< Oweruza 18 >
1 Masiku amenewo munalibe mfumu mu Israeli. Ndipo anthu a fuko la Dani amafunafuna malo okhalamo ngati cholowa chawo, chifukwa kufikira nthawi imeneyo anali asanalandire cholowa chawo pakati pa mafuko a Israeli.
V těch dnech nebylo krále v Izraeli, a toho času pokolení Dan hledalo sobě dědičného místa k bydlení, nebo se mu ještě nebylo dostalo dílu u prostřed synů Izraelských až do dne toho.
2 Choncho fuko la Dani linatumiza kuchokera ku mabanja awo onse anthu olimba mtima asanu. Anthuwa anachokera ku Zora ndi ku Esitaoli ndipo anatumidwa kukazonda ndi kuliyendera dzikolo. Anthu amenewa ankayimira fuko lonse la Dani. Anthuwa anawawuza kuti, “Pitani mukazonde dzikolo.” Anthuwa anafika ku dziko la mapiri la Efereimu ndi kupita ku nyumba ya Mika komwe anakagona.
Tedy poslali synové Dan z čeledi své pět mužů z končin svých, mužů silných z Zaraha a Estaol, aby spatřili zemi a pilně prohlédli ji, a řekli jim: Jděte, shlédněte zemi. Kteřížto když přišli na horu Efraim až do domu Míchova, přenocovali tam.
3 Ali ku nyumba ya Mika anazindikira mawu a mnyamata, Mlevi uja. Choncho anapita kwa iye namufunsa kuti, “Unabwera ndi ndani kuno? Nanga ukuchita chiyani ku malo ano? Komanso nʼchifukwa chiyani uli kuno?”
Když pak byli blízko domu Míchova, poznali hlas toho mládence Levíty, a uchýlivše se tam, řekli jemu: Kdo tě sem přivedl? Co ty zde děláš? A co ty zde máš?
4 Iye anawawuza zimene Mika anamuchitira ndipo anati, “Iye anandilemba ntchito ndipo ndine wansembe wake.”
Odpověděl jim: Toto mi a toto učinil Mícha, a ze mzdy najal mne, abych byl jeho knězem.
5 Kenaka iwo anati kwa iye, “Chonde tifunsire kwa Mulungu kuti tidziwe ngati ulendo wathuwu tiyende bwino.”
I řekli jemu: Poraď se, prosíme, s Bohem, abychom věděli, zdaří-li se nám cesta naše, kterouž jdeme.
6 Wansembeyo anawayankha kuti, “Pitani mu mtendere, Yehova ali ndi inu pa ulendo wanuwu.”
Odpověděl jim kněz: Jděte v pokoji, Hospodinť spravuje cestu vaši, po níž jdete.
7 Choncho anthu asanuwo ananyamuka ndipo anafika ku Laisi, kumene anaona kuti anthu ankakhala mwabata monga anthu a ku Sidoni. Anali anthu opanda chowavuta ndiponso aphee. Tsono popeza mʼdziko mwawo analibe chosowa, iwo anali a chuma. Anaonanso kuti anthuwo ankakhala kutali ndi Sidoni ndipo analibe ubale ndi wina aliyense.
Tedy odešlo pět mužů těch, a přišli do Lais, a viděli lid, kterýž tam byl, bezpečně bydlící, vedlé obyčeje Sidonských v zahálce a bezpečnosti, a že nebylo, co by je kormoutiti mělo v té zemi, ani kdo by dědičně ujíti chtěl království. K tomu i od Sidonských vzdáleni byli, aniž spříznění jaké s kým měli.
8 Ozonda dziko aja atabwerera kwa abale awo ku Zora ndi Esitaoli, abale awowo anawafunsa kuti, “Mwaonako zotani?”
Když se pak navrátili k bratřím svým do Zaraha a Estaol, řekli jim bratří jejich: Což vy?
9 “Tiyeni tikamenyane nawo nkhondo popeza taliona dziko lawolo kuti ndi lachonde kwambiri. Kodi simuchitapo kanthu? Musachite mphwayi kupita mʼdzikomo ndi kukalilanda.
I odpověděli: Vstaňte a táhněme na ně, nebo shlédli jsme tu zemi, a aj, velmi dobrá jest; a vy mlčíte? Nelenujtež se táhnouti, a vjíti k opanování té země.
