< Oweruza 16 >

1 Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
Sansão foi para Gaza, e viu lá uma prostituta, e foi até ela.
2 Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
Foi dito aos gazitas: “Sansão está aqui!”. Eles o cercaram e o esperaram a noite toda no portão da cidade, e ficaram quietos a noite toda, dizendo: “Espere até a luz da manhã; então o mataremos”.
3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
Sansão deitou-se até a meia-noite, depois levantou-se à meia-noite e pegou as portas do portão da cidade, com os dois postes, e os arrancou, bar e tudo, e os colocou sobre seus ombros e os carregou até o topo da montanha que está antes de Hebron.
4 Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
Aconteceu depois que ele amava uma mulher no vale de Sorek, cujo nome era Delilah.
5 Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
Os senhores dos filisteus se aproximaram dela e lhe disseram: “Atice-o e veja em que consiste sua grande força, e por que meios podemos prevalecer contra ele, a fim de amarrá-lo para afligi-lo; e cada um de nós lhe dará onzecentas moedas de prata”.
6 Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
Delilah disse a Samson: “Por favor, diga-me onde está sua grande força e o que você pode estar destinado a lhe afligir”.
7 Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
Sansão disse a ela: “Se eles me amarrarem com sete cordas verdes que nunca foram secas, então eu ficarei fraco e serei como outro homem”.
8 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
Então os senhores dos filisteus trouxeram-lhe sete cordas verdes que não tinham sido secas, e ela o amarrou com elas.
9 Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
Now ela teve uma emboscada esperando na sala interna. Ela disse a ele: “Os filisteus estão em cima de você, Samson”! Ele quebrou os cordões enquanto um fio de linho é quebrado quando toca o fogo. Portanto, sua força não era conhecida.
10 Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
Delilah disse a Samson: “Eis que você zombou de mim, e me disse mentiras. Agora, por favor, diga-me como você pode estar vinculado”.
11 Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
Ele lhe disse: “Se eles só me amarram com cordas novas com as quais não foi feito nenhum trabalho, então eu me tornarei fraco e serei como outro homem”.
12 Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
Então Delilah pegou novas cordas e o amarrou com elas, então disse a ele: “Os filisteus estão em você, Samson! A emboscada estava esperando na sala interna. Ele as quebrou de seus braços como um fio.
13 Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
Delilah disse a Samson: “Até agora, você tem zombado de mim e me dito mentiras. Diga-me com o que você pode estar amarrado”. Ele lhe disse: “Se você tecer as sete fechaduras da minha cabeça com o tecido no tear”.
14 Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
She prendeu-o com o alfinete, e disse-lhe: “Os filisteus estão em você, Samson! Ele acordou de seu sono, e arrancou o pino da viga e o tecido.
15 Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
Ela lhe disse: “Como você pode dizer: 'Eu te amo', quando seu coração não está comigo? Você zombou de mim estas três vezes, e não me disse onde está sua grande força”.
16 Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
Quando ela o pressionou diariamente com suas palavras e o exortou, sua alma ficou perturbada até a morte.
17 Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
Ele disse a ela todo o seu coração e lhe disse: “Nunca nenhuma lâmina de barbear veio sobre minha cabeça; pois desde o ventre de minha mãe tenho sido um nazista para Deus. Se eu for barbeado, então minha força irá de mim e ficarei fraco, e serei como qualquer outro homem”.
18 Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
Quando Delilah viu que ele tinha dito a ela todo o seu coração, ela enviou e chamou os senhores dos filisteus, dizendo: “Suba esta vez, pois ele me disse todo o seu coração”. Então os senhores dos filisteus se aproximaram dela e trouxeram o dinheiro em suas mãos.
19 Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
Ela o fez dormir de joelhos; e chamou por um homem e raspou as sete trancas de sua cabeça; e começou a afligi-lo, e sua força passou dele.
20 Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
Ela disse: “Os filisteus estão sobre você, Samson”! Ele acordou do sono e disse: “Vou sair como em outros momentos, e me sacudirei livre”. Mas ele não sabia que Yahweh havia partido dele.
21 Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
Os filisteus o seguraram e lhe arrancaram os olhos; e o levaram para Gaza e o amarraram com grilhões de bronze; e ele moeu no moinho da prisão.
22 Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
However, os cabelos de sua cabeça começaram a crescer novamente depois que ele foi barbeado.
23 Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
Os senhores dos filisteus se reuniram para oferecer um grande sacrifício a Dagon, seu deus, e para se regozijar; pois eles disseram: “Nosso deus entregou Sansão nosso inimigo em nossas mãos”.
24 Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
Quando o povo o viu, elogiaram seu deus; pois disseram: “Nosso deus entregou nosso inimigo e o destruidor de nosso país, que matou muitos de nós, em nossas mãos”.
25 Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
Quando seus corações estavam alegres, eles disseram: “Chamem por Sansão, para que ele nos entretenha”. Eles chamaram Samson para fora da prisão; e ele se apresentou diante deles. Colocaram-no entre os pilares;
26 Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
e Sansão disse ao rapaz que o segurava pela mão: “Permitam-me sentir os pilares sobre os quais repousa a casa, para que eu possa apoiar-me neles”.
27 Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
Agora a casa estava cheia de homens e mulheres; e todos os senhores dos filisteus estavam lá; e havia no telhado cerca de três mil homens e mulheres, que viram enquanto Sansão se apresentava.
28 Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
Sansão chamou a Javé, e disse: “Senhor Javé, lembra-te de mim, por favor, e fortalece-me, por favor, só desta vez, Deus, para que eu possa ser vingado imediatamente dos filisteus pelos meus dois olhos”.
29 Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
Sansão tomou posse dos dois pilares intermediários sobre os quais a casa descansava e se apoiava neles, um com sua mão direita e o outro com sua esquerda.
30 ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
Sansão disse: “Deixe-me morrer com os filisteus”! Ele se curvou com todas as forças; e a casa caiu sobre os senhores, e sobre todas as pessoas que nela estavam. Assim, os mortos que ele matou na sua morte foram mais do que aqueles que ele matou em sua vida.
31 Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.
Então seus irmãos e toda a casa de seu pai desceram e o levaram, e o criaram e o enterraram entre Zorah e Eshtaol no local de sepultamento de Manoah, seu pai. Ele julgou Israel vinte anos.

< Oweruza 16 >