< Oweruza 16 >

1 Tsiku lina Samsoni anapita ku Gaza. Kumeneko anaonako mkazi wachiwerewere, ndipo analowa mu nyumba yake.
Also Sampson yede in to Gazam, and he siy there a womman hoore, and he entride to hir.
2 Anthu a ku Gaza anawuzidwa kuti, “Samsoni ali kuno!” Choncho anthuwo anazungulira malowo, kumubisalira usiku wonse ku chipata cha mzindawo. Iwo anakhala chete usiku wonse namanena kuti, “Tidzamupha mmamawa.”
And whanne Filisteis hadden seyn this, and it was pupplischid at hem, that Sampson entride in to the citee, thei cumpassiden hym, whanne keperis weren set in the yate of the citee; and thei abididen there al nyyt `with silence, that in the morewtid thei schulen kille Sampson goynge out.
3 Koma Samsoni anangogonako mpaka pakati pa usiku. Kenaka pakati pa usiku anadzuka nagwira zitseko za chipata cha mzinda ndi maferemu ake awiri, ndipo anazizula zonse pamodzi ndi mpiringidzo womwe. Anazisenza pa mapewa pake napita nazo pamwamba pa phiri loyangʼanana ndi Hebroni.
Forsothe Sampson slepte til to `the myddis of the nyyt; and `fro thennus he roos, and took bothe the closyngis, ethir leeues, of the yate, with hise postis and lok; and he bar tho leeues, put on the schuldris, to the cop of the hil that biholdith Ebron.
4 Pambuyo pake, Samsoni anayamba kukonda mtsikana wina wa ku chigwa cha Soreki dzina lake Delila.
After these thingis Sampson louyde a womman that dwellide in the valey of Soreth, and sche was clepid Dalida.
5 Olamulira Afilisti anapita kwa mkaziyo ndipo anati, “Umunyengerere Samsoni kuti udziwe chinsinsi cha mphamvu zake zoopsazi, komanso ndi mmene ife tingamupambanire kuti timumange ndi kumugonjetsa. Ukatero aliyense wa ife adzakupatsa ndalama zasiliva 1,100.”
And the princes of Filisteis camen to hir, and seiden, Disseyue thou hym, and lerne thou of hym, in what thing he hath so greet strengthe, and how we mowen ouercome hym, and turmente hym boundun; that if thou doist, we schulen yyue to thee ech man a thousynde and an hundrid platis of siluer.
6 Choncho Delila anati kwa Samsoni, “Inu tandiwuzani pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi ndi mmene anthu akhoza kukumangirani kuti akugonjetseni.”
Therfor Dalida spak to Sampson, Y biseche, seie thou to me, wher ynne is thi gretteste strengthe, and what is that thing, with which thou boundun maist not breke?
7 Samsoni anamuyankha kuti, “Ngati wina atandimanga ndi zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndidzafowoka ndi kusanduka ngati munthu wina aliyense.”
To whom Sampson answeride, If Y be boundun with seuene coordis of senewis not yit drye `and yit moiste, Y schal be feble as othere men.
8 Tsono atsogoleri a Afilisti aja anapita kwa mkazi uja namupatsa zingwe zisanu ndi ziwiri zatsopano zosawuma, ndipo mkaziyo anamanga nazo Samsoni.
And the princis of Filisteis brouyten `to hir seuene coordis, as he hadde seide; with whiche sche boond him,
9 Nthawi imeneyo nʼkuti mkazi uja atayika anthu omubisalira mʼchipinda. Tsono anati kwa mwamuna wake, “Amuna anga, Afilisti aja afika!” Koma iye anangodula zingwe zija ngati mmene imadukira nkhosi ya chingwe ikamapsa. Choncho chinsinsi cha mphamvu zake sichinadziwike.
while buyschementis weren hid at hir, and abididen in a closet the ende of the thing. And sche criede to hym, Sampson, Filisteis ben on thee! Which brak the boondis, as if a man brekith a threed of herdis, writhun with spotle, whanne it hath take the odour of fier; and it was not knowun wher ynne his strengthe was.
10 Kenaka Delila anati kwa Samsoni, “Inu mwandipusitsa ndi kundiwuza zabodza. Chonde tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.”
And Dalida seide to hym, Lo! thou hast scorned me, and thou hast spok fals; nameli now schewe thou to me, with what thing thou schuldist be boundun.
11 Iye anati, “Ngati aliyense atandimanga ine ndi zingwe zatsopano zimene sanazigwiritseko ntchito, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala monga munthu wina aliyense.”
To whom he answeride, If Y be boundun with newe coordis, that weren not yit in werk, I schal be feble, and lijk othere men.
12 Choncho Delila anatenga zingwe zatsopano namumanga nazo. Kenaka anati “Amuna anga, Afilisti aja afikanso!” Nthawi iyi nʼkuti anthu omubisalira aja ali mʼchipinda chamʼkati. Koma iye anadulanso zingwe mʼmanja ake ngati akudula ulusi wa thonje.
