< Oweruza 16 >
1 Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
I HO aku la o Samesona i Gaza, a ike iho la ilaila i kekahi wahine hookamakama, a komo aku la io na la.
2 Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
Haiia'ku la i ko Gaza, Ua hiki mai nei o Samesona. Hoopuni iho la lakou ia wahi, a hoohalua ia ia, ia po a ao, ma ka puka o ke kulanakauhale, a moe malie no ia po a pau, i iho la, A kakahiaka, i ke ao ana ae, make no oia ia kakou.
3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
Moe iho la o Samesona, a iwaena konu o ka po; alaila, ala mai la ia iwaena konu o ka po, a lawe iho la i na pani o ke kulanakauhale, a me na lapauwila elua, unuhi ae la ia laua me ka hoaka o ka puka, kau iho la maluna o kona mau poohiwi, a lawe aku la iluna pono o kahi puu, ma ke alo o Heberona.
4 Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
A mahope iho, aloha ae la ia i kekahi wahine ma ke kahawai o Soreka, o Delila kona inoa.
5 Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
Pii ae la na'lii o Pilisetia io na la, i ae la ia ia, E hoowalewale oe ia ia, a e nana hoi i kahi o kona ikaika nui, a me ka mea e lanakila'i makou maluna ona, i nakinaki makou ia ia, a pilikia ia; alaila, e uku aku makou ia oe, i hookahi tausani apana kala, a me ka haneri keu.
6 Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
I aku la o Delila ia Samesona, Ke nonoi aku nei au ia oe, e hai mai oe ia'u i kou mea e ikaika nui ai, a me ka mea e paa ai oe, i pilikia ai oe.
7 Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
I mai la o Samesona ia ia, Ina nakinaki mai lakou ia'u i na kaula maka ehiku, i hoomaloo ole ia, alaila, e nawaliwali au, a like auanei me kekahi kanaka.
8 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
Alaila, lawe mai na'lii o ko Pilisetia ia ia i ehiku kaula maka, i hoomaloo ole ia, a me ia no ia i nakinaki ai ia ia.
9 Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
E moe malu ana no na kanaka maloko o ia keena me ia. I mai la kela, Maluna on auanei ko Pilisetia, e Samesona. Moku ae la ia ia na kaula, e like me ka moku ana o ke kaula oka, i kona wa e honi ai i ke ahi, aole hoi i loaa kahi o kona ikaika.
10 Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
I mai la o Delila ia Samesona, Aia hoi, ua hoowahawaha mai oe ia'u, a ua hoopunipuni mai ia'u. Nolaila, ke nonoi aku nei au ia oe, e hai mai oe ia'u i kou mea e paa ai.
11 Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
I aku la keia ia ia, Ina nakinaki paa loa mai lakou ia'u i na kaula hou, aole i hoohanaia, alaila e nawaliwali au, a e like auanei me kekahi kanaka.
12 Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
Kii ae la o Delila i na kaula hou, a nakinaki iho la ia ia me ia, i ae la, Maluna ou auanei o ko Pilisetia, e Samesona. E moe malu ana no na kanaka maloko o ia keena. Moku ae la ia ia na kaula, mai kona lima aku, me he lopi la.
13 Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
I mai o Delila ia Samesona, Ua hoowahawaha mai oe ia'u, a hiki mai i keia manawa, a ua hoopunipuni ia'u. E hai mai oe ia'u i kou mea e paa ai. I aku la keia ia ia, Ina e ulana pu oe i na will ehiku o ko'u poo, me ka lole.
14 Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
Alaila, makia iho la ia i ke kui, i ae la, Maluna ou auanei ko Pilisetia, e Samesona. Ala ae la ia mai kona hiamoe ana, a hele aku la me ke kui o ka mea nana i ulana, a me ka lole pu.
15 Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
I mai la oia ia ia, Pehea la oe e olelo ai, Ua aloha au ia oe? Aole hoi kou naau me au. Ekolu ou hoowahawaha ana mai ia'u, aole hoi i hai mai ia'u i kahi o kou ikaika nui.
