< Oweruza 15 >

1 Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
And it was from days in [the] days of [the] harvest of wheat and he visited Samson wife his with a kid of goats and he said let me go into wife my the chamber towards and not he permitted him father her to go.
2 Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
And he said father her certainly I thought that certainly you hated her and I gave her to companion your ¿ not [is] sister her young good more than her let her belong please to you in place of her.
3 Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
And he said to them Samson I will be free this time from [the] Philistines for [am] about to do I with them harm.
4 Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
And he went Samson and he captured three hundred foxes and he took torches and he turned tail to tail and he put a torch one between [the] two the tails in the middle.
5 Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
And he kindled fire on the torches and he sent [them] among [the] standing grain of [the] Philistines and it burned up from [the] heap of sheaves and unto [the] standing grain and unto [the] vineyard of olive tree[s].
6 Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
And they said [the] Philistines who? did he do this [thing] and they said Samson [the] son-in-law of the Timnite for he has taken wife his and he has given her to companion his and they went up [the] Philistines and they burned her and father her with fire.
7 Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
And he said to them Samson if you will do! like this that except I have avenged myself on you and after I will cease.
8 Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
And he struck them leg with thigh a defeat great and he went down and he dwelt in [the] cleft of [the] rock of Etam.
9 Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
And they went up [the] Philistines and they encamped in Judah and they were spread out at Lehi.
10 Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
And they said [the] man of Judah why? have you come up on us and they said to bind Samson we have come up to do to him just as he did to us.
11 Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
And they went down three thousand man from Judah to [the] cleft of [the] rock of Etam and they said to Samson ¿ not do you know that [are] ruling over us [the] Philistines and what? this have you done to us and he said to them just as they did to me so I have done to them.
12 Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
And they said to him to bind you we have come down to give you in [the] hand of [the] Philistines and he said to them Samson swear to me lest you should fall! on me you.
13 Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
And they said to him saying In-deed certainly we will bind you and we will give you in hand their and certainly not we will kill you and they bound him with two ropes new and they brought up him from the rock.
14 Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
He [was] coming to Lehi (and [the] Philistines *L(abh)*) they shouted to meet him and it rushed on him [the] spirit of Yahweh and they became the ropes which [were] on arms his like flax which people have burned with fire and they dropped off bonds his from on hands his.
15 Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
And he found a jawbone of a donkey fresh and he stretched out hand his and he took it and he struck down with it a thousand man.
16 Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
And he said Samson with [the] jawbone of the donkey a heap two heaps with [the] jawbone of the donkey I struck down a thousand man.
17 Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
And it was when finished he to speak and he threw the jawbone from hand his and he called the place that Ramath Lehi.
18 Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
And he was thirsty very and he called out to Yahweh and he said you you have given by [the] hand of servant your the victory great this and now [must] I die with thirst and I fall in [the] hand of the uncircumcised [men]?
19 Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
And he split open God the deep hollow which [is] at Lehi and they came out from it waters and he drank and it returned spirit his and he lived there-fore - he called name its En Hakkore which [is] at Lehi until the day this.
20 Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.
And he judged Israel in [the] days of [the] Philistines twenty year[s].

< Oweruza 15 >