With whiche Dalida boond him eft, and criede, Sampson, Filistees ben on thee! the while buyschementis weren maad redi in closet. Which brak `so the boondis as thredis of webbis.
13 Ndipo Delila anati kwa Samsoni, “Mpaka tsopano mwakhala mukundipusitsa ndi kumandiwuza zabodza. Chonde, tandiwuzani mmene munthu angakumangireni.” Iye anayankha kuti, “Ngati njombi zisanu ndi ziwiri za kumutu kwanga utazilukira mu cholukira nsalu ndi kuchimanga molimbika ndi chikhomo, ndidzasanduka wofowoka ndi kukhala wofanana ndi munthu wina aliyense.”
And Dalida seide eft to hym, Hou long schalt thou disseyue me, and schalt speke fals? Schew thou to me, with what thing thou schalt be boundun. To whom Sampson answeryde, he seide, If thou plattist seuene heeris of myn heed with a strong boond, and fastnest to the erthe a naile boundun a boute with these, Y schal be feble.
14 Choncho iye akugona, Delila analukira njombi za ku mutu kwa Samsoni mu cholukira nsalu nachimanga molimba ndi chikhomo. Pambuyo pake anati kwa Samsoni, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Tsono iye anadzuka ku tulo, nazula chikhomo chija ndipo njombi zinachoka mu cholukira chija.
And whanne Dalida hadde do this, sche seide to hym, Sampson, Filisteis ben on thee! And he roos fro sleep, and drow out the nail, with the heeris and strong boond.
15 Tsono mkaziyo ananenanso kwa iye kuti, “Munganene bwanji kuti mumandikonda pamene mtima wanu suli pa ine? Aka ndi kachitatu mukundipusitsa ndipo simunandiwuze pamene pagona mphamvu zanu zoopsazi.”
And Dalida seide to hym, Hou seist thou, that thou louest me, sithen thi soule is not with me? Bi thre tymes thou liedist to me, and noldist seie to me, wher ynne is thi moost strengthe.
16 Tsono popeza anamupanikiza ndi mawu ake tsiku ndi tsiku ndi kumukakamiza, mtima wa Samsoni unatopa pafupi kufa.
And whanne sche was diseseful to hym, and cleuyde to hym contynueli bi many daies, and yaf not space to reste, his lijf failide, and was maad wery `til to deeth.
17 Choncho anamuwuza mkaziyo zonse za mu mtima mwake nati “Lumo silinapitepo pa mutu wanga chifukwa ndakhala ndili Mnaziri wopatulikira Mulungu chibadwire. Ngati nditametedwa mphamvu zanga zidzandichokera, ndidzasanduka wofowoka ndipo ndidzafanana ndi munthu wina aliyense.”
Thanne he openyde the treuthe of the thing, and seide to hir, Yrun stiede neuere on myn heed, for Y am a Nazarei, that is, halewid to the Lord, fro `the wombe of my modir; if myn heed be schauun, my strengthe schal go awei fro me, and Y schal faile, and Y schal be as othere men.
18 Delila ataona kuti wamuwuza zonse za mu mtima mwake anatumiza uthenga kukayitana akuluakulu a Afilisti nati, “Bweraninso kamodzi kano kokha popeza wandiwululira zonse za mu mtima mwake.” Choncho akuluakulu a Afilisti aja anabwera ndi ndalama za siliva mʼmanja mwawo.
And sche siy that he knowlechide to hir al his wille, `ether herte; and sche sente to the princes of Filisteis, and comaundide, Stie ye yit onys, for now he openyde his herte to me. Whiche stieden, with the money takun which thei bihiyten.
19 Mkazi uja anagoneka Samsoni pa miyendo yake. Kenaka anayitana munthu wina ndipo anadzameta Samsoni njombi zisanu ndi ziwiri zija kumutu kwake. Pamenepo anayamba kufowoka, ndipo mphamvu zake zinamuchokera.
And sche made hym slepe on hir knees, and `bowe the heed in hir bosum; and sche clepide a barbour, and schauede seuene heeris of hym; and sche bigan to caste hym awei, and to put fro hir; for anoon the strengthe yede awei fro him.
20 Pambuyo pake mkaziyo anamuyitana kuti, “Amuna anga, Afilisti aja abwera!” Iye anadzuka kutuloko, naganiza kuti, “Ndituluka monga ndimachitira nthawi zonse ndi kudzimasula.” Koma sanadziwe kuti Yehova wamuchokera.
And sche seide, Sampson, Filisteis ben on thee! And he roos fro sleep, and seide to his soule, Y schal go out, as and Y dide bifore, and Y schal schake me fro boondis; and he wiste not, that the Lord hadde goon awei fro hym.
