкий, — бо Бог дав його в вашу ру́ку, — це місце, що там нема недостачі жодної речі, що на землі“.
11 Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
І рушили звідти з Данового роду з Цор'и та з Ештаолу шістсот чоловіка, опере́заних збро́єю.
12 Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
І пішли вони й таборува́ли в Кір'ят-Єарімі в Юді. Тому вони назвали ім'я тому місцю: Махане-Дан, і так воно зветься аж до цього дня, — оце за Кір'ят-Єарімом.
13 Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
І перейшли вони звідти на Єфремові го́ри, і прийшли аж до Михиного дому.
14 Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
І відповіли п'ятеро тих мужів, що ходили ви́відати той Край до Лаїшу, і сказали своїм бра́ттям: „Чи ви знаєте, що в цих домах є ефо́д та тера́фи, і бовва́н рі́зьблений та бовван литий? А тепер знайте, що́ зробите“.
15 Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
І вони зайшли туди до дому того юнака Левита, до Михиного дому, і запитали його про мир.
16 Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
А шість сотень мужа, що з Данових синів, опере́заних своєю зброєю, стояли при вході до брами.
17 Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
І пішли п'ятеро тих мужів, що ходили ви́відати той Край, увійшли туди, узяли рі́зьбленого боввана, і ефо́да та тера́фи, і боввана литого. А при вході до брами стояв священик та шістсот мужа, опере́заних зброєю.
18 Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
І ті ввійшли до Михиного дому, і взяли рі́зьбленого боввана, ефода й терафи та боввана литого. І сказав до них той священик: „Що́ ви робите?“
19 Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
А вони відказали йому: „Мовчи! Поклади свою руку на уста свої та й іди з нами, і стань нам за отця та за священика. Чи тобі ліпше бути священиком дому одно́го чоловіка, чи бути тобі священиком для пле́мени та для роду Ізра́їлевого?“
20 Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
І стало добре на серці того священика, і він узяв ефо́да та тера́фи й рі́зьбленого боввана, і ввійшов поміж народ.
21 Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
І повернулися вони та й пішли, а дітей, і худобу, і тяга́р пустили перед себе.
22 Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
Коли вони віддали́лися від Михиного дому, то люди, що в дома́х, які разом із домом Михиним, були скликані, та й догнали Данових синів.
23 Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
І кричали вони до Данових синів, а ті обернули обличчя свої та й сказали до Михи: „Що́ тобі, що ти кричиш?“
24 Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
І він сказав: „Ви забрали бога мого, що я зробив, та священика, та й пішли. І що мені ще? І що то ви говорите мені: що тобі?“
25 Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
І сказали до нього Данові сини: „Мовчи, щоб не чути нам твого голосу, а то наші люди із зло́сти нападуть на вас, і ти долучиш душу свою до своєї рідні.
26 Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
І Данові сини пішли на свою дорогу. І побачив Миха, що вони сильніші від нього, і обернувся, та й пішов до свого дому.
27 Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
А вони взяли́, що́ зробив був Миха, та священика, що був у нього, та й пішли на Лаїш, на народ спокійний та безпечний. І вони побили їх ві́стрям меча, а місто спалили огнем.
28 Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
А рятівника́ не було, бо далеке воно від Сидону, і не було в них ді́ла ні з ким, і воно було в долині, що при Бет-Рехові. А вони збудували місто, та й осілися в ньому.
29 Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
І вони назвали ім'я́ тому містові: Дан, іменем Дана, їхнього батька, що був уроджений Ізраїлеві, але напочатку ім'я́ того міста було Лаїш.
30 Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
І поставили Данові сини того рі́зьбленого боввана в себе, а Йоната́н, син Ґершома, Манасіїного сина, він та сини його були священиками для Данового племени аж до дня ви́ходу на вигна́ння того кра́ю.
31 Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.
І поклали вони в себе Михиного рі́зьбленого боввана, що зробив він, і він був у них по всі дні буття Божого дому в Шіло́.

< Oweruza 18 >