< Oweruza 15 >

1 Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
After some days, during the time of wheat harvest, Samson took a young goat and went to visit his wife. He said to himself, “I will go to my wife's room.” But her father would not allow him to go in.
2 Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
Her father said, “I really thought you hated her, so I gave her to your friend. Her younger sister is more beautiful than she is, is she not? Take her instead.”
3 Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
Samson said to them, “This time I will be innocent in regard to the Philistines when I hurt them.”
4 Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
Samson went and caught three hundred foxes and he tied together each pair, tail to tail. Then he took torches and tied them in the middle of each pair of tails.
5 Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
When he had set the torches on fire, he let the foxes go into the standing grain of the Philistines, and they set fire to both the stacked grain and the grain standing in the field, along with the vineyards and the olive orchards.
6 Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
The Philistines asked, “Who did this?” They were told, “Samson, the Timnite's son-in-law, did this because the Timnite took Samson's wife and gave her to his friend.” Then the Philistines went and burned up her and her father.
7 Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
Samson said to them, “If this is what you do, I will get my revenge against you, and after that is done, I will stop.”
8 Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
Then he cut them to pieces, hip and thigh, with a great slaughter. Then he went down and lived in a cave in the cliff of Etam.
9 Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
Then the Philistines came up and they prepared for battle in Judah and set up their army in Lehi.
10 Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
The men of Judah said, “Why have you come up to attack us?” They said, “We are attacking so we may capture Samson, and do to him as he has done to us.”
11 Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
Then three thousand men of Judah went down to the cave in the cliff of Etam, and they said to Samson, “Do you not know that the Philistines are rulers over us? What is this you have done to us?” Samson said to them, “They did to me, and so I have done to them.”
12 Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
They said to Samson, “We have come down to tie you up and give you into the hands of the Philistines.” Samson said to them, “Swear to me that you will not kill me yourselves.”
13 Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
They said to him, “No, we will only tie you with ropes and hand you over to them. We promise we will not kill you.” Then they tied him up with two new ropes and brought him up from the rock.
14 Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
When he came to Lehi, the Philistines came shouting as they met him. Then Yahweh's Spirit came on him with power. The ropes on his arms became like burnt flax, and they fell off his hands.
15 Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
Samson found a fresh jawbone of a donkey, and he picked it up and killed a thousand men with it.
16 Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
Samson said, “With the jawbone of a donkey, heaps upon heaps, with the jawbone of a donkey I have killed a thousand men.”
17 Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
When Samson finished speaking, he threw away the jawbone, and he called the place Ramath Lehi.
18 Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
Samson was very thirsty and called on Yahweh and said, “You have given this great victory to your servant. But now will I die of thirst and fall into the hands of those who are uncircumcised?”
19 Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
God split open the hollow place that is at Lehi and water came out. When he drank, his strength returned and he revived. So he called the name of that place En Hakkore, and it is at Lehi to this day.
20 Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.
Samson judged Israel in the days of the Philistines for twenty years.

< Oweruza 15 >