10 Mukalowa, mukapeza anthu amene ali osatekeseka ndi dziko lalikulu. Yehova wakupatsani dziko limeneli. Malowo ngosasowa kanthu kalikonse kopezeka pa dziko lapansi.”
(Když přijdete, vejdete k lidu bezpečnému, a do země prostranné; ) nebo dal ji Bůh v ruku vaši, místo, v němž není žádného nedostatku jakýchkoli věcí, kteréž na zemi býti mohou.
11 Kenaka anthu 600 a fuko la Dani ananyamuka ku Zora ndi Esitaoli atanyamula zida za nkhondo.
Tedy vyšlo z čeledi Dan odtud, totiž z Zaraha a Estaol, šest set mužů oděných v odění válečné.
12 Tsono anakamanga msasa ku Kiriati-Yearimu mʼdziko la Yuda. Malowa ali kumadzulo kwa Kiriati-Yearimu. Ichi ndi chifukwa chake malowo akutchedwa Mahane Dani mpaka lero.
A vytáhše, položili se u Kariatjeharim Judova; pročež nazvali to místo Mahane Dan až do dnešního dne, a jest za Kariatjeharim.
13 Kuchokera kumeneko anapita ku dziko lamapiri la Efereimu ndipo anafika ku nyumba ya Mika.
A odtud táhnouce na horu Efraim, přišli až k domu Míchovu.
14 Anthu asanu amene anakazonda dziko la Laisi anati kwa abale awo, “Kodi mukudziwa kuti imodzi mwa nyumba izi muli efodi, mafano a mʼnyumba otchedwa terafimu, fano losema ndiponso fano lokuta ndi siliva? Ndiye mudziwe chochita.”
I mluvilo těch pět mužů, kteříž chodili k shlédnutí země Lais, a řekli bratřím svým: Víte-liž, že v domích těchto jest efod a terafim, a rytina a slitina? Protož nyní vězte, co máte činiti.
15 Choncho anthuwa anapatuka napita ku nyumba ya Mika kumene mnyamata, Mlevi uja ankakhala ndipo anamufunsa za mmene zinthu zilili.
A uchýlivše se tam, vešli do domu mládence Levíty v domě Míchově, a pozdravili ho pokojně.
16 Nthawi imeneyi nʼkuti anthu 600 a fuko la Dani aja atayima pa chipata atanyamula zida za nkhondo.
Ale šest set mužů oděných v zbroj svou válečnou, kteříž byli z pokolení Dan, stáli přede dveřmi.
17 Anthu asanu amene anakazonda dziko aja analowa ndi kukatenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba lotchedwa terafimu, ndi fano lokutidwa ndi siliva. Nthawiyi nʼkuti wansembe uja ndi anthu 600 okhala ndi zida za nkhondo aja ali chiyimire pa chipata.
A šedše pět mužů, kteříž chodili k shlédnutí země, vešli tam a vzali rytinu a efod a terafim a slitinu; kněz pak stál u vrat brány s šesti sty muži oděnými v zbroji.
18 Anthuwo atalowa mʼnyumba ya Mika ndi kutenga fano losema, efodi, fano la mʼnyumba, ndi fano lokutidwa ndi siliva, wansembeyo anawafunsa kuti, “Kodi mukuchita chiyani?”
A ti, kteříž vešli do domu Míchova, vzali rytinu, efod a terafim, a slitinu. I řekl jim kněz: Což to děláte?
19 Iwo anamuyankha kuti, “Khala chete usayankhule. Tsagana nafe ndipo udzakhala mlangizi wathu ndi wansembe wathu. Kodi si kwabwino kwa iwe kukhala wansembe wa fuko lonse la Israeli mʼmalo mokhala wansembe wa munthu mmodzi yekha?”
Kteříž odpověděli: Mlč, vlož ruku svou na ústa svá a poď s námi, a budeš nám za otce a za kněze. Což jest lépe tobě, knězem-li býti v domě jednoho člověka, či býti knězem pokolení a čeledi v Izraeli?
20 Wansembeyo anakondwera ndipo anatenga efodi, fano la mʼnyumba ndi fano losema natsagana nawo.
I zradovalo se srdce kněze, a vzav efod a terafim a rytinu, šel u prostřed lidu toho.
