< Oweruza 18 >

1 Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
I de Dage var der ingen Konge i Israel, og i de Dage var Daniternes Stamme i Færd med at søge sig en Arvelod, hvor de kunde bo, thi hidindtil var der ikke tilfaldet dem nogen Arvelod blandt Israels Stammer.
2 Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
Daniterne udtog da af deres Slægt fem stærke Mænd fra Zora og Esjtaol og udsendte dem for at udspejde og undersøge Landet, og de sagde til dem: "Drag hen og undersøg Landet!" De kom da til Mikas Hus i Efraims Bjerge og overnattede der.
3 Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
Da de kom i Nærheden af Mikas Hus og kendte den unge Levits Stemme, tog de derind og spurgte ham: "Hvem har ført dig herhen, hvad tager du dig for på dette Sted, og hvorfor er du her?"
4 Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
Han svarede dem: "Det og det har Mika gjort for mig; han har lejet mig til Præst."
5 Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
Da sagde de til ham: "Adspørg da Gud, at vi kan få at vide, om vor Færd skal lykkes!"
6 Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
Præsten sagde da til dem: "Far med Fred, HERREN våger over eders Færd!"
7 Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
Så drog de fem Mænd videre og kom til Lajisj; og de så, at Byen levede trygt på Zidoniernes Vis, at Folket der levede sorgløst og trygt og ikke manglede nogen Verdens Ting, men var rigt, og at de boede langt fra Zidonierne og intet havde med Aramæerne at gøre.
8 Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
Da de kom tilbage til deres Brødre i Zora og Esjtaol, spurgte disse dem: "Hvad har I at melde?"
9 “Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
De svarede: "Kom, lad os drage op til Lajisj, thi vi har set Landet, og se, det er såre godt! Hvorfor holder I eder uvirksomme? Nøl ikke med at drage hen og underlægge eder Landet!
10 Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
Thi Gud bar givet det i eders Hånd et Sted, hvor der ikke er Mangel på nogen Verdens Ting! Når l kommer derhen, kommer I til et Folk, der lever i Tryghed, og det er et vidtstrakt Land!"
11 Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
Så brød 600 væbnede Mænd af Daniternes Slægt op fra Zora og Esjtaol,
12 Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
og de drog op og slog Lejr i Kirjat Jearim i Juda; derfor kalder man endnu den Dag i Dag dette Sted hans Lejr; det ligger vesten for Kirjat Jearim.
13 Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
Derfra drog de over til Efraims Bjerge; og da de kom til Mikas Hus,
14 Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
tog de fem Mænd, der havde været henne at udspejde Landet, til Orde og sagde til deres Brødre: "Ved I, at der i Husene her findes en Efod, en Husgud og et udskåret og støbt Billede? Så indser I vel, hvad I har at gøre!"
15 Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
De begav sig derhen og kom til den unge Levits Hus, Mikas Hus, og hilste på ham,
16 Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
medens de 600 væbnede danitiske Mænd stod ved Porten.
17 Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
Og de fem Mænd, der havde været henne at udspejde Landet, gik op og tog det udskårne og støbte Billede, Efoden og Husguden, medens Præsten og de 600 væbnede Mænd stod ved Porten.
18 Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
Hine gik ind i Mikas Hus og tog det udskårne og støbte Billede, Efoden og Husguden. Præsten sagde til dem: "Hvad er det, I gør?"
19 Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
Og de svarede ham: "Stille, læg Fingeren på Munden og følg med os og bliv vor Fader og Præst! Hvad båder dig vel bedst, at være Præst for een Mands Hus eller for en Stamme og Slægt i Israel?"
20 Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
Da blev Præsten glad, tog Efoden, Husguden og Gudebilledet og sluttede sig til Krigsfolkene.
21 Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
Derpå vendte de om og drog bort, idet de stillede Kvinderne og Børnene, Kvæget og Trosset forrest i Toget.
22 Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
Da de var kommet et Stykke fra Mikas Hus, stævnedes Mændene i de Huse, der lå ved Mikas Hus, sammen, og de indhentede Daniterne.
23 Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
Da de råbte efter Daniterne, vendte disse sig om og sagde til Mika: "Hvad er der i Vejen, siden du har kaldt Folk til Hjælp?"
24 Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
Han svarede: "I har taget min Gud, som jeg havde lavet mig, tillige med Præsten og er rejst eders Vej! Hvad har jeg nu tilbage? Hvor kan I spørge mig, hvad der er i Vejen?"
25 Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
Men Daniterne svarede ham: "Lad os ikke høre et Ord mere fra dig, ellers kunde det hænde, at nogle Mænd, som er bitre i Hu, faldt over eder, og at du satte både dit eget og dine Husfolks Liv på Spil!"
26 Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
Dermed drog Daniterne deres Vej, og da Mika så, at de var ham for stærke, vendte han om og begav sig tilbage til sit Hus.
27 Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
De tog så Guden, som Mika havde lavet, tillige med hans Præst og drog mod Lajisj, mod et Folk, der levede sorgløst og trygt, huggede dem ned med Sværdet og stak Ild på Byen,
28 Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
uden at nogen kunde komme den til Hjælp, thi den lå langt fra Zidon, og de havde intet med Aramæerne at gøre. Den ligger i Bet Rehobs Dal. Så byggede de Byen op igen og bosatte sig der;
29 Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
og de gav den Navnet Dan efter deres Stamfader Dan, Israels Søn; men før var Byens Navn Lajisj.
30 Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
Derpå stillede Daniterne Gudebilledet op hos sig; og Jonatan, en Søn af Moses's Søn Gersom, og hans Efterkommere var Præster for Daniternes Stamme, indtil Landets Indbyggere førtes i Landflygtighed.
31 Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.
Og det Gudebillede, Mika havde lavet sig, stillede de op hos sig, og det stod der, al den Tid Guds Hus var i Silo.

< Oweruza 18 >