< Oweruza 16 >

1 Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
Och Simson gick till Gasa, och fick der se ena sköko, och lade sig när henne.
2 Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
Då vardt sagdt de Gasiter: Simson är kommen härin; och de omhvärfde honom, och läto taga vara på honom i stadsportenom i hela nattene; och voro stilla i hela nattene, och sade: I morgon, då ljust varder, vilje vi slå honom ihjäl.
3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
Men Simson låg intill midnatt. Då stod han upp om midnatt, och fattade båda dörrarna i stadsporten med båda dörrträn, och skottbommen, och lade dem på sina axlar, och bar dem upp på bergshöjdena för Hebron.
4 Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
Derefter fick han kärlek till ena qvinno vid den bäcken Sorek, hvilken het Delila.
5 Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
Upp till henne kommo de Philisteers Förstar, och sade till henne: Tala så vid honom, att du kan få se, hvarutinnan han sådana stor kraft hafver, och hvarmed vi kunne varda honom öfverhändige, så att vi finge bindan och tvingan; så vilje vi gifva dig hvar våra tusende och hundrade silfpenningar.
6 Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
Och Delila sade till Simson: Käre, säg mig, hvaruti står din stora starkhet; och hvarmed man kunde binda dig, och tvinga dig?
7 Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
Simson sade till henne: Om man bunde mig med sju ny tåg, som ännu intet förtorkad voro, så vorde jag svag, och såsom en annor menniska.
8 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
Då förde de Philisteers Förstar upp till henne sju ny tåg, som ännu intet förtorkad voro, och hon band honom dermed.
9 Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
Och de hade håll på honom när henne i kammaren; och hon sade till honom: De Philisteer öfver dig, Simson! Och han slet sönder tågen, såsom ett vridet snöre söndergår, när det af eld förbrändt är; och vardt icke kunnigt, hvarutinnan hans starkhet var.
10 Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
Då sade Delila till Simson: Si, du hafver gäckat mig, och ljugit för mig; säg mig dock nu, hvarmed man dig binda kan?
11 Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
Han svarade: Om jag vorde bunden med ny tåg, der ännu intet arbete med gjordt är, så vorde jag svag, och såsom en annor menniska.
12 Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
Så tog Delila ny tåg, och band honom dermed, och sade: De Philisteer öfver dig, Simson! Och de hade håll på honom i kammaren; och han slet sönder dem utaf sina armar, såsom ett snöre.
13 Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
Delila sade till honom: Du hafver ännu gäckat mig, och ljugit för mig. Käre, säg mig dock, hvarmed man kan dig binda? Han svarade henne: Om du flätade sju lockar af mitt hufvud uti ett fläteband.
14 Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
Och hon fäste dem in med en nagla, och sade till honom: De Philisteer öfver dig, Simson! Och han vaknade upp af sinom sömn, och drog de flätade lockar med nagla och fläteband ut.
15 Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
Då sade hon till honom: Huru kan du säga, att du hafver mig kär, efter ditt hjerta är dock icke när mig? I tre gånger hafver du gäckat mig, och icke sagt mig, hvarutinnan din stora starkhet är.
16 Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
Och som hon alla dagar låg honom uppå med sådana ordom, och lät honom ingen ro få, vardt hans själ uppgifven allt intill döden.
17 Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
Och sade henne allt sitt hjerta, och sade till henne: På mitt hufvud hafver aldrig någon rakoknif kommit, ty jag är en Guds Nazir af moderlifvet; om man rakar håret af mig, så går min starkhet ifrå mig, så att jag varder svag, lika som andra menniskor.
18 Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
Då nu Delila såg, att han hade uppenbarat henne allt sitt hjerta, sände hon bort, och lät kalla de Philisteers Förstar, och sade: Kommer än en gång hitupp; ty han hafver uppenbarat mig allt sitt hjerta. Då kommo de Philisteers Förstar upp till henne, och hade penningarna med sig i sine hand.
19 Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
Och hon lät honom sofva på sitt knä, och kallade en, som rakade honom bort de sju lockar af hans hufvud; och hon begynte till att tvinga honom, och hans magt var gången ifrå honom.
20 Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
Och hon sade till honom: De Philisteer öfver dig, Simson! Som han nu vaknade af sinom sömn, tänkte han: Jag vill gå ut, såsom jag i flera resor gjort hafver, jag vill slita mig lös; och visste icke, att Herren var viken ifrå honom.
21 Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
Men de Philisteer grepo honom, och stungo honom ögonen ut, och förde honom neder till Gasa, och bundo honom med två kopparfjettrar; och han måste mala i fängelset.
22 Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
Och hans hufvudhår begynte åter växa, der han rakad var.
23 Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
Då församlade sig de Philisteers Förstar, till att göra sinom gud Dagon ett stort offer, och göra sig glada, och sade: Vår gud hafver gifvit oss vår fienda Simson i våra händer.
24 Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
Sammalunda när folket såg honom, prisade de deras gud: ty de sade: Vår gud hafver gifvit vår fienda i våra händer, den vårt land förderfvade, och slog många af oss ihjäl.
25 Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
Då nu deras hjerta väl gladt var, sade de: Låt hemta Simson, att han må spela för oss. Så hemtade de Simson utu fängelset, och han spelade för dem, och de ställde honom emellan två pelare.
26 Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
Men Simson sade till drängen, som ledde honom vid handena: Låt mig taga på pelarena, på hvilka huset hänger, att jag må stödja mig derintill.
27 Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
Och huset var fullt med män och qvinnor; och de Philisteers Förstar voro der ock alle, och på taket vid tretusend män och qvinnor, de som sågo till huru Simson spelade.
28 Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
Men Simson åkallade Herran, och sade: Herre, Herre, tänk uppå mig, och styrk mig, Gud! i denna gången, att jag för båda min ögon må ena reso hämnas på de Philisteer.
29 Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
Och han fattade de två medelpelare, på hvilka huset hängde, och stödde sig på dem, och tog den ena i den högra, och den andra i den venstra handena;
30 ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
Och sade: Min själ dö med de Philisteer! och han böjde dem krafteliga. Så föll huset uppå Förstarna, och uppå allt folket, som derinne var, så att de döde, som han drap i sin död, voro flere, än de som han drap medan han lefde.
31 Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.
Då kommo hans bröder ditneder, och hela hans faders hus, och togo honom upp, och båro honom upp, och begrofvo honom i hans faders Manoahs graf, emellan Zorga och Esthaol. Men han dömde Israel i tjugu år.

< Oweruza 16 >