21 Choncho iwo anatembenuka nachoka, atatsogoza ana, zoweta ndi katundu wawo yense.
A obrátivše se odešli, a pustili napřed děti a dobytek, a což měli dražšího.
22 Atayenda mtunda pangʼono kuchokera pa nyumba ya Mika, anthu amene amakhala pafupi ndi nyumba ya Mika anasonkhana kulondola a fuko la Dani aja, ndipo anawapeza.
Když pak opodál byli od domu Míchova, tedy muži, kteříž bydlili v domích blízkých domu Míchova, shromáždili se a honili syny Dan.
23 Atawafuwulira, a fuko la Dani aja anachewuka ndipo anafunsa Mika kuti, “Chavuta nʼchiyani kuti usonkhanitse anthu chotere?”
I volali za syny Dan. Kteříž ohlédše se, řekli Míchovi: Cožtě, že jsi jich tolik shromáždil?
24 Iye anayankha kuti, “Inu mwanditengera milungu imene ndinapanga pamodzi ndi wansembe nʼkumapita. Tsono ine ndatsala ndi chiyani? Ndiye inu mungafunse kuti chavuta nʼchiyani?”
Odpověděl: Bohy mé, kteréž jsem udělal, vzali jste, i kněze, a odcházíte. Což pak již budu míti? A ještě se ptáte: Coť jest?
25 Anthu a fuko la Dani aja anayankha kuti, “Usayankhuleponso kanthu chifukwa anthu awa angapse mtima nakumenya ndipo iwe ndi banja lako lonse nʼkutayapo miyoyo yanu.”
Jemuž odpověděli synové Dan: Hlediž, ať více neslyšíme hlasu tvého za sebou, sic jináč oboří se na vás muži hněviví, a ztratíš duši svou i duše domu svého.
26 Choncho anthu a fuko la Dani anapitiriza ulendo wawo. Mika ataona kuti anthuwo anali amphamvu kuposa iye, anangotembenuka kubwerera kwawo.
I brali se muži Dan cestou svou. A vida Mícha, že by silnější byli nežli on, obrátiv se, šel do domu svého.
27 Anthu a fuko la Dani aja anatenga zinthu zimene Mika anapanga pamodzi ndi wansembe uja. Iwo anakafika ku Laisi kwa anthu a phee, osatekeseka aja ndipo anawathira nkhondo, nawapha ndi kutentha mzindawo ndi moto.
Oni pak vzavše, což byl udělal Mícha, i kněze, kteréhož měl, přitáhli do Lais k lidu zahálivému a bezpečnému; i pobili je ostrostí meče, a město vypálili ohněm.
28 Panalibe wowapulumutsa chifukwa anali kutali ndi Sidoni ndiponso sanali pa ubale ndi wina aliyense. Mzindawo unali mʼchigwa cha Beti-Rehobu. Anthu a fuko la Adaniwo anawumanganso mzindawo ndi kumakhalamo.
A nebylo žádného, kdo by jim spomohl; nebo daleko byl Sidon, aniž měli spříznění s kterými lidmi. Město pak bylo v údolí, kteréž jest v Betrohob. A vystavěvše zase město, bydlili v něm.
29 Iwo anawutcha mzindawo Dani, kutengera dzina la kholo lawo Dani, amene anali mwana wa Israeli, ngakhale kuti mzindawo poyamba unali Laisi.
A nazvali jméno města toho Dan, od jména otce svého, kterýž narozen byl Izraelovi, ješto prvé jméno města toho bylo Lais.
30 Anthu a fuko la Dani anayimiritsa fano losema lija. Yonatani mwana wa Geresomu, mwana wa Mose pamodzi ndi ana ake onse anakhala ansembe a fuko la Dani mpaka pa tsiku la ukapolo wa dzikolo.
Postavili pak sobě synové Dan tu rytinu, a Jonatan syn Gersonův, syna Mojžíšova, on i synové jeho byli kněžími v pokolení Dan, až do dne zajetí obyvatelů země.
31 Choncho anthu a fuko la Dani ankapembedza fano limene Mika anapanga nthawi yonse pamene nyumba ya Mulungu inali ku Silo.
Vystavili tedy sobě tu rytinu, kterouž udělal Mícha, a byla tam po všecky dny, v nichž dům Boží byl v Sílo.