21 Afilisti anamugwira ndipo anamukolowola maso. Kenaka anapita naye ku Gaza atamumanga ndi maunyolo achitsulo. Kumeneko anakhala wa pamphero mu ndende.
And whanne Filisteis hadden take hym, anoon thei diden out hise iyen, and ledden hym boundun with chaynes to Gaza, and `maden hym closid in prisoun to grynde.
22 Pambuyo pake tsitsi la pa mutu wake, monga linametedwa, linayambanso kumera.
And now hise heeris bigunnen to growe ayen;
23 Tsono atsogoleri a Afilisti anasonkhana kuti adzapereke nsembe yayikulu kwa Dagoni mulungu wawo ndi kukondwerera popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka Samsoni mdani wathu mʼmanja mwathu.”
and the princes of Filisteis camen togidere to offre grete sacrifices to Dagon, her god, and `to ete, seiynge, Oure god hath bitake oure enemy Sampson in to oure hondis.
24 Anthuwo atamuona Samsoni, anayamba kutamanda mulungu wawo popeza ankanena kuti, “Mulungu wathu wapereka mdani wathu mʼmanja mwathu, ndiye amene anawononga dziko lathu, napha anthu athu ambirimbiri.”
And the puple seynge also this thing preiside her god, and seide the same thingis, Our god hath bitake oure aduersarie in to oure hondis, which dide awey oure lond, and killide ful many men.
25 Ali mʼkati mosangalala, anthu aja amafuwula kuti, “Mutulutseni Samsoniyo kuti adzatisangalatse.” Choncho anamutulutsadi Samsoni mʼndende, ndipo anawasangalatsadi. Ndipo anamuyimiritsa pakati pa mizati.
And thei weren glad bi feestis, for thei hadden ete thanne; and thei comaundiden, that Sampson schulde be clepid, and schulde pleie bifor hem; which was led out of prisoun, and pleiede bifor hem; and thei maden hym stonde bitwixe twei pileris.
26 Pambuyo pake Samsoni anawuza mnyamata amene anamugwira dzanja kuti, “Ndilole kuti ndikhudze mizati imene yachirikiza nyumba yonseyi kuti ndiyitsamire.”
And he seide to the `child gouernynge hise steppis, Suffre thou me, that Y touche the pilers on whiche al the hows stondith, that Y be bowid on tho, and reste a litil.
27 Nthawi imeneyi nʼkuti nyumbayo ili yodzaza ndi anthu aamuna ndi aakazi. Olamulira onse a Afilisti anali momwemo, ndipo pamwamba pa nyumbayo panali anthu 3,000 aamuna ndi aakazi amene amaonerera Samsoni akusewera.
Sotheli the hows was ful of men and of wymmen, and the princes of the Filisteis weren there, and aboute thre thousynde of `euer either kynde, biholdynge fro the roof and the soler Sampson pleynge.
28 Tsono Samsoni anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova Ambuye anga, ndikumbukireni. Chonde ndilimbitseni nthawi yokha ino, inu Yehova, kuti ndiwabwezere Afilistiwa chifukwa cha maso anga awiri.”
And whanne the Lord `was inwardli clepid, he seide, My Lord God, haue mynde on me, and, my God, yelde thou now to me the formere strengthe, that Y venge me of myn enemyes, and that Y resseyue o veniaunce for the los of tweyne iyen.
29 Choncho Samsoni anagwira mizati iwiri yapakati imene inkachirikiza nyumbayo. Anayitsamira ndi mphamvu zake zonse, dzanja lake lamanja ku mzati wina ndi dzanja lamanzere ku mzati winanso,
And he took bothe pilers, on whiche the hows stood, and he helde the oon of tho in the riythond, and the tother in the left hond; and seide,
30 ndipo Samsoni anati, “Ndife nawo pamodzi!” Nthawi yomweyo anakankha ndi mphamvu zake zonse ndipo mizati inagwera atsogoleri a Afilisti ndi anthu onse anali mʼmenemo. Tsono chiwerengero cha anthu amene Samsoni anapha pa nthawi ya imfa yake chinaposa cha iwo amene anawapha akanali ndi moyo.
My lijf die with Filesteis! And whanne the pileris weren schakun togidere strongli, the hows felde on alle the princes, and on the tother multitude, that was there; and he diynge killide many moo, than he quyk hadde slayn bifore.
31 Kenaka abale ake ndi onse a pa banja la abambo ake anapita kukamutenga. Ndipo anakamuyika pakati pa Zora ndi Esitaoli mʼmanda a abambo ake, Manowa. Iye anatsogolera Israeli kwa zaka makumi awiri.
Forsothe hise britheren and al the kinrede camen doun, and token his bodi, and birieden bitwixe Saraa and Escahol, in the sepulcre of his fadir Manue; and he demyde Israel twenti yeer.

< Oweruza 16 >