< Oweruza 16 >

1 Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
Самсон а плекат ла Газа; аколо а вэзут о курвэ ши а интрат ла еа.
2 Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
С-а спус оаменилор дин Газа: „Самсон а венит аич.” Ши л-ау ынконжурат ши ау пындит тоатэ ноаптя ла поарта четэций. Ау стат лиништиць тоатэ ноаптя ши ау зис: „Кынд се ва лумина де зиуэ, ыл вом оморы.”
3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
Самсон а рэмас кулкат пынэ ла мезул нопций. Пе ла мезул нопций, с-а скулат ши а апукат порциле четэций ку амындой стылпий, ле-а скос ымпреунэ ку зэворул, ле-а пус пе умерь ши ле-а дус пе вырфул мунтелуй дин фаца Хебронулуй.
4 Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
Дупэ ачея, а юбит пе о фемее ын валя Сорек. Еа се нумя Далила.
5 Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
Домниторий филистенилор с-ау суит ла еа ши й-ау зис: „Ындуплекэ-л ши афлэ де унде-й вине путеря луй чя маре ши кум ам путя сэ-л бируим, ка сэ-л легэм ши сэ-л слэбим, ши-ць вом да фиекаре кыте о мие о сутэ де сикли де арӂинт.”
6 Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
Далила а зис луй Самсон: „Спуне-мь, те рог, де унде-ць вине путеря та чя маре ши ку че ар требуи сэ фий легат ка сэ фий бируит.”
7 Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
Самсон й-а зис: „Дакэ аш фи легат ку шапте фуний ной, каре сэ ну фие ускате ынкэ, аш слэби ши аш фи ка орьче алт ом.”
8 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
Домниторий филистенилор ау адус Далилей шапте фуний ной, неускате ынкэ. Ши еа л-а легат ку фунииле ачестя.
9 Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
Яр ниште оамень стэтяу ла пындэ ла еа, ынтр-о одае. Еа й-а зис: „Филистений сунт асупра та, Самсон!” Ши ел а рупт фунииле кум се рупе о ацэ де кылць кынд се атинӂе де фок. Ши, астфел, н-ау штиут де унде-й веня путеря.
10 Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
Далила а зис луй Самсон: „Везь, ць-ай бэтут жок де мине, мь-ай спус минчунь. Акум, те рог, аратэ-мь ку че требуе сэ фий легат.”
11 Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
Ел й-а зис: „Дакэ аш фи легат ку фуний ной, каре сэ ну фи фост ынтребуинцате ничодатэ, аш слэби ши аш фи ка орьче алт ом.”
12 Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
Далила а луат ниште фуний ной ши л-а легат ку еле. Апой й-а зис: „Филистений сунт асупра та, Самсон!” Яр ниште оамень стэтяу ла пындэ ынтр-о одае. Ши ел а рупт фунииле де ла браце ка пе о ацэ.
13 Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
Далила а зис луй Самсон: „Пынэ акум ць-ай бэтут жок де мине ши мь-ай спус минчунь. Спуне-мь ку че требуе сэ фий легат.” Ел й-а зис: „Н-ай декыт сэ ымплетешть челе шапте шувице де пэр дин капул меу ын урзяла цесэтурий.”
14 Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
Ши еа ле-а пиронит ку ун куй де лемн ын пэмынт. Апой й-а зис: „Филистений сунт асупра та, Самсон!” Ши ел с-а трезит дин сомн ши а смулс куюл де лемн дин пэмынт ку урзялэ ку тот.
15 Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
Еа й-а зис: „Кум поць спуне: ‘Те юбеск!’, кынд инима та ну есте ку мине? Ятэ кэ де трей орь ць-ай бэтут жок де мине ши ну мь-ай спус де унде-ць вине путеря та чя маре.”
16 Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
Фииндкэ еа ыл некэжя ши-л кинуя ын фиекаре зи ку стэруинцеле ей, суфлетул и с-а умплут де о нелиниште де моарте,
17 Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
шь-а дескис тоатэ инима фацэ де еа ши й-а зис: „Бричул н-а трекут песте капул меу, пентру кэ сунт ынкинат Домнулуй дин пынтечеле майчий меле. Дакэ аш фи рас, путеря м-ар пэрэси, аш слэби ши аш фи ка орьче алт ом.”