16 Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
I kona koi ana ia ia i na la a pau, i kana olelo ana, a hookaumaha loa ia ia, a pilikia kona manao, aneane make;
17 Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
Alaila, hai aku la oia ia ia i kona naau a pau, i aku la ia ia, Aole i kau mai ka pahikahi maluna o ko'u poo; no ka mea, ua laa au i ke Akua, mai ka opu mai o ko'u makuwahine. Ina e kahiia au, alaila, lilo aku hoi ko'u ikaika mai o'u aku nei, a nawaliwali auanei au e like me kekahi kanaka.
18 Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
A ike iho la o Delila, ua hai mai kela ia ia i kona naau a pau, alaila kii aku la ia, a hoakoakoa mai la i na'lii o ko Pilisetia, i ae la, E pii hou mai oukou, no ka mea, ua hai mai oia ia'u i kona naau a pau. Alaila, pii ae la na'lii o ko Pilisetia io na la, a lawe ae la i ke kala, ma ko lakou lima.
19 Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
Hoomoe iho la oia ia ia ma kona uha; a hea aku la i ke kanaka a haawi ia ia e kahi i na wili ehiku o kona poo a hemo; a hoomaka ia i ka hoopilikia ana ia ia, a lilo aku la kona ikaika, mai ona aku la.
20 Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
I mai la ia, Maluna ou auanei ko Pilisetia, e Samesona. Ala ae la ia, mai kona hiamoe ana, i mai la, E hele au iwaho e like me na wa mamua, e hooluliluli. Aole ia i ike, ua haalele o Iehova ia ia.
21 Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
Hoopaa iho la ko Pilisetia ia ia, poalo aku la i kona mau maka, a lawe ae la ia ia i Gaza, a hoopaa iho la ia ia i na kupee keleawe; a wili ae la ia iloko o ka halepaahao.
22 Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
Hoomaka iho la ka lauoho o kona poo i ka ulu hou, e like me ia i ka wa i kahiia'i.
23 Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
Alaila hoakoakoa mai la na'lii o ko Pilisetia e kaumaha aku i mohai nui no Dagona, ko lakou akua, a e olioli; no ka mea, olelo mai la lakou, Ua haawi mai ko kakou akua ia Samesona o ko kakou enemi, iloko o ko kakou lima.
24 Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
A ike aku la na kanaka ia ia, hoomana aku la lakou i ko lakou akua; no ka mea, olelo mai la lakou, Ua haawi mai ko kakou akua iloko o ko kakou lima, i ko kakou enemi, i ka mea i anai ai i ko kakou aina, a luku nui mai ia kakou.
25 Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
A i ka wa lealea ai ko lakou naau, i ae la lakou, E kii aku ia Samesona, i hula mai ia no kakou. Kii aku la lakou ia Samesona ma ka halepaahao, a hula mai la ia imua o lakou. A hooku iho la lakou ia ia iwaena o na kia.
26 Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
I ae la o Samesona i ke keiki e paa ana i kona lima, E hoomaha mai oe ia'u i hana aku au i na kia e paa ai ka hale, i hilinai hoi au ma ia mau mea.
27 Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
Ua piha ka hale i na kanaka, a me na wahine. Malaila no na'lii a pau o ko Pilisetia. Ekolu tausani kanaka a me na wahine maluna o ka hale i nana mai i ko Samesona hula ana.
28 Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
Hea aku la o Samesona ia Iehova, i aku la, E ka Haku, e Iehova e, e hoomanao mai oe ia'u; ke nonoi aku nei au ia oe, e hooikaika mai oe ia'u, e ke Akua e, i keia manawa hookahi no, i uku koke ia mai au e ko Pilisetia, no ko'u mau maka elua.
29 Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
Lalau iho la o Samesona ma na kia waenakonu elua, a oia hoi na mea e paa ai ka hale. Hilinai iho la oia ma ia mau mea, o ka lima akau ma kekahi, a o ka lima hema ma kekahi.
30 ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
I iho la o Samesona, E make pu au me ko Pilisetia. Kulou iho la me ka ikaika nui, a hina iho la ka hale maluna o na'lii, a maluna o na kanaka a pau maloko. Ua nui ka poe make, ana i luku ai i kona make ana, he hapa ka poe ana i luku ai i kona wa i ola'i.
31 Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.
Iho aku la kona poe hoahanau, a me ko ka hale o kona makuakane, lalau iho la ia ia, a lawe ae la, a kanu iho la mawaena o Zora, a me Esetaola, ma ka ilina o Manoa, o kona makuakane. He iwakalua makahiki ana i hooponopono ai i ka Iseraela.