18 Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
Далила, вэзынд кэ ышь дескисесе тоатэ инима фацэ де еа, а тримис сэ кеме пе домниторий филистенилор ши а пус сэ ле спунэ: „Суици-вэ де дата ачаста, кэч мь-а дескис тоатэ инима луй.” Ши домниторий филистенилор с-ау суит ла еа ши ау адус арӂинтул ын мынь.
19 Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
Еа л-а адормит пе ӂенункий ей. Ши, кемынд ун ом, а рас челе шапте шувице де пе капул луй Самсон ши а ынчепут астфел сэ-л слэбяскэ. Ел шь-а пердут путеря.
20 Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
Атунч, еа а зис: „Филистений сунт асупра та, Самсон!” Ши ел с-а трезит дин сомн ши а зис: „Вой фаче ка ши май ынаинте ши мэ вой скутура.” Ну штия кэ Домнул Се депэртасе де ел.
21 Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
Филистений л-ау апукат ши й-ау скос окий; л-ау коборыт ла Газа ши л-ау легат ку ниште ланцурь де арамэ. Ел ынвыртя ла рышницэ ын темницэ.
22 Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
Дар пэрул капулуй луй а ынчепут ярэшь сэ кряскэ дупэ че фусесе рас.
23 Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
Ши домниторий филистенилор с-ау стрынс ка сэ адукэ о маре жертфэ думнезеулуй лор Дагон ши ка сэ се веселяскэ. Ей зичяу: „Думнезеул ностру а дат ын мыниле ноастре пе Самсон, врэжмашул ностру.”
24 Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
Ши, кынд л-а вэзут попорул, ау лэудат пе думнезеул лор, зикынд: „Думнезеул ностру а дат ын мыниле ноастре пе врэжмашул ностру, пе ачела каре не пустия цара ши не ынмулця морций.”
25 Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
Ын букурия инимий лор, ау зис: „Кемаць пе Самсон, ка сэ не десфэтезе!” Ау скос пе Самсон дин темницэ ши ел а жукат ынаинтя лор. Л-ау ашезат ынтре стылпь.
26 Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
Ши Самсон а зис тынэрулуй каре-л циня де мынэ: „Ласэ-мэ ка сэ мэ пот атинӂе де стылпий пе каре се ряземэ каса ши сэ мэ рязем де ей.”
27 Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
Каса ера плинэ де бэрбаць ши де фемей; тоць домниторий филистенилор ерау аколо ши пе акопериш ерау апроапе трей мий де иншь, бэрбаць ши фемей, каре привяу ла Самсон кум жука.
28 Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
Атунч Самсон а стригат кэтре Домнул ши а зис: „Доамне Думнезеуле, аду-Ць аминте де мине, Те рог; Думнезеуле, дэ-мь путере нумай де дата ачаста ши, ку о сингурэ ловитурэ, сэ мэ рэзбун пе филистень пентру чей дой окь ай мей!”
29 Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
Ши Самсон а ымбрэцишат амындой стылпий де ла мижлок пе каре се сприжиня каса ши с-а реземат де ей; унул ера ла дряпта луй ши алтул, ла стынга.
30 ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
Самсон а зис: „Сэ мор ымпреунэ ку филистений!” С-а плекат ку тоатэ путеря, ши каса а кэзут песте домниторь ши песте тот попорул каре ера аколо. Чей пе каре й-а прэпэдит ла моартя луй ау фост май мулць декыт чей пе каре-й оморысе ын тимпул веций.
31 Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.
Фраций луй ши тоатэ каса татэлуй сэу с-ау коборыт ши л-ау луат. Кынд с-ау суит ынапой, л-ау ынгропат ынтре Цорея ши Ештаол, ын мормынтул татэлуй сэу Маноах. Ел фусесе жудекэтор ын Исраел доуэзечь де ань.

< Oweruza 16 >